Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 102
  • Kodi Kutchova Juga Ndi Tchimo?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Kutchova Juga Ndi Tchimo?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Kodi Kutchova Juga ndi kwa Akristu?
    Galamukani!—1994
  • Kodi Kutchova Njuga Kuli Ndi Vuto Lanji?
    Galamukani!—2002
  • Oseŵera Juga Atsopano—Achichepere!
    Galamukani!—1995
  • Peŵani Msampha wa Kutchova Njuga
    Galamukani!—2002
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 102
Munthu wotchova juga akuona patikiti yake ya loto pamene zotsatira za maere zikulengezedwa pa TV

Kodi Kutchova Juga Ndi Tchimo?

Yankho la m’Baibulo

Ngakhale kuti Baibulo silifotokoza mwatsatanetsatane zokhudza juga, mfundo za m’Baibulo zingatithandize kuzindikira kuti Mulungu amaona kuti khalidweli ndi tchimo.​—Aefeso 5:17.a

  • Anthu amatchova juga chifukwa cha dyera ndipo Mulungu amadana ndi khalidwe limeneli. (1 Akorinto 6:9, 10; Aefeso 5:3, 5) Kuti munthu wotchova juga awine, pamafunika kuti anzake aluze, koma Baibulo limaletsa kusirira zinthu za anthu ena mwansanje.​—Ekisodo 20:17; Aroma 7:7; 13:9, 10.

  • Kutchova juga, ngakhale pang’ono pokha, kungachititse munthu kuti ayambe kukonda kwambiri ndalama.​—1 Timoteyo 6:9, 10.

  • Nthawi zambiri anthu otchova juga amadalira matsenga kapena mwayi. Komabe, Mulungu amaona kuti kukhulupirira zimenezi ndi kulambira mafano, komwe sikugwirizana ndi kulambira kumene iye amavomereza.​—Yesaya 65:11.

  • M’malo molimbikitsa khalidwe lomapeza zinthu zomwe sitinazigwirire ntchito, Baibulo limatilimbikitsa kugwira ntchito mwakhama. (Mlaliki 2:24; Aefeso 4:28) Anthu omwe amatsatira malangizowa ‘amadya chakudya chimene achigwirira ntchito.’​—2 Atesalonika 3:10, 12.

  • Kutchova juga kumalimbikitsa khalidwe la mpikisano, lomwe limaletsedwa m’Baibulo.​—Agalatiya 5:26.

a M’Baibulo, kutchova juga kumatchulidwa mwachindunji kamodzi kokha pa nkhani yonena za asilikali a Roma omwe anachita maere, kapena kuti “anatchova juga” pa chovala cha Yesu.​—Mateyu 27:35; Yohane 19:23, 24; Contemporary English Version; Good News Translation.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena