LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 May masa. 4-5
  • May 12-18

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • May 12-18
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 May masa. 4-5

MAY 12-18

MIYAMBO 13

Nyimbo 34 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Musapusitsidwe ndi “Nyale ya Anthu Oipa”

(Mph. 10)

Anthu oipa alibe ciyembekezo ca tsogolo labwino (Miy. 13:9; w03-CN 9/15 24 ¶5-6)

Musamagwilizane ndi anthu amene angacititse kuti muziona zinthu zoipa ngati zabwino (Miy. 13:20; w12-CN 7/15 12 ¶3)

Yehova amadalitsa munthu wolungama (Miy. 13:25; w04-CN 7/15 31 ¶6)

Zithunzi: Kuyelekezela zisankho zoipa zimene munthu amene si Mboni anapanga ndi zimene a Mboni ena anasankha kucita. 1. Mwamuna akuvina ku naitikilabu atanyamula cakumwa. 2. Pambuyo pake wadwala ndipo akumwa mankhwala. 3. Abale ndi alongo akuceza nthawi yamadzulo. Iwo akuimba nyimbo, akuvina, ndi kudyela pamodzi. 4. Tsiku lotsatila akugwila nchito yolalikila.

Umoyo wa anthu amene amafunafuna zinthu za m’dzikoli sukhaladi wacimwemwe ngati mmene umaonekela. Koma anthu amene amacita zimene Yehova amafuna amakhala ndi umoyo wabwino zedi

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 13:24​—Kodi lembali litiphunzitsa ciyani pa nkhani yoonetsa cikondi komanso kupeleka cilango? (w08-CN 4/1 14 ¶4)

  • Pa kuwelenga Baibulo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibulo

(Mph. 4) Miy. 13:​1-17 (th phunzilo 10)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Yambani mwa kukambilana nkhani imene ili m’kamwam’kamwa, kenako onetsani munthuyo mfundo ya m’Baibulo imene angagwilizane nayo. (lmd phunzilo 2 mfundo 5)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) ULALIKI WAMWAYI. Itanilani munthuyo ku msonkhano. (lmd phunzilo 2 mfundo 3)

6. Nkhani

(Mph. 5) lmd zakumapeto A mfundo 9​—Mutu: Ana Amene Amalemekeza Makolo Awo ndi Kuwamvela, Zinthu Zimawayendela Bwino. (th phunzilo 16)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 77

7. “Kuwala Kwa Nyale ya Anthu Olungama Kukuwonjezeka Kwambili”

(Mph. 8) Kukambilana.

M’mawu a Mulungu muli nzelu zabwino koposa. Tikamawadalila kuti atitsogolele pa umoyo wathu, timakhala ndi umoyo wabwino komanso wacimwemwe. Dziko silingathe kutipatsa zinthu zimenezi.

Cithunzi ca m’vidiyo yakuti “Dzikoli Siingakupatse Zimene Ilibe.” Mlongo Gainanshina wakhala pansi m’munda ndipo akuyang’ana kumwamba.

Tambitsani VIDIYO YAKUTI Dzikoli Siingakupatse Zimene Ilibe. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi nkhani ya mlongo Gainanshina ionetsa bwanji kuti “nyale ya anthu olungama” ndi yabwino kuposa “nyale ya anthu oipa”?​—Miy. 13:9

Musamataye nthawi yanu kulakalaka zinthu za m’dzikoli, kapena kudziimba mlandu cifukwa ca zisankho zimene munapanga kuti mutumikile Yehova. (1 Yoh. 2:​15-17) M’malomwake, muziganizila kwambili nzelu zimene munapeza ‘zomwe n’zamtengo wapatali kwambili.’​—Afil. 3:8.

ZIMENE MUNGACITE PA KULAMBILA KWA PABANJA:

Nthawi ndi nthawi, muzionelela vidiyo imodzi kapena awili pa mavidiyo akuti Coonadi Cimasintha Anthu. Muziganizila mmene vidiyo iliyonse ionetsela ubwino wa coonadi.

8. Zofunikila za Mpingo

(Mph. 7)

9. Phunzilo la Baibulo la Mpingo

(Mph. 30) bt mutu 26 ¶9-17

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 43 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani