-
Anaphunzira pa Zolakwa ZakeTsanzirani Chikhulupiriro Chawo
-
-
18, 19. (a) Kodi n’chiyani chinachitikira Yona atafika pansi pa nyanja, nanga anamezedwa ndi chiyani? (b) Kodi ndani anapangitsa zimenezi? (Onaninso mawu a m’munsi.)
18 Koma mwadzidzidzi anangoona chinthu chinachake chachikulu, chabii chikubwera poteropo. Kenako chinam’thamangira kukamwa kwake kuli yasaa. Chinthuchi chinali chinsomba ndipo Yona anangozindikira kuti cham’meza.
“Yehova anatumiza chinsomba chachikulu kuti chikameze Yona”
19 Apa anaganiza kuti afa basi. Komabe Yona anadabwa kuti adakali moyo. Chinsomba chomwe chinamumezachi, sichinam’tafune ndipo atafika m’mimba mwa nsombayo sanagayidwe. Iye ankathanso kupuma bwinobwino ngakhale kuti amenewa anayenera kukhala manda ake. Patapita nthawi, Yona anayamba kuchita mantha kwambiri. N’zosakayikitsa kuti Mulungu wake,Yehova, ndi amene ‘anatumiza chinsomba chachikuluchi kuti chim’meze.’c—Yona 1:17.
20. Kodi tingaphunzire chiyani pa pemphero la Yona ali m’mimba mwa chinsomba?
20 Yona anakhala m’mimba mwa chinsombacho kwa maola ambiri. M’mimba mwa chinsombacho munali chimdima chandiweyani. Iye anayamba kusinkhasinkha ndiponso kupemphera kwa Yehova Mulungu. Pemphero lake, lomwe lili m’chaputala chachiwiri cha buku la Yona, limatithandiza kum’dziwa bwino. Limasonyeza kuti Yona ankadziwa bwino Malemba chifukwa anatchula mfundo zambiri za m’buku la Masalimo. Limasonyezanso kuti iye anali ndi mtima woyamikira. Yona ananena kuti: “Koma ine, ndidzakutamandani ndi kupereka nsembe kwa inu. Zimene ndalonjeza ndidzazikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”—Yona 2:9.
21. Kodi Yona anaphunzira chiyani pa nkhani ya chipulumutso, nanga ifeyo tikuphunzirapo chiyani?
21 Yona anaphunzira kuti Yehova angathe kupulumutsa munthu aliyense, kulikonse ndiponso nthawi ina iliyonse. Ngakhale kuti mtumiki wakeyu anali “m’mimba mwa nsomba,” Yehova anam’pulumutsa. (Yona 1:17) Yehova yekha ndi amene akanatha kuchititsa kuti munthu akhalebe ndi moyo m’mimba mwa nsomba kwa masiku atatu, usana ndi usiku. Masiku ano ndi bwino kuti tizikumbukira zoti Yehova ndi ‘amene amasunga mpweya wathu.’ (Dan. 5:23) Izi zikusonyeza kuti Yehova ndi amene amatisamalira kuti tikhalebe ndi moyo. Kodi timayamikira zimenezi? Ndiyetu tizimumvera nthawi zonse.
22, 23. (a) Kodi Yona anasonyeza bwanji kuti anali woyamikira? (b) Kodi tingatsanzire bwanji Yona ngati titalakwitsa zinthu?
22 Kodi Yona anayamba kumvera Yehova posonyeza kuyamikira kwake? Inde. Patatha masiku atatu, chinsomba chija chinapita m’mphepete mwa nyanja ndipo “chinalavula Yona kumtunda.” (Yona 2:10) Tangoganizirani, Yona sanafunike kusambira kuti akafike kumtunda. Komabe, atafika kumtundako anafunika kudziwa kolowera. Pasanapite nthawi, Yona anakumananso ndi mayesero ena amene akanaonetsa ngati iye ankayamikira Yehova chifukwa cha zimene anamuchitira. Lemba la Yona 3:1, 2, limati: “Yehova analankhula ndi Yona kachiwiri kuti: ‘Nyamuka, upite kumzinda waukulu wa Nineve, ndipo kumeneko ukalalikire zimene ndikuuze.’” Kodi Yona anatani?
-
-
Anaphunzira pa Zolakwa ZakeTsanzirani Chikhulupiriro Chawo
-
-
c Mawu achiheberi amene anawamasulira kuti “nsomba,” m’Chigiriki anawamasulira kuti “chilombo cha m’nyanja,” kapena kuti “chinsomba chachikulu.” Ngakhale kuti sitikudziwa kuti imeneyi inali nsomba yanji, komabe tikudziwa kuti m’nyanja ya Mediterranean muli nsomba zikuluzikulu zamtundu wa shaki zimene zingathe kumeza munthu wathunthu. M’nyanja zina nsomba zimenezi zimatha kukula kwambiri moti zina zimakhala zazitali mamita 15, kapenanso kuposa.
-