LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb24 May masa. 8-9
  • June 3-9

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • June 3-9
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2024
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2024
mwb24 May masa. 8-9

JUNE 3-9

MASALIMO 45-47

Nyimbo 27 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Yesu na mkwatibwi wake wophiphilitsa agwilana manja ndipo akuyang’ana dziko lapansi ali kumwamba.

Yesu na mkwatibwi wake, amene ni a 144,000

1. Nyimbo ya Ukwati wa Mfumu

(Mph. 10)

Salimo 45 imakamba za ukwati wa Mfumu Mesiya (Sal. 45:​1, 13, 14; w14-CN 2/15 9-10 ¶8-9)

Ukwati wa Mfumu udzakhalako Aramagedo ikadzacitika (Sal. 45:​3, 4; w22.05 17 ¶10-12)

Anthu onse adzadalitsidwa cifukwa ca ukwati umenewu (Sal. 46:​8-11; it-2-E 1169)


DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi ‘mtima wanga umasangalala kwambili’ kulengeza uthenga wabwino wonena za Mfumu yathu, Yesu Khristu?’—Sal. 45:1.

Amuna na akazi akusangalala m’paradaiso.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Sal. 45:16—Kodi vesiyi itiphunzitsa kuti umoyo udzakhala wotani m’Paradaiso? (w17.04 11 ¶9)

  • Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutigaŵilako?

3. Kuŵelenga Baibo

(Mph. 4) Sal. 45:​1-17 (th Phunzilo 5)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) ULALIKI WAMWAYI. (lmd phunzilo 1 mfundo 3)

5. Nkhani

(Mph. 5) ijwbv 26—Mutu: Kodi Salimo 46:10 itanthauzanji? (th phunzilo 18)

6. Kufotokoza Zimene Mumakhulupilila

(Mph. 4) Citsanzo. g 12/10 22-23—Mutu: Kodi Mumauona Bwanji Mcitidwe wa Mathanyula? (lmd phunzilo 6 mfundo 5)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 131

7. Musaleke Kuonetsana Cikondi mu Ukwati Wanu

(Mph. 10.) Kukambilana.

Cithunzi ca m’vidiyo yakuti “Kuti Banja Likhale Lacimwemwe: Onetsani Cikondi.” Mwamuna akupsopsona mkazi wake atakhala pa benchi.

Phwando la ukwati limakhala cocitika cosangalatsa kwambili. (Sal. 45:​13-15) Kambili, tsiku la cikwati limakhala losangalatsa kwambili kwa okwatilanawo. Koma kodi n’ciyani cingathandize anthu okwatilana kukhalabe acimwemwe pa umoyo wawo wonse?—Mlal. 9:9.

Kuonetsana cikondi ndiye cinsinsi ca ukwati wacimwewe. Anthu okwatilana ayenela kutengela citsanzo ca Isaki na Rabeka. Baibo imatiuza kuti ngakhale patapita zaka 30 mu ukwati wawo, iwo anali kuonetsanabe cikondi cacikulu. (Gen. 26:8) N’ciyani cingathandize anthu ali pa banja kuonetsana cikondi cotelo?

Tambitsani VIDIYO YAKUTI Kuti Banja Likhale Lacimwemwe: Onetsani Cikondi. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi n’ciyani cingapangitse kuti cikondi pakati pa anthu okwatilana ciyambe kucepekela?

  • Kodi mungatani kuti mnzanu wa mu ukwati azimva kuti mumam’konda na kum’samalila?—Mac. 20:35

8. Zofunikila za Mpingo

(Mph. 5)

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) bt mutu. 10 ¶13-21

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 111 na Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani