Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Yesu Amasonyeza Bwanji Chilungamo cha Mulungu?
    Nsanja ya Olonda—2010 | August 15
    • 7. Kodi Yesu anali ndi chiyani chomwe chinali chamtengo wapatali?

      7 Yesu anasonyeza kuti ankakonda kwambiri zinthu zauzimu, chifukwa nthawi zonse ankapita ku misonkhano yolambira Mulungu. Popeza anali ndi maganizo angwiro, iye anamvetsa bwino chilichonse chimene anamva ndiponso kuwerenga m’Malemba Achiheberi. (Luka 4:16) Iye analinso ndi chinthu china cha mtengo wapatali. Anali ndi thupi langwiro limene akanatha kulipereka nsembe m’malo mwa anthu onse. Pa ubatizo wake, Yesu ankapemphera ndipo n’kutheka kuti ankaganizira mawu aulosi a pa Salmo 40:6-8.​—Luka 3:21; werengani Aheberi 10:5-10.a

  • Kodi Yesu Amasonyeza Bwanji Chilungamo cha Mulungu?
    Nsanja ya Olonda—2010 | August 15
    • a Pa lemba la Aheberi 10:5-10, mtumwi Paulo anagwira mawu Salmo 40:6-8 kuchokera m’Baibulo la Greek Septuagint limene lili ndi mawu akuti, “munandikonzera thupi.” Mawu amenewa sapezeka m’mipukutu yakale yomasulira Malemba Achiheberi.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena