LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • gf phunzilo 9 tsa. 15
  • Kodi Anzake a Mulungu ni Andani?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Anzake a Mulungu ni Andani?
  • Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Nkhani Zofanana
  • Mmene Angelo Angakuthandizileni
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Zoona Zake Ponena za Angelo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Tengelani Citsanzo ca Angelo Okhulupilika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Ndani Amene Ali ku Malo a Mizimu?
    Njila ya Kumoyo Wamuyaya—Kodi Mwaipeza?
Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
gf phunzilo 9 tsa. 15

Phunzilo 9

Kodi Anzake a Mulungu ni Andani?

Yesu Khristu ni Mwana wa Mulungu, ndipo ni mnzake wapamtima. Poyamba, Yesu anali kumwamba monga mngelo wamphamvu. (Yohane 17:5) Ndiyeno, anabwela kudzakhala munthu padziko lapansi, kudzaphunzitsa coonadi ponena za Mulungu. (Yohane 18:37) Pambuyo pake, anataya moyo wake waumunthu kuti apulumutse anthu omvela Mulungu ku ucimo na imfa. (Aroma 6:23) Panthawi ino, Yesu ni Mfumu ya Ufumu wa Mulungu. Ufumu umenewo ni boma imene idzabweletsa Paladaiso padziko lapansi pano.—Cibvumbulutso 19:16.

Angelo nawo ni anzake a Mulungu. Angelo sanayambile moyo wawo padziko lapansi. Mulungu anawalengela kumwamba akalibe kupanga dziko lapansi. (Yobu 38:4-7) Angelo aliko mamiliyoni ambili. (Danieli 7:10) Anzake a Mulungu akumwamba amenewa amafuna kuti anthu aphunzile coonadi conena za Yehova.—Cibvumbulutso 14:6, 7.

Mulungu ali na anzake ena padziko lapansi; iye amawaitana kuti mboni zake. Mboni, ni munthu amene mu khoti amanena zimene adziŵa ponena za munthu kapena cinthu cina. A Mboni za Yehova amauza anthu zimene adziŵa ponena za Yehova na cifunilo cake. (Yesaya 43:10) Mofanana na angelo, a Mboni amafuna kukuthandizani kuti muphunzile coonadi conena za Yehova. Afuna kuti na imwe mukhale mnzake wa Mulungu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani