14 Anamudyetsanso mafuta a mkaka wa ng’ombe ndi mkaka wa nkhosa,+
Pamodzi ndi mafuta a nkhosa.
Anamudyetsa nkhosa zamphongo za ku Basana, mbuzi zamphongo,+
Pamodzi ndi tirigu wabwino koposa ngati mafuta okuta impso.+
Ndipo anali kumwa magazi a mphesa monga vinyo.+