Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lmd phunziro 3
  • Kukoma Mtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kukoma Mtima
  • Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Yesu Anachita
  • Zomwe Tikuphunzira kwa Yesu
  • Zomwe Mungachite Potsanzira Yesu
  • Kuchita Chidwi ndi Anthu
    Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa
  • “Lamulo la Kukoma Mtima Kosatha” Lizikutsogolerani
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
  • Kukhala Okoma Mtima M’dziko Losaganiziranali
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Mkondweretseni Yehova Mwakusonyeza Kukoma Mtima
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa
lmd phunziro 3

ULENDO WOYAMBA

Yesu mokoma mtima akukhudza munthu wavuto losaona kuti amuchiritse.

Yohane 9:1-7

PHUNZIRO 3

Kukoma Mtima

Mfundo yaikulu: “Chikondi . . . n’chokoma mtima.”​—1 Akor. 13:4.

Zomwe Yesu Anachita

Yesu mokoma mtima akukhudza munthu wavuto losaona kuti amuchiritse.

VIDIYO: Yesu Anachiritsa Munthu Wavuto Losaona

1. Onerani VIDIYO, kapena werengani Yohane 9:1-7. Kenako kambiranani mafunso otsatirawa:

  1. Kodi Yesu anayamba n’kutani, kuchiritsa munthuyo kapena kukambirana naye uthenga wabwino?​—Onani Yohane 9:35-38.

  2. N’chifukwa chiyani tinganene kuti mmene Yesu anafikira, zinathandiza kuti munthuyo amvetsere uthenga wabwino?

Zomwe Tikuphunzira kwa Yesu

2. Nthawi zambiri munthu angachite chidwi ndi uthenga wathu akaona kuti tikuchita naye zinthu momuganizira.

Zomwe Mungachite Potsanzira Yesu

3. Muzikhala achifundo. Muziganizira mmene munthuyo akumvera.

  1. Dzifunseni kuti: ‘Kodi akhoza kukhala kuti akuda nkhawa ndi chiyani? Kodi angasangalale nditamuuza zotani?’ Mukamaganizira zimenezi, mwachibadwa mudzamusonyeza kukoma mtima.

  2. Muzisonyeza kuti mukumudera nkhawa pomumvetsera. Akakuuzani mmene akumvera ndi nkhani inayake kapena akakuuzani mavuto omwe akukumana nawo, musamasinthe nkhani.

4. Muzilankhula mokoma mtima komanso mwaulemu. Ngati mwakhudzika ndi munthuyo ndipo mukufunitsitsa kumuthandiza, adzazindikira zimenezo poona mmene mukulankhulira. Muzisamala ndi zomwe mukulankhula komanso mmene mukulankhulira kuti musamukhumudwitse.

5. Muzikhala ofunitsitsa kuthandiza. Yesetsani kupeza mipata yothandizira munthuyo. Mukamachita zinthu mokoma mtima simudzavutika kuyamba kukambirana ndi anthu.

ONANINSO MALEMBA AWA

Aroma 12:15, 16; Agal. 6:10; Aheb. 13:16

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena