LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 May masa. 12-13
  • June 16-22

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • June 16-22
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 May masa. 12-13

JUNE 16-22

MIYAMBO 18

Nyimbo 90 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Muzilankhula Mawu Olimbikitsa kwa Amene Akudwala

(Mph. 10)

Muzilola nzelu za Mulungu kukuthandizani kudziwa zoyenela kukamba (Miy. 18:4; w22.10 22 ¶17)

Muziyesa kumvetsa zimene munthuyo akukumana nazo (Miy. 18:13; mrt-CN nkhani 19 bokosi)

Khalani bwenzi lothandiza komanso loleza mtima (Miy. 18:24; wp23.1 14 ¶3–15 ¶1)

Mwamuna akumvetsela mwachelu pamene mkazi wake akufutokoza mmene akumvela.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi ndingatani kuti ndithandize mnzanga wa mu ukwati ngati akudwala kapena ali ndi matenda a maganizo?’

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 18:18​—N’cifukwa ciyani m’nthawi za m’Baibulo anthu anali kugwilitsa nchito maele? (it-2-E 271-272)

  • Pa kuwelenga Baibulo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibulo

(Mph. 4) Miy. 18:​1-17 (th phunzilo 11)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 1) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Munthuyo akulankhula cinenelo cina. (lmd phunzilo 2 mfundo 5)

5. Kubwelelako

(Mph. 3) ULALIKI WAPOYELA. Munthuyo wakuuzani kuti mukambe mwacidule. (lmd phunzilo 7 mfundo 4)

6. Kubwelelako

(Mph. 3) ULALIKI WAMWAYI. Phunzitsani munthuyo mfundo yofunika ya coonadi cokhudza Ufumu wa Mulungu (lmd phunzilo 9 mfundo 5)

7. Kufotokoza Zimene Mumakhulupilila

(Mph. 4) Citsanzo. Ijwfq-CN nkhani 29​—Mutu: Kodi Mumakhulupilila Kuti Dziko Linalengedwa m’Masiku 6 Enieni? (lmd phunzilo 5 mfundo 5)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 144

8. Thandizani Okondedwa Anu Kuyandikila Yehova Popanda Mawu

(Mph. 15) Kukambilana.

Ambili a ife tidziwako munthu wina wake amene pali pano sakutumikila Yehova. Munthuyo angakhale mnzathu wa mu ukwati, mwana wathu, kapena mnzathu wapamtima amene anasiya kutumikila Yehova. Kodi munakakamizapo munthu, ngakhale kufika pomukalipila, kuti ayambe kutumikila Yehova? Ngakhale kuti zolinga zathu n’zabwino, mawu athu angapangitse kuti zinthu ziipileipile. (Miy. 12:18) Kodi njila yabwino yothandizila anthu otelo ndi iti?

1 Petulo 3:1 imakamba kuti mwamuna wosakhulupilila angakopeke popanda mawu. Ngakhale kuti mwamuna wa mlongo angakane kukambilana naye coonadi ca m’Baibulo, mlongoyo angapitilize kumuthandiza kudziwa Yehova. Makhalidwe ake abwino omwe amaphatikizapo cikondi, kukoma mtima, komanso nzelu, angafewetse mtima wa mwamuna wake. (Miy. 16:23) Khalidwe lathu labwino komanso kukoma mtima kwathu zingacititse kuti okondedwa athu amene satumikila Yehova pali pano akopeke.

Tambitsani VIDIYO yakuti Omenya Nkhondo ya Cikhulupililo Mwacipambano​—Aja Amene Mnzawo wa m’Cikwati si Mboni. Kenako funsani omvela kuti:

    Cithunzi ca m’vidiyo yakuti “Omenya Nkhondo ya Cikhulupililo Mwacipambano​​—Aja Amene Mnzawo wa m’Cikwati si Mboni.” Mlongo Hideko Sasaki.
  • Kodi mwaphunzila ciyani kwa mlongo Sasaki?

  • Cithunzi ca m’vidiyo yakuti “Omenya Nkhondo ya Cikhulupililo Mwacipambano​​—Aja Amene Mnzawo wa m’Cikwati si Mboni.” Mlongo Noriko Ito.
  • Kodi mwaphunzila ciyani kwa mlongo Ito?

  • Cithunzi ca m’vidiyo yakuti “Omenya Nkhondo ya Cikhulupililo Mwacipambano​​—Aja Amene Mnzawo wa m’Cikwati si Mboni.” Mlongo Tomoe Okada.
  • Kodi mwaphunzila ciyani kwa mlongo Okada?

9. Phunzilo la Baibulo la Mpingo

(Mph. 30) bt mutu 27 ¶23-26, mabokosi pa masamba 214, 217

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 60 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani