Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • fy mutu 11 tsamba 128-141
  • Sungani Mtendere m’Banja Mwanu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sungani Mtendere m’Banja Mwanu
  • Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • NGATI MWAMUNA WANU ALI NDI CHIKHULUPIRIRO CHINA
  • PAMENE MKAZI ALI NDI CHIKHULUPIRIRO CHINA
  • KUPHUNZITSA ANA
  • NGATI CHIPEMBEDZO CHANU CHILI CHOSIYANA NDI CHA MAKOLO ANU
  • VUTO LA KUKHALA KHOLO LOPEZA
  • KODI KUFUNA ZINTHU ZAKUTHUPI KUKUGAŴA BANJA LANU?
  • Zimene Mungachite Kuti Banja Lanu Lizisangalala
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kupangitsa Moyo Wabanja Kukhala Wabwino
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Kumaumanga Moyo Wabanja Wacimwemwe
    Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya
  • Makiyi Aŵiri a Ukwati Wokhalitsa
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
Onani Zambiri
Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
fy mutu 11 tsamba 128-141

Mutu 11

Sungani Mtendere m’Banja Mwanu

1. Kodi ndi zinthu zina ziti zimene zingachititse magaŵano m’mabanja?

ACHIMWEMWE ali awo amene ali m’mabanja mmene muli chikondi, chifundo, ndi mtendere. Tikhulupirira banja lanu lili lotero. Nzachisoni kuti mabanja ambiri sali otero ndipo ali ogaŵanika pazifukwa zosiyanasiyana. Kodi nchiyani chimene chimagaŵanitsa mabanja? M’mutu uno tidzakambitsirana zinthu zitatu. M’mabanja ena, anthu amakhala ndi zipembedzo zosiyana. Mwa ena, ana angakhale ndi makolo owabala osiyana. Mwa enanso, ntchito yochirikizira moyo kapena kufuna zinthu zakuthupi zambiri zimagaŵanitsa apabanja. Komabe, mikhalidwe imene imagaŵanitsa banja lina siingakhale vuto lalikulu ku banja lina. Kodi nchiyani chimachititsa kusiyana?

2. Kodi ena amakafuna kuti chithandizo pa moyo wa banja, koma kodi chitsogozo chabwino kopambana chimachokera kuti?

2 Chimodzi cha izo ndicho kaonedwe ka zinthu. Ngati mumayesayesa moona mtima kumvetsetsa lingaliro la mnzanu, mudzakhala wokhoza kuzindikira mmene mungasungire umodzi wa banja. Chinthu chachiŵiri ndicho amene mumafunako chithandizo. Anthu ambiri amalondola uphungu wa anzawo akuntchito, anansi awo, olemba m’madanga a manyuzipepala, kapena aphungu ena. Komabe, ena apeza zimene Mawu a Mulungu amanena za mkhalidwewo, ndiyeno amagwiritsira ntchito zimene amaphunzira. Kodi kuchita zimenezi kungathandize motani banja kusunga mtendere?—2 Timoteo 3:16, 17.

NGATI MWAMUNA WANU ALI NDI CHIKHULUPIRIRO CHINA

Chithunzi patsamba 130

Yesani kumvetsetsa lingaliro la mnzanu

3. (a) Kodi uphungu wa Baibulo ndi wotani ponena za kukwatirana ndi munthu wa chikhulupiriro china? (b) Kodi ndi mapulinsipulo ofunika ati amene amagwirabe ntchito ngati wina wa muukwati ali wokhulupirira koma osati mnzakeyo?

3 Baibulo limatichenjeza mwamphamvu kusakwatirana ndi munthu wa chikhulupiriro china. (Deuteronomo 7:3, 4; 1 Akorinto 7:39) Komabe, mwina inu munaphunzira choonadi cha Baibulo mutakwatirana kale koma mwamuna wanu sanatero. Pamenepo bwanji? Ndithudi, malumbiro aukwati akugwirabe ntchito. (1 Akorinto 7:10) Baibulo limagogomezera kukhalitsa kwa ukwati ndipo limalimbikitsa okwatirana kuthetsa mavuto awo m’malo mwa kuwathaŵa. (Aefeso 5:28-31; Tito 2:4, 5) Nanga bwanji ngati mwamuna wanu amakuletsani mwamphamvu kuchita chipembedzo chanu cha m’Baibulo? Iye angayese kukuletsani kupita kumisonkhano ya mpingo, kapena anganene kuti samafuna mkazi wake kumapita kunyumba ndi nyumba, akumalankhula za chipembedzo. Kodi mungachitenji?

4. Kodi mkazi angasonyeze motani kumvetsetsa ngati mwamuna wake sali naye m’chikhulupiriro chimodzi?

4 Dzifunseni kuti, ‘Kodi nchifukwa ninji mwamuna wanga amaganiza choncho?’ (Miyambo 16:20, 23) Ngati iye sakumvetsetsadi zimene mukuchita, angakhale wodera nkhaŵa za inu. Kapena angakhale akuvutitsidwa ndi achibale ake chifukwa chakuti simukuchitanso miyambo ina yofunika kwambiri kwa iwo. Mwamuna wina anati: “Potsala ndekha m’nyumba, ndinamva monga wosiyidwa.” Mwamunayu anaona monga kuti chipembedzo chinali kumlanda mkazi wake. Komabe, kunyada kunamlepheretsa kuvomera kuti anali kusungulumwa. Mwamuna wanu angafunikire kusonyezedwa kuti kukonda kwanu Yehova sikutanthauza kuti tsopano simumamkonda kwambiri kuposa kale. Patulani nthaŵi ya kucheza naye.

5. Kodi ndi kulinganiza zinthu kotani kumene mkazi ayenera kuchita amene mwamuna wake ali wa chikhulupiriro china?

5 Komabe, palinso chinthu china chofunika koposa chimene muyenera kuchilingalira ngati mufuna kuchita ndi mkhalidwewo mwanzeru. Mawu a Mulungu amalimbikitsa akazi kuti: “Akazi inu, muzimvera amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.” (Akolose 3:18) Motero, limachenjeza za mzimu wa kudzigangira. Ndiponso, mwa kunena kuti “monga kuyenera mwa Ambuye,” lembali limasonyeza kuti mkazi wogonjera kwa mwamuna wake ayeneranso kugonjera kwa Ambuye. Pafunika kulinganiza bwino.

6. Kodi ndi mapulinsipulo otani amene mkazi wachikristu ayenera kukumbukira?

6 Kwa Mkristu, kupezeka pamisonkhano ya mpingo ndi kuchitira umboni kwa ena za chikhulupiriro chanu cha Baibulo ndiko mbali zofunika kwambiri za kulambira koona zimene siziyenera kunyalanyazidwa. (Aroma 10:9, 10, 14; Ahebri 10:24, 25) Pamenepo, kodi mungachitenji ngati munthu akuletsani mwachindunji kulabadira zofunika za Mulungu zakutizakuti? Atumwi a Yesu Kristu analengeza kuti: “Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu.” (Machitidwe 5:29) Chitsanzo chawo chimatipatsa choonerapo chogwira ntchito pamikhalidwe yambiri m’moyo. Kodi chikondi chanu pa Yehova chidzakusonkhezerani kumpatsa kulambira koyenera iye yekha? Panthaŵi imodzimodzi, kodi chikondi chanu ndi ulemu kwa mwamuna wanu zidzakuchititsani kuyesa kuchita zimenezi mwa njira yolandirika kwa iye?—Mateyu 4:10; 1 Yohane 5:3.

7. Kodi mkazi wachikristu ayenera kukhala wofunitsitsa kuchitanji?

7 Yesu anasonyeza kuti si nthaŵi zonse pamene izi zidzakhala zotheka. Iye anachenjeza kuti chifukwa cha chitsutso pa kulambira koona, okhulupirira a m’mabanja ena angadzione kukhala opatulidwa, monga kuti lupanga linawadula kwa ena onse m’banja. (Mateyu 10:34-36) Zimenezi zinachitika kwa mkazi wina ku Japan. Iye anatsutsidwa ndi mwamuna wake kwa zaka 11. Mwamunayo anamzunza iye ndipo kaŵirikaŵiri anamkhomera kunja. Koma iye anapirira. Mabwenzi mumpingo wachikristu anamthandiza. Anapemphera mosaleka ndi kupeza chilimbikitso chachikulu pa 1 Petro 2:20. Mkazi wachikristu ameneyu anali wokhutira maganizo kuti ngati anakhalabe wolimba, tsiku lina mwamuna wake adzagwirizana naye pakulambira Yehova. Ndipo anaterodi.

8, 9. Kodi mkazi ayenera kuchita motani kuti apeŵe kuika zopinga zosafunika kwa mwamuna wake?

8 Pali zinthu zambiri zimene mungachite zothandiza mwamuna wanu kusintha maganizo. Mwachitsanzo, ngati mwamuna wanu amatsutsa chipembedzo chanu, musampatse zifukwa zodandaulira m’zinthu zina. Sungani nyumba kukhala yaukhondo. Samalani maonekedwe anu. Khalani wopatsa m’mawu achikondi ndi oyamikira. M’malo mokhala wosuliza, khalani wochirikiza. Sonyezani kuti mumadalira iye monga mutu wanu. Musabwezere ngati muona kuti wakulakwirani. (1 Petro 2:21, 23) Khalani wololera kupanda ungwiro kwaumunthu, ndipo ngati pabuka mkangano, khalani woyamba kupepesa modzichepetsa.—Aefeso 4:26.

9 Musalole misonkhano kukhala chifukwa chochedwetsera chakudya chake. Mungagaŵanenso mu utumiki wachikristu panthaŵi zimene mwamuna wanu sali panyumba. Nkwanzeru kwa mkazi wachikristu kusalalikira mwamuna wake ngati samafuna zimenezo. M’malo mwake, ayenera kutsatira uphungu wa mtumwi Petro wakuti: “Akazi inu, mverani amuna anu a inu nokha; kuti, ngatinso ena samvera mawu, akakodwe opanda mawu mwa mayendedwe a akazi; pakuona mayendedwe anu oyera ndi [ulemu wanu waukulu, NW].” (1 Petro 3:1, 2) Akazi achikristu amayesayesa kwambiri kusonyeza zipatso za mzimu wa Mulungu.—Agalatiya 5:22, 23.

PAMENE MKAZI ALI NDI CHIKHULUPIRIRO CHINA

10. Kodi mwamuna wokhulupirira ayenera kuchita motani kulinga kwa mkazi wake ngati ali wa chikhulupiriro china?

10 Bwanji ngati mwamuna ali wokhulupirira koma osati mkazi wake? Baibulo limapereka chitsogozo pa mikhalidwe yoteroyo. Limati: “Ngati mbale wina ali naye mkazi wosakhulupira, ndipo iye avomera mtima kukhala naye pamodzi, asalekane naye.” (1 Akorinto 7:12) Limalangizanso amuna kuti: “Kondani akazi anu.”—Akolose 3:19.

11. Kodi mwamuna angasonyeze motani kuti ali wozindikira bwino ndi wosamala pochita umutu wake pa mkazi wake wa chikhulupiriro china?

11 Ngati ndinu mwamuna wa mkazi wa chikhulupiriro china, khalani wosamala kwambiri kusonyeza ulemu kwa mkazi wanu ndi kulolera malingaliro ake. Monga munthu wachikulire, ayenera kukhala ndi ufulu winawake wa kutsatira zikhulupiriro za chipembedzo chake, ngakhale ngati simukugwirizana nazo. Panthaŵi yoyamba imene mulankhula naye za chikhulupiriro chanu, musayembekezere kuti pamenepo adzasiya zimene wakhulupirira kwa nthaŵi yaitali ndi kutsatira zina zatsopano. M’malo mwa kufulumira kutsutsa kuti zachipembedzo zimene iye ndi a banja lake akhala akuchita kwa nthaŵi yaitali zili zonyenga, yesani moleza mtima kulingalira naye za m’Malemba. Mwina amaona kukhala wonyalanyazidwa pamene mupereka nthaŵi yaikulu ku zochita za mpingo. Angatsutse zochita zanu za kutumikira Yehova, pamene kwenikweni pansi pa mtima akunena kuti: “Ndifuna muzikhalanso ndi ine nthaŵi yochuluka!” Lezani mtima. Mwa chifundo chanu chachikondi, m’kupita kwa nthaŵi angathandizidwe kuzindikira kulambira koona.—Akolose 3:12-14; 1 Petro 3:8, 9.

KUPHUNZITSA ANA

12. Ngakhale ngati mwamuna ndi mkazi ali ndi zikhulupiriro zosiyana, kodi mapulinsipulo a Malemba ayenera kugwiritsidwa ntchito motani pophunzitsa ana awo?

12 M’banja losagwirizana pakulambira, kuphunzitsa ana malangizo achipembedzo kumakhala kovuta nthaŵi zina. Kodi mapulinsipulo a Malemba ayenera kugwiritsiridwa ntchito motani? Baibulo limapatsa tate thayo lalikulu la kuphunzitsa ana, koma mayinso ali ndi mbali yofunika. (Miyambo 1:8; yerekezerani ndi Genesis 18:19; Deuteronomo 11:18, 19.) Ngakhale ngati savomereza umutu wa Kristu, tate amakhalabe mutu wa banja.

13, 14. Ngati mwamuna aletsa mkazi wake kupita ndi ana kumisonkhano yachikristu kapena kuphunzira nawo, kodi mkaziyo angachitenji?

13 Atate ena osakhulupirira samaletsa ngati mayi aphunzitsa ana nkhani zachipembedzo. Ena amaletsa. Bwanji ngati mwamuna wanu sakulolani kupita ndi ana kumisonkhano ya mpingo kapena ngakhale kukuletsani kuphunzira nawo Baibulo panyumba? Pamenepo mudzafunikira kuganizira mathayo anu ena—thayo lanu kwa Yehova Mulungu, kwa umutu wa mwamuna wanu, ndi kwa ana anu okondedwa. Kodi mungayanjanitse motani zimenezi?

14 Ndithudi mudzapempherera nkhaniyo. (Afilipi 4:6, 7; 1 Yohane 5:14) Koma potsirizira pake, ndinu amene muyenera kupanga chosankha cha njira imene mudzatenga. Ngati muchita mwanzeru, mukumamveketsa bwino kwa mwamuna wanu kuti simukutsutsa umutu wake, chitsutso chake chingachepe m’kupita kwa nthaŵi. Ngakhale ngati mwamuna wanu amakuletsani kupita ndi ana anu kumisonkhano kapena kuphunzira nawo Baibulo, mukhozabe kuwaphunzitsa. Polankhula nawo masiku onse ndi mwa kupereka chitsanzo chabwino, yesani kuwaphunzitsa kukonda Yehova, kukhulupirira Mawu ake, ndi kulemekeza makolo—kuphatikizapo atate awo—kudera nkhaŵa anthu ena, ndi kugwira ntchito mwakhama. M’kupita kwa nthaŵi, tateyo angaone zotulukapo zabwino ndipo angaone phindu la kuyesayesa kwanu kwakhama.—Miyambo 23:24.

15. Kodi tate wokhulupirira ali ndi thayo lotani pakuphunzitsa ana?

15 Ngati ndinu mwamuna wokhulupirira koma osati mkazi wanu, pamenepo muyenera kusenza thayo la kulera ana anu “m’chilango cha Yehova ndi kuwawongolera maganizo m’njira yake.” (Aefeso 6:4, NW) Pochita zimenezo, muyenera kukhala wokoma mtima, wachikondi, ndi wachifundo kwa mkazi wanu.

NGATI CHIPEMBEDZO CHANU CHILI CHOSIYANA NDI CHA MAKOLO ANU

16, 17. Kodi ndi mapulinsipulo a Baibulo otani amene ana ayenera kukumbukira ngati alondola chikhulupiriro chosiyana ndi cha makolo awo?

16 Sikulinso kwachilendo kuona ngakhale ana aang’ono akutsatira malingaliro achipembedzo osiyana ndi a makolo awo. Kodi nzimene zachitika kwa inu? Ngati ndi choncho, Baibulo lili ndi uphungu kwa inu.

17 Mawu a Mulungu amati: “Mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ichi nchabwino. Lemekeza atate wako ndi amako.” (Aefeso 6:1, 2) Zimenezo zimaphatikizapo ulemu woyenera kwa makolo. Komabe, ngakhale kuti kumvera makolo kuli kofunika, sikuyenera kuchitidwa mwa kunyalanyaza Mulungu woona. Pamene mwana afika pamsinkhu woyamba kupanga zosankha, amakhala ndi mlingo wokulirapo wa thayo la zochita zake. Zimenezi nzoona osati chabe ndi lamulo la boma komanso makamaka ponena za lamulo laumulungu. Baibulo limati: “Munthu aliyense wa ife adzadziŵerengera mlandu wake kwa Mulungu.”—Aroma 14:12.

18, 19. Ngati ana ali ndi chipembedzo chosiyana ndi cha makolo awo, kodi angathandize motani makolo awo kumvetsetsa bwino chikhulupiriro chawo?

18 Ngati zikhulupiriro zanu zikuchititsani kusintha moyo wanu, yesani kumvetsetsa malingaliro a makolo anu. Mwachionekere, iwo angakondwere pamene kuphunzira kwanu Baibulo ndi kugwiritsira ntchito ziphunzitso zake kumakuchititsani kuwalemekeza kwambiri, kuwamvera kwambiri, ndi kukhala wakhama pa zimene akuuzani kuchita. Komabe, ngati chikhulupiriro chanu chatsopano chimakuchititsaninso kukana zikhulupiriro ndi miyambo imene iwo amatsatira, angaone kuti mukutaya choloŵa chimene akufuna kukupatsani. Angaoperenso ubwino wanu ngati zimene mukuchita anthu sakuziyamikira kwanuko kapena ngati zikuchotsa maganizo anu pa kuchita zimene iwo aona kuti zingakuthandizeni kupita patsogolo mwakuthupi. Kunyada kungakhalenso chopinga. Angalingalire kuti, kwenikweni, mukusonyeza kuti ndinu wolondola ndipo iwo ali olakwa.

19 Chotero, mwamsanga yesani kupanga makonzedwe akuti makolo anu akaonane ndi ena a akulu kapena Mboni zina zokhwima za mpingo wanu. Limbikitsani makolo anu kufika ku Nyumba ya Ufumu kuti akadzimverere okha zimene zimaphunzitsidwa ndi kudzionera okha mtundu wa anthu amene Mboni za Yehova zili. M’kupita kwa nthaŵi, makolo anu angafeŵetse mtima. Ngakhale pamene makolo atsutsa mouma khosi, kuwononga mabuku ofotokoza Baibulo, ndi kuletsa ana kupita kumisonkhano yachikristu, kaŵirikaŵiri pamakhalabe mipata yokaŵerengera kwina kwake, kukambitsirana ndi Akristu anzanu, ndi kuchitira umboni anthu ena mwamwaŵi ndi kuwathandiza. Mungapempherenso kwa Yehova. Achichepere ena ayembekezera kufikira atakula ndi kudzikhalira okha kuti ayambe kuchita zowonjezereka. Komabe, mulimonse mmene mkhalidwe ungakhalire panyumba, musaiŵale ‘kulemekeza atate anu ndi amayi anu.’ Chitani mbali yanu kuthandizira kusunga mtendere panyumba. (Aroma 12:17, 18) Choposa zonse, funani mtendere ndi Mulungu.

VUTO LA KUKHALA KHOLO LOPEZA

20. Kodi ana angakhale ndi malingaliro otani ngati tate kapena mayi wawo ali kholo lopeza?

20 M’nyumba zambiri, mkhalidwe umene umabweretsa vuto lalikulu kwambiri si wa chipembedzo koma chibale. Mabanja ambiri lerolino ali ndi ana ochokera ku ukwati wakale wa kholo limodzi kapena onse aŵiri. M’banja lotero, ana angachite nsanje ndi kuipidwa kapena angakhale ndi vuto pofuna kumvera makolo onse. Chotulukapo, iwo angalefule kuyesayesa koona mtima kwa kholo lopezalo kuti likhale atate kapena amayi wabwino. Kodi nchiyani chimene chingathandize banja lopeza kukhala lachipambano?

Chithunzi patsamba 138

Kaya ndinu kholo lenileni kapena lopeza, dalirani chitsogozo cha Baibulo

21. Mosasamala kanthu za mikhalidwe yawo yovuta, kodi nchifukwa ninji makolo opeza ayenera kufuna chithandizo ku mapulinsipulo opezeka m’Baibulo?

21 Zindikirani kuti mosasamala kanthu za mikhalidwe yovuta imeneyo, mapulinsipulo a Baibulo amene adzetsa chipambano m’mabanja ena amagwiranso ntchito pambaliyi. Kunyalanyaza mapulinsipulo amenewo mwakanthaŵi, kungaoneke kuti kwathetsa vuto, koma mwachionekere kudzachititsa kusweka mtima pambuyo pake. (Salmo 127:1; Miyambo 29:15) Kulitsani nzeru ndi luntha—nzeru yogwiritsira ntchito mapulinsipulo aumulungu mukumakumbukira za mapindu amtsogolo, ndi luntha la kuzindikira chifukwa chimene ena m’banja amanenera kapena kuchita zinthu zina. Mufunikiranso kukhala wachifundo.—Miyambo 16:21; 24:3; 1 Petro 3:8.

22. Kodi nchifukwa ninji kungakhale kovuta kwa ana kulemekeza kholo lopeza?

22 Ngati ndinu kholo lopeza, mungakumbukire kuti pamene munali bwenzi chabe la banjalo, mwinamwake anawo anakulandirani bwino. Koma pamene mwakhala kholo lawo lopeza, mwina maganizo awo asintha. Pokumbukira kholo lawo lowabala limene silikukhalanso nawo, anawo angakhale akulimbana ndi vuto lofuna kumvera makolo onse, mwinamwake akumalingalira kuti mukufuna kulanda chikondi chimene ali nacho kwa kholo lawolo limene palibe. Nthaŵi zina, angakuuzeni poyera kuti sindinu atate wawo kapena amayi wawo. Mawu amenewo amapweteka. Komabe, ‘musakangaze mumtima mwanu kukwiya.’ (Mlaliki 7:9) Luntha ndi chifundo nzofunika kuti muchite ndi malingaliro a ana.

23. Kodi chilango chingaperekedwe motani m’banja la ana opeza?

23 Mikhalidwe imeneyo njofunika kwambiri pamene mukupereka chilango. Chilango choyenera nchofunika. (Miyambo 6:20; 13:1) Ndipo popeza kuti ana sali ofanana, chilangonso chingakhale chosiyana kwa wina ndi mnzake. Makolo ena opeza amaona kuti kumakhala bwino ngati kholo lobala nlimene liyamba kupereka chilango. Komabe, nkofunika kuti makolo onse aŵiri agwirizane pa chilangocho ndi kuchichirikiza, osati kukondera mwana amene munabala ndi kuchitira mwina kwa wopeza. (Miyambo 24:23) Kumvera nkofunika kwambiri, koma kulolera kupanda ungwiro kuyeneranso kukhalapo. Musachite mopambanitsa. Perekani chilango mwachikondi.—Akolose 3:21.

24. Kodi nchiyani chimene chingathandize kupeŵa mavuto a makhalidwe osayenera pakati pa osiyana ziŵalo m’banja lopeza?

24 Makambitsirano a banja angathandize kwambiri kuchinjiriza vuto. Angathandize banja kukumbukira nkhani zofunika kwambiri m’moyo. (Yerekezerani ndi Afilipi 1:9-11.) Akhozanso kuthandiza aliyense kuona mmene angathandizire banja kufikira zonulirapo zawo. Ndiponso, makambitsirano oona mtima a banja angapeŵetse mavuto a makhalidwe osayenera. Atsikana afunikira kudziŵa kuvala bwino ndi kudzisungira pamaso pa atate wawo wopeza ndi alongo awo opeza, ndipo anyamata ayenera kulangizidwa za khalidwe labwino kulinga kwa amayi wawo wopeza ndi alongo awo opeza.—1 Atesalonika 4:3-8.

25. Kodi ndi mikhalidwe yotani imene ingathandize kusunga mtendere m’banja lopeza?

25 Pochita ndi vuto lapadera la kukhala kholo lopeza, khalani woleza mtima. Kumatenga nthaŵi kukulitsa chibale chatsopano. Kuchititsa ana amene simunabale kuti akukondeni ndi kukulemekezani kungakhale ntchito yaikulu kwambiri. Koma nkotheka. Mtima wanzeru ndi waluntha, limodzi ndi chikhumbo champhamvu chofuna kukondweretsa Yehova, ndizo kiyi yodzetsa mtendere m’banja lopeza. (Miyambo 16:20) Mikhalidwe yoteroyo ingakuthandizeninso kuchita ndi mikhalidwe inanso.

KODI KUFUNA ZINTHU ZAKUTHUPI KUKUGAŴA BANJA LANU?

26. Kodi kusoŵa zinthu zakuthupi ndi kaonedwe ka zinthu zakuthupi zingachititse magaŵano m’banja m’njira zotani?

26 Kusoŵa zinthu zakuthupi ndi kaonedwe ka zinthu zakuthupi kungachititse magaŵano m’mabanja m’njira zambiri. Mwachisoni, mabanja ena amasokonezedwa ndi mikangano ya ndalama ndi chikhumbo cha kufuna kulemera—kapena kulemera koposerapo. Magaŵano angayambe pamene okwatirana onse aŵiri agwira ntchito ndipo akhala ndi maganizo akuti “ndalama zanga, ndi ndalama zako.” Ngakhale ngati mikangano ipeŵedwa, pamene okwatirana aŵiriwo agwira ntchito, angaone kuti ali otanganitsidwa ndi zochita kwakuti alibe nthaŵi yokwanira yokhala pamodzi. Mkhalidwe womakula m’dziko ndiwo wakuti tate akukakhala kutali ndi banja kwa nyengo yaitali—miyezi kapena ngakhale zaka—kuti apeze ndalama zochuluka kuposa zimene angapeze kwawo. Izi zingachititse mavuto aakulu kwambiri.

27. Kodi ndi mapulinsipulo ena ati amene angathandize banja lokhala pa vuto la ndalama?

27 Palibe malamulo amene angaikidwe ochitira ndi mikhalidwe imeneyi, chifukwa chakuti mabanja osiyanasiyana amakumana ndi mavuto osiyanasiyana ndi zosoŵa zosiyanasiyana. Chikhalirechobe, uphungu wa Baibulo ungathandize. Mwachitsanzo, Miyambo 13:10 imasonyeza kuti kupikisana kosafunikira kungapeŵedwe mwa kufunsirana “uphungu.” Zimenezi zimaloŵetsamo osati chabe kupereka malingaliro a munthuwe komanso kufuna chilangizo ndi kudziŵa mmene winayo amaonera nkhaniyo. Ndiponso, kupanga bajeti yabwino kungathandize kugwirizanitsa zoyesayesa za banja. Nthaŵi zina kumakhala kofunika—mwinamwake kwakanthaŵi chabe—kwa okwatirana onse aŵiri kukaloŵa ntchito kuti asamalire zolipirira zowonjezereka, makamaka pamene pali ana kapena ena amene amawasunga. Pamene zili choncho, mwamuna ayenera kusonyeza mkazi wake kuti akali ndi nthaŵi yocheza naye. Iye pamodzi ndi ana mwachikondi angathandize ntchito zina zimene kaŵirikaŵiri mkazi wake amazichita yekha.—Afilipi 2:1-4.

28. Kodi ndi zikumbutso zotani, zimene ngati zitsatiridwa, zingathandize banja kukulitsa umodzi?

28 Komabe, kumbukirani kuti ngakhale kuti ndalama zili zofunika m’dziko lino, sizimadzetsa chimwemwe. Sizimapatsa moyo ayi. (Mlaliki 7:12) Ndithudi, kukondetsa zinthu zakuthupi kungachititse ngozi yauzimu ndi yamakhalidwe. (1 Timoteo 6:9-12) Nkoposa kotani nanga kufuna choyamba Ufumu wa Mulungu ndi chilungamo chake, ndi chidaliro cha kulandira madalitso ake pa zoyesayesa zathu za kupeza zofunika m’moyo! (Mateyu 6:25-33; Ahebri 13:5) Mwa kuika zinthu zauzimu patsogolo ndi kufuna mtendere ndi Mulungu choyamba, mungapeze kuti banja lanu, ngakhale kuti mwina lingakhale logaŵanika chifukwa cha mikhalidwe ina, lidzakhala logwirizana kwenikweni m’mbali zofunika koposa.

KODI MAPULINSIPULO A BAIBULO AŴA ANGATHANDIZE MOTANI . . . A M’BANJA KUSUNGA MTENDERE M’NYUMBA MWAWO?

Akristu amakulitsa luntha.—Miyambo 16:21; 24:3.

Kusonyezana chikondi ndi ulemu muukwati sikumadalira pa kukhala ndi chipembedzo chimodzi.—Aefeso 5:23, 25.

Mkristu samayesa kuswa lamulo la Mulungu mwadala.—Machitidwe 5:29.

Akristu ali osunga mtendere.—Aroma 12:18.

Musafulumire kukwiya.—Mlaliki 7:9.

MAUKWATI OYENERA AMADZETSA ULEMU NDI MTENDERE

Masiku ano amuna ndi akazi ambiri amakhala pamodzi popanda ukwati wa lamulo. Uwu ndiwo mkhalidwe umene wokhulupirira watsopano angafunikire kuwongolera. M’zochitika zina ukwatiwo ungavomerezedwe ndi apamudzipo kapena mwambo wa mtunduwo, koma suli walamulo. Komabe, muyezo wa Baibulo umafuna ukwati wolembetsa bwino. (Tito 3:1; Ahebri 13:4) Kwa anthu amene ali mumpingo wachikristu, Baibulo limafunanso kuti akhale ndi mwamuna mmodzi ndi mkazi mmodzi muukwati. (1 Akorinto 7:2; 1 Timoteo 3:2, 12) Kutsatira muyezo umenewu ndiko njira yoyamba yopezera mtendere m’nyumba mwanu. (Salmo 119:165) Zofuna za Yehova sizili zosatheka kapena zolemetsa. Zimene amatiphunzitsa nzotipindulitsa.—Yesaya 48:17, 18.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena