Kalata Yopita kwa Akolose
3 Komabe ngati munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, pitilizani kufunafuna zinthu za kumwamba, kumene Khristu wakhala kudzanja lamanja la Mulungu. 2 Pitilizani kuganizila zinthu za kumwamba, osati za padziko lapansi. 3 Paja inu munafa, ndipo moyo wanu wakhala wobisidwa limodzi ndi Khristu amene ali mu mgwilizano ndi Mulungu. 4 Khristu amene ndi moyo wathu akadzaonetsedwa, inunso mudzaonetsedwa naye limodzi mu ulemelelo.
5 Conco iphani ziwalo za thupi lanu padziko lapansi pa nkhani ya ciwelewele,* zinthu zodetsa, cilakolako cosalamulilika ca kugonana, cilakolako cofuna kucita zoipa, komanso dyela limene ndi kulambila mafano. 6 Cifukwa ca zinthu zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwela. 7 Kale, inunso munali kucita zimenezo, malinga ndi umoyo wanu wa panthawi imeneyo. 8 Koma tsopano muzitayile kutali ndi inu zinthu zonsezi. Mutaye mkwiyo, kupsya mtima, kuipa, komanso mau acipongwe, ndipo pakamwa panu pasatuluke mau otukwana. 9 Musamauzane mabodza. Bvulani umunthu* wakale pamodzi ndi nchito zake. 10 Ndipo mubvale umunthu watsopano umene cifukwa ca cidziwitso colondola, umakhala watsopano malinga ndi cifanizilo ca Mulungu amene anaulenga. 11 Mukatelo, sipadzakhala Mgiriki kapena Myuda, kudulidwa kapena kusadulidwa, mlendo, Msukuti,* kapolo kapena mfulu, cifukwa Khristu ndi zonse ndipo ali mwa onse.
12 Conco popeza Mulungu anakusankhani, inu oyela ndi okondedwa, bvalani cifundo cacikulu, kukoma mtima, kudzicepetsa, kufatsa, komanso kuleza mtima. 13 Pitilizani kulolelana ndi kukhululukilana mocokela pansi pa mtima, ngakhale pamene wina ali ndi cifukwa comveka codandaulila za mnzake. Monga mmene Yehova anakukhululukilani ndi mtima wonse, inunso muzicita cimodzi-modzi. 14 Koma kuonjezela pa zonsezi, bvalani cikondi, cifukwa ndico comangila umodzi cangwilo.
15 Cinanso, lolani kuti mtendele wa Khristu uzilamulila m’mitima yanu, pakuti anakuitanani ku mtendele umenewu monga ziwalo za thupi limodzi. Ndipo muzionetsa kuti ndinu oyamikila. 16 Mau a Khristu akhazikike mofikapo mwa inu ndi nzelu zonse. Pitilizani kuphunzitsana ndi kulimbikitsana* wina ndi mnzake pogwilitsa nchito masalimo, nyimbo zotamanda Mulungu, komanso nyimbo zauzimu zoyamikila. Pitilizani kuimbila Yehova m’mitima yanu. 17 Ciliconse cimene mukucita, kaya mukulankhula kapena kugwila nchito, muzicita zonse m’dzina la Ambuye Yesu, ndipo muziyamika Mulungu Atate kudzela mwa iye.
18 Inu akazi, muzigonjela amuna anu, cifukwa ndi zimene Ambuye amafuna. 19 Inu amuna, muzikonda akazi anu ndipo musamawapsyele mtima.* 20 Inu ana, muzimvela makolo anu pa zinthu zonse, cifukwa zimenezi Ambuye amakondwela nazo. 21 Inu atate, musamakwiyitse* ana anu, kuti asakhale okhumudwa. 22 Inu akapolo, muzimvela ambuye anu pa zinthu zonse. Musamangocita zimenezi pamene muli pamaso pao, pofuna kukondweletsa anthu. Koma muzitelo moona mtima ndiponso moopa Yehova. 23 Ciliconse cimene mukucita, muzicicita ndi moyo wanu wonse, komanso mphamvu zanu zonse ngati kuti mukucitila Yehova, osati anthu, 24 cifukwa mukudziwa kuti Yehova ndiye adzakupatsani colowa monga mphoto. Tumikilani Ambuye wanu Khristu monga akapolo. 25 Ndithudi, amene akucita zolakwa sadzalephela kulandila cilango pa zolakwa zimene akucitazo, cifukwa Mulungu sakondela.