Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/04 tsamba 1
  • Kum’patsa Yehova Zabwino Koposa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kum’patsa Yehova Zabwino Koposa
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Nsembe Zotamanda Zimene Zimakondweretsa Yehova
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Phunzirani Kuchokera ku Choonadi cha M’chilamulo
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Tizipereka Nsembe kwa Yehova ndi Moyo Wathu Wonse
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Funafunani Ufumu wa Mulungu Choyamba—Mwa Kupereka Nsembe za Chitamando Nthaŵi Zonse
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 4/04 tsamba 1

Kum’patsa Yehova Zabwino Koposa

1 Chilamulo cha Yehova kwa Israyeli chinanena momveka bwino kuti nsembe za nyama zoperekedwa kwa iye zizikhala ‘zopanda chilema.’ Nyama yachilema inali yosayenera. (Lev. 22:18-20; Mal. 1:6-9) Komanso, popereka nsembe, mafuta onse—omwe anali mbali yabwino koposa—anali a Yehova. (Lev. 3:14-16) Popeza Yehova anali Atate ndi Mbuye wa Israyeli, iye anafunika zabwino koposa.

2 Monga mmene zinalili kale, masiku anonso Mulungu ali ndi chidwi choona mmene nsembe zathu zilili. Utumiki wathu uyenera kusonyeza kuti timam’patsa Yehova ulemu womuyenera. N’zoona kuti anthufe tili ndi moyo wosiyanasiyana. Komabe, tili ndi chifukwa chomveka chodzipendera kuti titsimikizire kuti tikum’patsa zabwino koposa.—Aef. 5:10.

3 Kutumikira ndi Mtima Wonse: Kuti utumiki wathu ulemekeze Yehova ndi kuwafika pamtima omvera athu, suyenera kuchitika mwachizoloŵezi chabe. Zimene timanena zokhudza Mulungu wathu ndi zolinga zake zazikulu zizichokera mu mtima woyamikira. (Sal. 145:7) Zimenezi zikutsindika kufunika kokhalabe ndi ndondomeko yabwino yoŵerenga ndi kuphunzira Baibulo patokha.—Miy. 15:28.

4 Kum’patsa Yehova zabwino koposa kumaphatikizaponso kutsanzira kukonda kwake anthu. (Aef. 5:1, 2) Kukonda anthu kudzatipangitsa kuyesetsa kufikira anthu ambiri mmene tingathere ndi uthenga wopatsa moyo wa choonadi. (Marko 6:34) Kumatilimbikitsa kusonyeza chidwi kwa anthu amene timalankhula nawo. Kumatipangitsa kuti tiziwaganizirabe tikachoka panyumba yawo paulendo woyamba ndipo kumatilimbikitsa kubwererakonso. Kumatilimbikitsa kuchita zonse zimene tingathe kuti tiwathandize kupita patsogolo mwauzimu.—Mac. 20:24; 26:28, 29.

5 “Nsembe Yakuyamika”: Njira ina imene timam’patsira Yehova zabwino koposa ndiyo kuchita khama mu utumiki. Ngati tili adongosolo ndiponso ngati tiika maganizo pantchito imene tapatsidwa, tingachite zambiri m’nthaŵi imene tili nayo. (1 Tim. 4:10) Kukonzekera bwino kumatithandiza kulankhula zomveka ndiponso mwachidaliro, zimene zimathandiza kuti anthu alabadire uthenga wathu. (Miy. 16:21) Pouza ena uthenga wabwino, zimene timalankhula kuchokera pansi pamtima zingatchedwedi kuti “nsembe yakuyamika.”—Aheb. 13:15.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena