Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w08 9/1 tsamba 3
  • Kodi Mumawadziwa Atate Wanu wa Kumwamba?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumawadziwa Atate Wanu wa Kumwamba?
  • Nsanja ya Olonda—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Atate Wathu Yehova Amatikonda Kwambiri
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
  • Kodi Mumaona Kuti Yehova Ndi Atate Wanu?
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Kodi Mulungu Ndi Ndani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2019
  • ‘Mwana Amakonda Kuululira Ena za Atate’
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2008
w08 9/1 tsamba 3

Kodi Mumawadziwa Atate Wanu wa Kumwamba?

KODI mumawadziwa bwino bambo wanu? Ngati munaleredwa ndi makolo achikondi mwina mungadabwe ndi funso limeneli. Ndipo mungayankhe mosakayika kuti, ‘Ee, ndimawadziwa bwinobwino.’ Inde, anthu ambiri amadziwa zimene bambo awo amakonda ndi zimene sakonda. Amadziwanso zimene angachite ngati patachitika zinthu zinazake, ndiponso amadziwa kuti amakonda kwambiri banja lawo.

Komabe n’kutheka kuti nthawi ina munadabwa kuona bambo anu atachita zinthu zinazake zimene simumayembekezera. Mwachitsanzo, mwana angaganize kuti bambo ake ndi munthu wofatsa waphee, koma angadabwe mmene bambowo angachitire patachitika zinazake mwadzidzidzi. Panthawiyi, angaone kuti bambo ake ndi olimba mtima kwambiri moti angalolere kuchita chilichonse kuti ateteze banja lawo.

Nanga bwanji Mlengi wathu? Baibulo limatiuza kuti: “Mwa iye tili ndi moyo, timayenda, ndi kukhalapo.” (Machitidwe 17:28) Moyo wathuwu anatipatsa ndi Mulungu, motero tingati iyeyo ndi Atate wa aliyense amene ali moyo. (Yesaya 64:8) Kodi Mulungu mumamuona m’njira imeneyi? Ngati mumatero ndiye kuti mukuchita bwino. Komatu pali zinthu zambiri zopindulitsa ndiponso zosalangalatsa zimene tiyenera kudziwa zokhudza iyeyu.

Bambo wanu mumawakonda ndi kuwalemekeza chifukwa choti mumawadziwa bwino. Umu ndi mmenenso zilili ndi Mulungu. Mukamudziwa bwino mumam’kondanso kwambiri. Mukam’dziwa bwino Mulungu n’kumachita chifuniro chake, angathe kukuthandizani pa mayesero ndi mavuto amene mumakumana nawo.

Ndiyeno kodi Mulungu ndi wotani kwenikweni? Kodi makhalidwe ake amayenera kukhudza bwanji mmene timam’kondera? Kodi kudziwa Mulungu kumakupatsani udindo uliwonse? Mayankho a mafunso amenewa muwapeza m’nkhani yotsatirayi.

[Mawu Otsindika patsamba 3]

Mumakonda munthu mogwirizana ndi mmene mumam’dziwira

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena