-
“Kuyenera Kuti Izi Zioneke”Nsanja ya Olonda—1999 | May 1
-
-
Anthu Okhalako Panthaŵiyo Anali Kudzaona Chisautsocho
11. Kodi Yesu anati bwanji ponena za “mbadwo uwu”?
11 Ayuda ambiri anali kuganiza kuti kulambira kwawo, kochitikira pa kachisi, sikudzatha. Koma Yesu anati: ‘Phunzirani ndi mkuyu . . . ; pamene tsopano nthambi yake ili yanthete, niphuka masamba ake, muzindikira kuti dzinja liyandikira; chomwechonso inu, pamene mudzaona zimenezo, zindikirani kuti iye ali pafupi, inde pakhomo. Indetu ndinena kwa inu, mbadwo uwu sudzatha kuchoka, kufikira zinthu zonsezi zidzachitidwa. Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mawu anga sadzachoka ayi.’—Mateyu 24:32-35.
12, 13. Kodi ophunzira ayenera kuti anawamva motani mawu a Yesu akuti “mbadwo uno”?
12 M’zaka zoyambirira chisanafike chaka cha 66 C.E., Akristu anaona mbali zambiri zoyambirira za chizindikiro chachiungwe zikukwaniritsidwa—nkhondo, njala, ngakhale kulalikidwa kwa uthenga wabwino wa Ufumu ponseponse. (Machitidwe 11:28; Akolose 1:23) Komano kodi mapeto anali kudzafika liti? Kodi Yesu anatanthauzanji pamene ananena kuti: “Mbadwo uwu [Chigiriki, ge·ne·aʹ] sudzatha kuchoka”? Nthaŵi zambiri Yesu anatcha makamu a Ayuda om’tsutsa, kuphatikizapo atsogoleri achipembedzo kuti ‘obadwa oipa, achigololo.’ (Mateyu 11:16; 12:39, 45; 16:4; 17:17; 23:36) Choncho, atanenanso za “mbadwo uwu” pa Phiri la Azitona, mwachionekere sanali kutanthauza fuko lonse la Ayuda m’mbiri yonse ya anthu; sanalinso kutanthauza otsatira ake, ngakhale kuti anali “mbadwa yosankhika.” (1 Petro 2:9) Komanso Yesu sanali kutanthauza kuti “mbadwo uwu” ndi nyengo inayake.
13 M’malo mwake, Yesu anali kunena za Ayuda otsutsa a panthaŵiyo amene anali kudzaona kukwaniritsidwa kwa chizindikiro chimene anapereka. Ponena za mawuwo “mbadwo uno” opezeka pa Luka 21:32, Polofesa Joel B. Green anati: “Mu Uthenga Wabwino Wachitatu, ‘mbadwo uno’ (ndi mawu ena ofanana nawo) nthaŵi zonse amatanthauza gulu la anthu amene akutsutsana ndi cholinga cha Mulungu. . . . [Amatanthauza] anthu amene akufulatira zolinga za Mulungu mouma khosi.”b
14. Kodi “mbadwo” umenewo unaona zotani, koma kodi Akristu anakhala motani ndi chotsatirapo chosiyana?
14 Mbadwo woipawo wa Ayuda otsutsa amene anali kuona chizindikiro chikukwaniritsidwa anali kudzaonanso chimaliziro. (Mateyu 24:6, 13, 14) Ndipo anachionadi! Mu 70 C.E., gulu lankhondo la Aroma linabweranso, lotsogozedwa ndi Titus, mwana wa Mfumu Vespasian. Kuzunzika kwa Ayuda amene anatsekeredwanso m’mzindawo n’kosaneneka.c Flavius Josephus, mboni yoona ndi maso, anasimba kuti podzafika nthaŵi imene Aroma amasakaza mzindawo, Ayuda pafupifupi 1,100,000 anali atamwalira ndipo enanso 100,000 anali atatengedwa ukapolo, ndipo ambiri a iwo anafa momvetsa chisoni ndi njala kapena anaphedwa m’mabwalo a maseŵero ku Roma. Ndithudi, chisautso cha mu 66-70 C.E. ndicho chinali chachikulu kwambiri chimene Yerusalemu ndi dongosolo lachiyuda linali lisanaonepo kapena linali kudzaonanso. Komatu zinali zosiyana kotheratu kwa Akristu amene anamvera ulosi wochenjeza wa Yesu natuluka m’Yerusalemu pambuyo poti magulu ankhondo a Aroma achoka mu 66 C.E.! Akristu “osankhidwawo” odzozedwa ‘anapulumuka,’ kapena anasungidwa amoyo, mu 70 C.E.—Mateyu 24:16, 22.
-
-
“Kuyenera Kuti Izi Zioneke”Nsanja ya Olonda—1999 | May 1
-
-
b Katswiri wamaphunziro wa ku Britain G. R. Beasley-Murray anati: “Omasulira sayenera kuvutika ndi mawu akuti ‘mbadwo uno.’ Pamenedi n’zoona kuti mawu akuti genea m’Chigiriki chakale anali kutanthauza kubadwa, mbadwa, chonchonso fuko, . . . mu [Septuagint yachigiriki] nthaŵi zambiri anagwiritsidwa ntchito potembenuza mawu achihebri akuti dôr, otanthauza nyengo, mbadwo wa anthu, kapena mbadwo kutanthauza anthu okhalako panthaŵiyo. . . . M’mawu onenedwa ndi Yesu mawuwo akuoneka kuti akutanthauza zinthu ziŵiri: choyamba nthaŵi zonse amatanthauza anthu amene analiko panthaŵiyo, ndipo chachiŵiri, nthaŵi zonse amasonyeza bwino lomwe kuti pali chidzudzulo.”
-