Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 | Musamabwezere
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2022 | Na. 1
    • Baibulo Limati:

      “Musabwezere choipa pa choipa. . . . Ngati ndi kotheka, khalani mwamtendere ndi anthu onse, monga mmene mungathere. Musabwezere, . . . pakuti Malemba amati: ‘“Kubwezera ndi kwanga, ndidzawabwezera ndine, watero Yehova.’”​—AROMA 12:17-19.

      Zimene Lembali Limatanthauza:

      Ngakhale kuti mwachibadwa anthufe timakwiya munthu wina akatilakwira, Mulungu safuna kuti tizibwezera. M’malomwake, iye amafuna kuti tizimuyembekezera moleza mtima chifukwa posachedwapa adzathetsa zinthu zonse zopanda chilungamo.​—Salimo 37:7, 10.

  • 2 | Musamabwezere
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2022 | Na. 1
    • Adrián anayamba kuphunzira Baibulo ali ndi zaka 16. Iye ananena kuti: “Ndinapitiriza kuphunzira Baibulo ndipo ndinayamba kuona kuti ndikufunika kusintha khalidwe langa.” Iye ankafunikira kuthetsa chidani mumtima mwake komanso kusiya kuchita zachiwawa. Lemba limene linamuthandiza kwambiri ndi la Aroma 12:17-19 lomwe limatilimbikitsa kuti tisamabwezere. Adrián akufotokoza kuti: “Zimenezi zinandithandiza kuzindikira kuti Yehova adzathetsa zinthu zopanda chilungamo pa nthawi yake ndiponso m’njira yabwino. Patapita nthawi ndinasiya kukonda ndewu.”

      Tsiku lina madzulo gulu la achinyamata lomwe linkakonda kumenyana ndi gulu la Adrián linayamba kumumenya. Mtsogoleri wawo ananena kuti: “Bwanji sukubwezera?” Adrián akunena kuti: “Ndinkafunitsitsa kubwezera.” Koma m’malo mobwezera iye anapemphera kwa Yehova mwachidule n’kuchokapo.

      Adrián akufotokozanso kuti: “Tsiku lotsatira ndinakumana ndi mtsogoleri wawo uja ali yekha. Nditamuona ndinkafuna kuti ndibwezere zimene anandichita koma ndinapempheranso chamumtima kuti Yehova andithandize kuugwira mtima. Koma ndinadabwa kuona kuti anabwera pafupi n’kundiuza kuti: ‘Undikhululukire chifukwa cha zimene zinachitika dzulo zija. Inenso ndikufuna nditakhala ngati iweyo. Ndikufuna kuphunzira Baibulo.’ Ndinasangalala kwambiri kuti ndinakwanitsa kuugwira mtima chifukwa zinathandiza kuti nayenso ayambe kuphunzira Baibulo.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena