-
“Mulungu Ndi Amene Anayamba Kutikonda”Yandikirani Yehova
-
-
“Mulungu Ndi Chikondi”
15. Kodi Baibulo limanena chiyani zokhudza chikondi cha Yehova zomwe silinena likamafotokoza za makhalidwe ake ena akuluakulu? (Onaninso mawu am’munsi.)
15 Baibulo limatiuza mfundo ina yokhudza chikondi, koma silitchula mfundoyi ponena za makhalidwe ena akuluakulu a Yehova. Malemba sanena kuti Mulungu ndi mphamvu, Mulungu ndi chilungamo kapenanso kuti Mulungu ndi nzeru. Iye ali ndi makhalidwe amenewo, makhalidwewa amachokera kwa iye ndipo palibe amene amasonyeza kwambiri makhalidwe atatuwa kuposa iyeyo. Koma Baibulo limanena chinthu china chokhudza chikondi, lomwe ndi khalidwe lake la nambala 4. Limati: “Mulungu ndi chikondi.”b (1 Yohane 4:8) Kodi zimenezi zikutanthauza chiyani?
16-18. (a) N’chifukwa chiyani Baibulo limanena kuti “Mulungu ndi chikondi”? (b) Pa zolengedwa zonse zapadzikoli, n’chifukwa chiyani m’pake kuti munthu ndi amene amaimira chikondi cha Yehova?
16 Kunena kuti “Mulungu ndi chikondi” n’kosiyana ndi kungonena kuti chinthu ichi n’chofanana ndi ichi. Mwachitsanzo, sitinganene kuti “Mulungu ndi wofanana ndi chikondi.” Komanso kungakhale kulakwitsa kutembenuza mawuwa n’kunena kuti “chikondi ndi Mulungu.” Yehova ndi weniweni osati khalidwe basi. Iye ndi Mulungu amene amaganiza, amasangalala kapena kukhumudwa komanso ali ndi makhalidwe ena kuwonjezera pa chikondi. Komabe khalidwe lake lalikulu ndi chikondi. Choncho buku lina ponena za vesili limati: “Mulungu ndi wachikondi pa chilichonse.” Kuti timvetse bwino zimenezi, taganizirani izi: Mphamvu za Yehova zimamuthandiza kuti akwanitse kuchita zinthu. Chilungamo ndi nzeru zake zimamuthandiza kudziwa njira imene angachitire zinthuzo. Koma chikondi ndi chimene chimamupangitsa kuti achite zinthuzo. Ndipo nthawi zonse akamasonyeza makhalidwe enawo, amasonyezanso chikondi.
17 Nthawi zambiri timanena kuti Yehova ndi chitsanzo chabwino kwambiri pa nkhani yosonyeza chikondi. Choncho ngati tikufuna kuphunzira chikondi chimene munthu amasonyeza chifukwa chotsatira mfundo za m’Baibulo, tiyenera kuphunzira za Yehova. Koma anthu nawonso amatha kusonyeza khalidwe labwinoli. N’chifukwa chiyani zili choncho? Pa nthawi imene ankalenga zinthu, Yehova analankhula mawu awa ndipo ayenera kuti ankauza Mwana wake: “Tiyeni tipange munthu m’chifaniziro chathu, kuti akhale wofanana nafe.” (Genesis 1:26) Pa zolengedwa zonse zapadzikoli, ndi anthu okha amene angasankhe kuti azikonda ena ndipo akamachita zimenezi amakhala kuti akutsanzira Atate awo akumwamba. Kumbukirani kuti Yehova anasankha zolengedwa zosiyanasiyana kuti ziziimira makhalidwe ake akuluakulu. Koma iye anasankha munthu, yemwe ndi wapamwamba pa zolengedwa zonse zapadzikoli, kuti aziimira chikondi, lomwe ndi khalidwe lake lalikulu.—Ezekieli 1:10.
-
-
“Mulungu Ndi Amene Anayamba Kutikonda”Yandikirani Yehova
-
-
b M’Baibulo muli mawu ena omwe analembedwa mofanana ndi amenewa. Mwachitsanzo, timawerenga kuti “Mulungu ndiye kuwala” ndiponso kuti “Mulungu . . . ndi moto wowononga.” (1 Yohane 1:5; Deuteronomo 4:24) Koma mawuwa tiyenera kuwaona kuti ndi ophiphiritsa chifukwa akuyerekezera Yehova ndi zinthu zooneka. Yehova ali ngati kuwala, chifukwa ndi woyera ndiponso wolungama. Kwa iye kulibe “mdima,” kapena kuti chinthu chodetsedwa. Ndipo tingamuyerekezere ndi moto chifukwa amagwiritsa ntchito mphamvu zake zowononga.
-