Kalata Yopita kwa Akolose
1 Ine Paulo amene ndinakhala mtumwi wa Khristu Yesu malinga ndi cifunilo ca Mulungu, ndili limodzi ndi Timoteyo m’bale wathu. 2 Ndikulembela oyela ndi abale okhulupilika a ku Kolose amene ali mu mgwilizano ndi Khristu kuti:
Cisomo komanso mtendele wa Mulungu Atate wathu zikhale nanu.
3 Nthawi zonse timakuchulani m’mapemphelo athu, ndipo timayamika Mulungu Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu. 4 Timatelo cifukwa tinamva za cikhulupililo canu mwa Khristu Yesu, komanso za cikondi cimene mumaonetsa kwa oyela onse. 5 Mukucita zimenezi cifukwa ca ciyembekezo ca zinthu zimene akusungilani kumwamba. Ciyembekezo cimeneci, munacimva m’mbuyomu pamene munamva uthenga wa coonadi 6 umene unafika kwa inu, ndipo ukubala zipatso komanso ukufalikila padziko lonse. Izi ndi zimenenso zakhala zikucitika kwa inu kuyambila tsiku limene munamva ndi kudziwa molondola za cisomo ca Mulungu cimene ndi ceniceni. 7 Izi n’zimene munaphunzila kwa Epafura, kapolo mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupilika wa Khristu m’malo mwa ife. 8 Iye ndi amenenso anatidziwitsa za cikondi canu cimene munationetsa mothandizidwa ndi mzimu wa Mulungu.*
9 N’cifukwa cake nafenso, kungoyambila tsiku limene tinamva zimenezo, sitinasiye kukupemphelelani. Ndipo takhala tikupemphanso kuti mudzadzidwe ndi cidziwitso colongosoka ca cifunilo ca Mulungu, kuti mukhale ndi nzelu zonse, komanso kuti muzimvetsetsa zinthu zauzimu. 10 Tacita izi kuti muziyenda mogwilizana ndi zimene Yehova amafuna, kuti muzimukondweletsa pa ciliconse, pamene mukupitiliza kubala zipatso pa nchito iliyonse yabwino, komanso kuonjezela cidziwitso colongosoka ca Mulungu. 11 Ndipo tikupemphelelanso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu zake zonse zaulemelelo, ndi colinga coti muthe kupilila zinthu zonse moleza mtima, ndiponso mwacimwemwe, 12 kwinaku mukuyamika Atate, amene anakuyeneletsani kuti mulandile nao colowa ca oyela amene ali m’kuwala.
13 Iye anatipulumutsa ku ulamulilo wa mdima, n’kutisamutsila mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa. 14 Kudzela mwa Mwana wakeyo, anatimasula ndi dipo,* ndipo macimo athu amakhululukidwa. 15 Iye ndi cifanizilo ca Mulungu wosaonekayo, woyamba kubadwa wa cilengedwe conse. 16 Kupyolela mwa iye, Mulungu analenga zinthu zina zonse, za kumwamba ndi za padziko lapansi. Analenga zinthu zooneka ndi zinthu zosaoneka. Kaya ndi mipando yacifumu, ambuye, maboma, komanso maulamulilo. Inde, analenga zinthu zina zonse kudzela mwa iye ndiponso cifukwa ca iye. 17 Iye analipo kale zinthu zina zonse zisanakhaleko, ndipo zinthu zina zonse zinakhalapo kupitila mwa iye. 18 Iye ndi mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndi ciyambi, woyamba kubadwa kucokela kwa akufa, kuti adzakhale woyamba pa zinthu zonse. 19 Zili conco cifukwa cakuti Mulungu zinamusangalatsa kuti makhalidwe ake onse akhale mwa Yesu. 20 Komanso kuti kudzela mwa Mwana wakeyo ayanjanitsenso zinthu zina zonse ndi iyeyo, kaya zinthuzo ndi za padziko lapansi kapena za kumwamba. Anacita zimenezi pokhazikitsa mtendele kudzela m’magazi amene Yesu anakhetsa pamtengo wozunzikilapo.*
21 Kale inu munali otalikilana ndi Mulungu, ndiponso munali adani ake cifukwa maganizo anu anali pa nchito zoipa. 22 Koma tsopano wakuyanjaninso kudzela mu imfa ya mwana wake amene anapeleka thupi lake la nyama kuti inu mukhale oyela, opanda ulemali, ndiponso opanda cifukwa cokunenezelani pamaso pake, 23 malinga ngati mupitilizabe m’cikhulupililo, muli okhazikika pa maziko ndiponso olimba, komanso muli osasunthika pa ciyembekezo ca uthenga wabwino umene munamva, umenenso unalalikidwa padziko lonse. Ine Paulo ndinakhala mtumiki wa uthenga wabwino umenewu.
24 Tsopano ine ndikusangalala kuti ndikubvutika cifukwa ca inu. Ndipo ine ndikuona kuti ndikalibe kufikapo pa kusautsika kwenikweni monga ciwalo ca thupi la Khristu, limene ndi mpingo. 25 Ndinakhala mtumiki wa mpingo umenewu malinga ndi udindo umene Mulungu anandipatsa wakuti ndilalikile mau a Mulungu mokwanila, kuti inuyo mupindule. 26 Mau amenewa akuphatikizapo cinsinsi copatulika cimene dziko silinacidziwe, ndiponso cinali cobisika ku mibadwo ya m’mbuyomu. Koma tsopano cabvumbulidwa kwa oyela ake, 27 amene Mulungu zinamusangalatsa kuwadziwitsa oyelawo pakati pa mitundu ina za cinsinsi copatulika, inde cuma caulemelelo cimeneci. Cinsinsici n’cakuti Khristu ali mu mgwilizano ndi inu, ndipo muli ndi ciyembekezo codzagawana naye ulemelelo wake. 28 Tikulengeza, kulangiza, ndi kuphunzitsa munthu aliyense za iyeyu mu nzelu zonse, kuti tipeleke munthu aliyense ali wathunthu kwa Mulungu mu mgwilizano ndi Khristu. 29 Kuti zimenezi zitheke, ndikugwila nchito mwakhama komanso mokangalika podalila mphamvu zake zimene zikugwila nchito mwa ine.