LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 May masa. 10-11
  • June 9-15

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • June 9-15
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 May masa. 10-11

JUNE 9-15

MIYAMBO 17

Nyimbo 157 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba(Mph. 10)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Mwamuna ndi mkazi wake mu Isiraeli wakale akudya mkate mu nyumba yawo yaing’ono.

Mwamuna ndi mkazi wake mu Isiraeli akudyela cakudya pamodzi ndipo akukhala mwamtendele

1. Khalani Mwamtendele mu Ukwati Wanu

(Mph. 10)

Kukhala mwamtendele kumafuna khama, koma mukatelo ukwati wanu udzakhala wacimwemwe (Miy. 17:1; onani cithunzi pacikuto)

Pewani kukangana pa nkhani zing’onozing’ono (Miy. 17:9; g-CN 9/14 11 ¶2)

Musalole kuti mkwiyo uzikulamulilani (Miy. 17:14; w08-CN 5/1 10 ¶6–11 ¶1)

Banja lolemela koma losasangalala la m’nthawi za m’Baibulo, lakhala pansi kuti lidye cakudya coculuka. Onse awili akhumata, ndipo mkazi akuyang’ana kumbali mosuliza pamene mwamuna wake akulankhula.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 17:24​—Kodi “maso a munthu wopusa amangoyendayenda mpaka kumalekezelo a dziko lapansi” m’lingalilo lotani? (it-1-E 790 ¶2)

  • Pa kuwelenga Baibulo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibulo

(Mph. 4) Miy. 17:​1-17 (th phunzilo 10)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) ULALIKI WAMWAYI. (lmd phunzilo 3 mfundo 5)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) ULALIKI WAPOYELA. M’pempheni kuti muziphunzila naye Baibulo. (lmd phunzilo 6 mfundo 4)

6. Nkhani

(Mph. 5) ijwbv nkhani 60​—Mutu: Kodi Miyambo 17:17 itanthauza ciyani? (th phunzilo 13)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 113

7. Kulitsani Makhalidwe Othandiza Kuti Muzikambilana Bwino

(Mph. 15) Kukambilana.

Kukambilana bwino n’kofunika kuti banja likhale lacimwemwe. Ngati anthu m’banja amakambilana momasuka angathandizane kukwanilitsa zolinga zawo, komanso angamathandizane panthawi ya mavuto (Miy. 15:22) Kodi mungacite ciyani kuti muthandize aliyense m’banja lanu kukhala womasuka kuti afotokoze maganizo ake komanso mmene akumvela?

Muzicitila zinthu pamodzi. (Deut. 6:​6, 7) Mabanja akamagwilila nchito pamodzi, kucitila zauzimu pamodzi, komanso kucita zosangalatsa pamodzi, cikondi cawo cimakula komanso amakhulupililana kwambili. Kucita izi kumawapatsanso mipata yokambilana momasuka. Nthawi zina, mungafunike kucita zinthu zimene a m’banja lanu akufuna m’malo mocita zimene inu mufuna. Koma kucita izi kumakhala ndi zotulukapo zabwino kwambili! (Afil. 2:​3, 4) Kodi mungacite ciyani kuti muzigwilitsa nchito bwino nthawi imene mumacitila zinthu limodzi ndi a m’banja lanu?​—Aef. 5:​15, 16.

Cithunzi ca m’vidiyo yakuti “Zofunikila Kuti M’banja Mukhale Mtendele​​—Kukambilana Momasuka.” Banja likudyela cakudya pamodzi.

Tambitsani VIDIYO yakuti Zofunikila Kuti M’banja Mukhale Mtendele​—Kukambilana Momasuka. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi kugwilitsa nchito zipangizo zamakono molakwika kungalepheletse bwanji anthu m’banja kulankhulana momasuka?

  • Kodi mwaphunzila ciyani mu vidiyo iyi pa nkhani ya kulankhulana bwino?

Muziwamvetsela. (Yak. 1:19) Nthawi zambili ana amakhala omasuka kufotokoza maganizo awo ngati akudziwa kuti makolo awo adzawamvetsela ndipo sadzakwiya. Conco, muziyesetsa kukhala wodekha ngati mwana wanu wakamba cina cake cimene cakudetsani nkhawa. (Miy. 17:27) Muzimumvetsela mokoma mtima. Yesani kumvetsela maganizo ake komanso mmene akumvela kuti mumuthandize komanso kumulimbikitsa mwacikondi.

8. Phunzilo la Baibulo la Mpingo

(Mph. 30) bt mutu 27 ¶19-22, bokosi patsamba 212

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 35 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani