Kalata Yopita kwa Akolose
2 Ndikufuna kuti mudziwe mabvuto aakulu amene ndikukumana nao cifukwa ca inu ndi anthu a ku Laodikaya, kuphatikizapo anthu onse amene sanandionepo maso ndi maso. 2 Ndikucita izi kuti mitima yao ilimbikitsidwe, ndiponso kuti onse akhale ogwilizana m’cikondi, komanso kuti alandile cuma conse cimene cimabwela cifukwa comvetsa bwino zinthu popanda kudodoma kulikonse, kuti apeze cidziwitso colongosoka ca cinsinsi copatulika ca Mulungu, comwe ndi Khristu. 3 Cuma conse cokhudzana ndi nzelu komanso kudziwa zinthu cinabisidwa mwa iye mosamala. 4 Ndikunena izi kuti munthu aliyense asakupusitseni ndi mfundo zokopa. 5 Ngakhale kuti sindili nanu kumeneko, mwa mzimu ndili nanu limodzi. Ndakondwela kumva kuti mumacita zinthu mwa dongosolo, komanso kuti muli ndi cikhulupililo colimba mwa Khristu.
6 Cotelo popeza mumakhulupilila Khristu Yesu Ambuye wathu, pitilizani kuyenda mogwilizana naye, 7 kukhala ozika mizu mwa iye ndi omangidwa pa iye, komanso okhazikika m’cikhulupililo, malinga ndi zimene munaphunzila. Ndipo mitima yanu izisefukila ndi mayamiko.
8 Cenjelani kuti wina asakugwileni ukapolo* ndi nzelu za anthu ndi cinyengo copanda pake, malinga ndi miyambo ya anthu, malinganso ndi mfundo zimene anthu a dzikoli amayendela, osati malinga ndi Khristu, 9 pakuti mwa Khristu ndi mmene muli makhalidwe onse aumulungu. 10 Conco inu simukusowa kalikonse cifukwa ca iye, amene ndi mutu wa boma ndi ulamulilo wonse. 11 Popeza muli naye pa ubale munacita mdulidwe, ndipo mdulidwe wake sunacitike ndi manja a anthu, koma unacitika pamene munabvula thupi laucimo. Umenewo ndiwo mdulidwe wa Khristu. 12 Pakuti munaikidwa naye limodzi m’manda pobatizidwa ubatizo wofanana ndi wake. Ndipo popeza muli naye pa ubale, munaukitsidwa naye limodzi cifukwa ca cikhulupililo canu mu mphamvu ya Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa.
13 Kuonjezela apo, inu munali akufa cifukwa ca macimo anu, komanso cifukwa coti munali osadulidwa. Ngakhale n’telo, Mulungu anakupatsani moyo limodzi ndi Khristu. Mokoma mtima iye anatikhululukila macimo athu onse, 14 ndipo anafafaniza cikalata cimene cinali ndi malamulo ndipo cinali kutitsutsa. Iye anacicotsa pocikhomelela pamtengo wozunzikilapo.* 15 Pogwilitsila nchito mtengo wozunzikilapowo, iye anabvula maboma ndi olamulila n’kuwasiya osabvala, ndipo anawaonetsa poyela kwa anthu onse kuti aone kuti wawagonjetsa, n’kumayenda nao ngati akaidi pa cionetselo conyadila kupambana.
16 Conco musalole kuti munthu aliyense akuweluzeni pa nkhani ya cakudya ndi cakumwa, kapena cikondwelelo cinacake, kapenanso kusunga tsiku lokhala mwezi kapena kusunga sabata. 17 Zinthu zimenezi ndi mthunzi wa zimene zinali kubwela, koma zenizeni zake ndi Khristu. 18 Musalole munthu aliyense amene amasangalala ndi kudzicepetsa kwaciphamaso komanso kulambila angelo* kukulepheletsani kudzalandila mphoto. “Munthu woteloyo amaumilila” zinthu zimene waona, ndipo maganizo ake ocimwa amamusonkhezela kuti azidzitukumula popanda cifukwa comveka. 19 Iye salumikizana ndi mutu, yemwe kudzela mwa iye, thupi lonse limapeza zonse zimene limafunikila, ndipo ziwalo zake ndi zolumikizana bwino ndi mfundo za thupilo komanso minyewa yake, ndipo limakulabe mothandizidwa ndi Mulungu.
20 Popeza munafa limodzi ndi Khristu, ndipo simukutsatilanso mfundo zimene anthu a dzikoli amayendela, n’cifukwa ciani mukukhala ngati a dzikoli, popitiliza kugonjela malamulo akuti: 21 “Usagwile cakuti,” “usalawe cakuti,” kapena “usakhudze cakuti”? 22 Zinthu zimenezi zimatha anthu akamazigwilitsila nchito. Amenewa ndi malamulo ndi ziphunzitso za anthu. 23 Ngakhale kuti zinthu zimenezi zimaoneka ngati zanzelu, ndi kulambila kongodzipangila okha, kudzicepetsa kwaciphamaso, kuzunza thupi, ndipo sizithandiza munthu polimbana ndi zilakolako za thupi.