LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 July masa. 4-5
  • July 14-20

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • July 14-20
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 July masa. 4-5

JULY 14-20

MIYAMBO 22

Nyimbo 79 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Malangizo Anzelu Othandiza Polela Ana

(Mph. 10)

Konzekeletsani ana anu kaamba ka zovuta za pa umoyo (Miy. 22:3; w20.10 27 ¶7)

Yambani kuwaphunzitsa akangobadwa (Miy. 22:6; w19.12 26 ¶17-19)

Muziwalangiza m’njila yacikondi (Miy. 22:15; w06-CN 4/1 9 ¶4)

Mokoma mtima tate akugwilitsa nchito Baibo pophunzitsa mwana wawo. Pa tabuleti ya mwanayo pakuoneka zithunzi zokhudza cisanduliko.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 22:29​—Kodi mwambi umenewu tingaugwilitsile nchito bwanji pa zimene timacita mu mpingo, nanga padzakhala mapindu otani? (w21.08 22 ¶11)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Miy. 22:​1-19 (th phunzilo 10)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. (lmd phunzilo 5 mfundo 4)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) ULALIKI WAMWAYI. Muonetseni mopezela nkhani zothandiza kwa makolo pa jw.org. (lmd phunzilo 1 mfundo 4)

6. Nkhani

(Mph. 5) ijwyp nkhani 100​—Mutu: Kodi Ndingatani Ngati Sindinamvele Lamulo la Makolo Anga? (th phunzilo 20)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 134

7. Khalani Oleza Mtima, Koma Musamalekelele Makhalidwe Oipa

(Mph. 15) Kukambilana.

Kulela ana kumafuna kukhala woleza mtima. Nthawi zonse makolo ayenela kumawamvetsela ana awo ndi kumapatula nthawi yokwanila yoceza nawo. (Deut. 6:​6, 7) Pofuna kudziwa zimene zili mumtima mwa ana awo, makolo ayenela kumawafunsa mafunso ndi kumvetsela mwachelu pamene akufotokoza. (Miy. 20:5) Makolo angafunike kubweleza malangizo awo nthawi zambili kuti ana awo awamvetsetse ndi kuwagwilitsa nchito.

Koma izi sizitanthauza kuti makolo oleza mtima amalekelela makhalidwe oipa. Yehova anapatsa makolo mphamvu zoikila ana awo malile a zimene angacite ndi kuwapatsa cilango cofunikila akaphwanya malamulo.​—Miy. 6:20; 23:13.

Welengani Aefeso 4:31. Kenako funsani omvela kuti:

  • N’cifukwa ciyani makolo sayenela kukhala okwiya pamene akupeleka cilango kwa ana awo?

Welengani Agalatiya 6:7. Kenako funsani omvela kuti:

  • N’cifukwa ciyani m’pofunika kuti makolo azithandiza ana awo kudziwa kuti ngati acita zoipa adzakumana ndi mavuto?

Cithunzi ca mu vidiyo yakuti “‘Moleza Mtima, Pitilizani Kulolelana m’Cikondi’​—Ana Anu.” M’bale Max akumvetsela moleza mtima kwa mwana wake Sue.

Tambitsani VIDIYO YAKUTI ‘Moleza Mtima, Pitilizani Kulolelana m’Cikondi’​—Ana Anu. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi mwaphunzila ciyani mu vidiyo iyi?

8. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr “Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila,” ndi “Matanthauzo a Zinthu Zina Zapadela”

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 95 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani