24 Zitatero, mfumu inalamula kuti abweretse amuna amphamvu amene ananenera Danieli zoipa aja,+ ndipo anawabweretsadi. Kenako anawaponya m’dzenje la mikango+ pamodzi ndi ana awo ndi akazi awo.+ Iwo asanafike n’komwe pansi pa dzenjelo, mikango inawakhadzulakhadzula ndi kuphwanya mafupa awo onse.+