Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • “Uzikwaniritsa Zinthu Zimene Walonjeza”
    Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2017 | April
    • 7. (a) Kodi Hana analonjeza Yehova chiyani, nanga zotsatira zake zinali zotani? (b) Kodi Samueli ankayenera kudzakhala wotani mogwirizana ndi lonjezo la Hana? (Onani mawu a m’munsi.)

      7 Nayenso Hana anakwaniritsa zimene analonjeza kwa Yehova. Iye ananena lonjezo lake pamene anali wokhumudwa kwambiri chifukwa cha vuto lake la kusabereka komanso chipongwe chimene mkazi mnzake ankamuchitira. (1 Sam. 1:4-7, 10, 16) Iye anauza Yehova zakukhosi kwake komanso anamulonjeza kuti: “Inu Yehova wa makamu, mukaona nsautso yanga, ine kapolo wanu wamkazi, ndi kundikumbukira, ndiponso ngati simudzaiwala kapolo wanu wamkazi ndi kum’patsa mwana wamwamuna, ndidzam’pereka kwa Yehova masiku onse a moyo wake, ndipo lezala silidzadutsa m’mutu mwake.”a (1 Sam. 1:11) Yehova anayankha pemphero la Hanali ndipo anamupatsadi​ mwana wamwamuna. Hana ayenera kuti anasangalala kwambiri. Komabe iye sanaiwale lonjezo lake komanso sanaiwale kuti Yehova ndi amene anamuthandiza kuti abereke mwanayu. Moti mwanayu atangobadwa iye anati: “Ndinam’pempha kwa Yehova.”​—1 Sam. 1:20.

  • “Uzikwaniritsa Zinthu Zimene Walonjeza”
    Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2017 | April
    • a Zimene Hana analonjezazi zinkatanthauza kuti mwana wakeyo adzakhala Mnaziri kwa moyo wake wonse. Zinkatanthauzanso kuti mwanayo adzakhala wosiyana ndi ana ena, adzaperekedwa kwa Yehova ndipo azidzachita utumiki wopatulika.​—Num. 6:2, 5, 8.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena