LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g20 na. 3 masa. 14-15
  • Mankhwala Amene Adzathetselatu Tsankho

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mankhwala Amene Adzathetselatu Tsankho
  • Galamuka!—2020
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • Boma Labwino Koposa
  • 1. Lidzapeleka Maphunzilo Abwino Kwambili
  • 2. Lidzathetsa Zinthu Zopanda Cilungamo
  • 3. Mtsogoleli Wake Adzakhala Wacilungamo
  • 4. Lidzagwilizanitsa Anthu Onse
  • Tsankho—Kodi Na Imwe Muli Nalo?
    Galamuka!—2020
  • Tikhale Amodzi, Monga Mmene Yehova na Yesu Alili Amodzi
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
Galamuka!—2020
g20 na. 3 masa. 14-15
Gulu la anthu a zaka komanso mitundu yosiyana-siyana likumwetulila.

Mankhwala Amene Adzathetselatu Tsankho

Anthu mamiliyoni aseŵenzetsa mfundo zimene zafotokozedwa m’nkhani zapita, ndipo zawathandiza kwambili kuthetsa tsankho mu mtima mwawo. Koma kukamba zoona, mwa mphamvu zathu sitingakwanitse kuthetselatu tsankho. Kodi izi zitanthauza kuti tsankho silikatha mpaka kale-kale?

Boma Labwino Koposa

Maboma a anthu alephela kuthetsa tsankho. Koma kodi zimenezi zitanthauza kuti palibe boma limene lingakwanitse kuthetsa tsankho?

Kuti boma likwanitse kuthetsa tsankho, lingafunike:

  1. 1. Kulimbikitsa anthu kusintha maganizo awo komanso mmene amaonela anthu ena.

  2. 2. Kuthetsa zinthu zopanda cilungamo zimene zimasonkhezela tsankho pakati pa anthu.

  3. 3. Kukhala na olamulila acilungamo amene alibiletu tsankho.

  4. 4. Kugwilizanitsa anthu a mitundu yonse.

Baibo imatitsimikizila kuti Mulungu anapanga boma laconco. Limachedwa “Ufumu wa Mulungu.”—Luka 4:43.

Onani zimene boma limenelo lidzacitila nzika zake:

1. Lidzapeleka Maphunzilo Abwino Kwambili

“Anthu okhala panthaka ya dzikolo adzaphunzila cilungamo.”—YESAYA 26:9.

“Nchito ya cilungamo ceni-ceni idzakhala mtendele, ndipo zocita za cilungamo ceni-ceni zidzakhala bata ndi mtendele mpaka kale-kale.”—YESAYA 32:17.

Kodi malembawa atanthauza ciani? Ufumu wa Mulungu udzaphunzitsa anthu kucita zabwino. Anthu akadziŵa coyenela na cosayenela, colungama na cosalungama, amasintha mmene amaonela wina na mnzake. Aliyense adzadziŵa kuti ayenela kukonda anthu a mitundu yonse.

2. Lidzathetsa Zinthu Zopanda Cilungamo

Mulungu “adzapukuta misozi yonse m’maso mwawo, ndipo imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulila, kapena kubuula, ngakhale zopweteka. Zakalezo zapita.”—CHIVUMBULUTSO 21:4.

Kodi lembali litanthauza ciani? Ufumu wa Mulungu udzathetsa mavuto onse obwela cifukwa ca zinthu zopanda cilungamo zimene anthu amacita. Anthu sadzakhalanso pa udani cifukwa ca zinthu zopanda cilungamo zimene ena anawacitila.

3. Mtsogoleli Wake Adzakhala Wacilungamo

“Sadzaweluza potengela zimene wangoona ndi maso ake, kapena kudzudzula potengela zimene wangomva ndi makutu ake. Adzaweluza mwacilungamo anthu onyozeka ndipo adzadzudzula anthu mowongoka mtima, pothandiza ofatsa a padziko lapansi.”—YESAYA 11:3, 4.

Kodi lembali litanthauza ciani? Yesu Khristu, Mfumu ya Ufumu wakumwamba wa Mulungu, adzalamulila dziko lapansi mwacilungamo komanso mopanda tsankho. Yesu sakonda mtundu wina kuposa unzake, ndipo adzaonetsetsa kuti anthu onse padziko lapansi akutsatila malamulo ake olungama.

4. Lidzagwilizanitsa Anthu Onse

Ufumu wa Mulungu umaphunzitsa anthu kuti akhale “ndi maganizo amodzi, ndi cikondi cofanana. [Akhalenso] ogwilizana mu mzimu umodzi ndi mtima umodzi.”—AFILIPI 2:2.

Kodi lembali litanthauza ciani? Mgwilizano umene nzika za Ufumu wa Mulungu zidzakhala nawo udzakhala weni-weni. Adzakhala ‘ogwilizana ndi mtima umodzi’ cifukwa adzakhala okondana na mtima wonse.

Kodi zingathekedi kukhala na boma laconco?

Inde, n’zotheka. Kuti mukhulupilile zimenezi, mufunika kupenda umboni umene ulipo. Tikupemphani kuti mupende maumboni amenewo mwa kucita zinthu zitatu izi:

  • Pemphani wa Mboni za Yehova kuti akuuzeni umboni woonetsa kuti posacedwa Ufumu wa Mulungu udzakwanilitsa malonjezo a m’Baibo.

  • Loŵani pa jw.org ku Chichewa na kupita pa mbali yakuti ZIMENE BAIBULO IMAPHUNZITSA > KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO > UFUMU WA MULUNGU.

  • Pitani ku misonkhano ya Mboni za Yehova kuti mukadzionele mwekha cikondi na mgwilizano zimene zili pakati pawo.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani