Wolembedwa na Mateyo
11 Yesu atatsiliza kupeleka malangizo kwa ophunzila ake 12, anacoka kumeneko n’kupita kukaphunzitsa na kukalalikila ku mizinda ina.
2 Koma pamene Yohane anali m’ndende, anamva za nchito za Khristu, ndipo anatuma ophunzila ake 3 kukamufunsa kuti: “Kodi Mesiya uja amene tikuyembekezela ndinu, kapena tiyembekezelebe wina?” 4 Poyankha Yesu anawauza kuti: “Pitani mukamuuze Yohane zimene mukumva na kuona: 5 Tsopano akhungu akuona, olemala akuyenda, akhate akuyeletsedwa, ogontha akumva, akufa akuukitsidwa, ndipo osauka akuuzidwa uthenga wabwino. 6 Wodala ni munthu amene sapeza copunthwitsa mwa ine.”
7 Pamene ophunzila a Yohane anali kubwelela, Yesu anayamba kulankhula na khamu la anthulo za Yohane kuti: “Kodi munapita ku cipululu kukaona ciyani? Kodi munapita kukaona bango logwedezeka na mphepo? 8 Nanga munapita kukaona ciyani? Munthu wovala zovala zapamwamba?* Iyai, anthu ovala zovala zapamwamba amapezeka m’nyumba za mafumu. 9 Ndiye n’cifukwa ciyani munapita kumeneko? Kukaona mneneli? Inde, nikukuuzani kuti iye amaposanso mneneli. 10 Uyu ni amene Malemba amati za iye: ‘Taona! Nikutumiza mthenga wanga patsogolo pako, amene adzakukonzela njila!’ 11 Ndithu nikukuuzani kuti pa anthu onse obadwa kwa akazi, sipanabadwepo aliyense wamkulu kuposa Yohane M’batizi. Koma wocepelapo mu Ufumu wa kumwamba ni wamkulu kuposa iye. 12 Kuyambila m’masiku a Yohane M’batizi mpaka pano, anthu akhala akulimbikila kuti apeze mwayi wokaloŵa mu Ufumu wa kumwamba. Ndipo amene akucita khama akuupeza. 13 Pakuti zonse, zolemba za aneneli komanso Cilamulo, zinalosela mpaka nthawi ya Yohane. 14 Kaya mukhulupilila kapena ayi, iye ndiye ‘Eliya amene aneneli anakamba kuti adzabwela.’ 15 Ali na matu amve.
16 “Kodi m’badwo uwu niuyelekezele na ndani? Uli ngati ana aang’ono opezeka m’misika amene akuitana anzawo oseŵela nawo 17 kuti: ‘Tinakuimbilani citolilo, koma inu simunavine. Tinalila mokweza, koma inu simunadzigugude pa cifuwa pomva cisoni.’ 18 Mofananamo, Yohane anabwela ndipo sanali kudya kapena kumwa, koma anthu anali kunena kuti, ‘Iye ali na ciŵanda.’ 19 Mwana wa munthu anabwela ndipo amadya na kumwa, koma anthu amati, ‘Taonani! Munthu wosusuka komanso wokonda kumwa vinyo, bwenzi la okhometsa misonkho na ocimwa.’ Mulimonsemo, nzelu imatsimikizilika kuti ni yolungama mwa nchito zake.”*
20 Kenako anayamba kudzudzula mizinda imene anacitamo nchito zamphamvu zambili cifukwa sinalape. 21 Anati: “Tsoka kwa iwe Korazini! Tsoka kwa iwenso Betsaida! Cifukwa nchito zamphamvu zomwe zinacitika mwa inu zikanacitika ku Turo na ku Sidoni, anthu kumeneko akanalapa kale-kale, ndipo akanavala masaka aciguduli n’kukhala pa phulusa. 22 Koma ine nikukuuzani kuti, cilango ca Turo na Sidoni pa Tsiku la Ciweluzo, cidzakhala cocepelako poyelezekela na canu. 23 Ndipo iwe Kaperenao, kodi mwina udzakwezedwa kumwamba? Ayi udzatsikila ku Manda,* cifukwa nchito zamphamvu zimene zinacitika mwa iwe zikanacitikila ku Sodomu, mzindawo ukanakhalapobe mpaka lelo. 24 Koma nikukuuzani kuti cilango ca Sodomu pa Tsiku la Ciweluzo cidzakhala cocepelako poyelekezela na ca Kaperenao.”
25 Panthawiyo Yesu anati: “Nikukutamandani inu Atate, Ambuye wa kumwamba na dziko lapansi, cifukwa zinthu zimenezi mwazibisa kwa anthu anzelu komanso ophunzila kwambili, koma mwaziulula kwa ana aang’ono. 26 Inde Atate, cifukwa munaona kuti zimenezi ndiye zili bwino. 27 Atate wanga wapeleka zinthu zonse kwa ine, ndipo palibe amene akumudziŵa bwino Mwana kupatulapo Atate. Palibenso amene akuwadziŵa bwino Atate kupatulapo Mwana, komanso aliyense amene Mwanayo wafuna kumuululila za Atatewo. 28 Bwelani kwa ine inu nonse ogwila nchito zolemetsa komanso inu olemedwa, ndipo ine nidzakutsitsimutsani. 29 Nyamulani joko yanga na kuphunzila kwa ine, cifukwa ndine wofatsa komanso wodzicepetsa, ndipo mudzatsitsimutsidwa. 30 Cifukwa joko yanga ni yosavuta kunyamula, ndipo katundu wanga ni wopepuka.”