LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 July masa. 6-7
  • July 21-27

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • July 21-27
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 July masa. 6-7

JULY 21-27

MIYAMBO 23

Nyimbo 97 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Malangizo Anzelu pa Nkhani ya Mowa

(Mph. 10)

Ngati mwasankha kumwa mowa, pewani kumwa kwambili (Miy. 23:​20, 21; w04-CN 12/1 19 ¶5-6)

Muziganizila zotulukapo zoipa za kuledzela (Miy. 23:​29, 30, 33-35; w10-CN 1/1 4 ¶7-5 ¶3)

Musapusitsidwe n’kumaganiza kuti kumwa mowa mwaucidakwa kulibe vuto lililonse (Miy. 23:​31, 32)

Mlongo wakhala pa mpando m’nyumba yake ndipo akuyang’ana botolo la mowa.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 23:21​—Kodi ngati munthu ndi wonenepa kwambili ndiye kuti ndi wosusuka? Fotokozani. (w04-CN 11/1 31 ¶2)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa Mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Miy. 23:​1-24 (th phunzilo 5)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAPOYELA. (lmd phunzilo 3 mfundo 5)

5. Kubwelelako

(Mph. 5) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Muonetseni mmene phunzilo la Baibo limacitikila. (lmd phunzilo 9 mfundo 5)

6. Kupanga Ophunzila

(Mph. 5) Limbikitsani wophunzila wanu amene akuvutika kusiya khalidwe lina lake limene silikondweletsa Yehova. (lmd phunzilo 12 mfundo 4)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 35

7. Kodi Ndikaikepo Mowa Kapena Ayi?

(Mph. 8) Kukambilana.

Kodi munthu amene wakonza zokhala ndi maceza kapena phwando lina lake, monga la ukwati, ayenela kuikapo mowa? Pambuyo pakuti munthuyo waganizila mosamala mfundo za m’Baibo ndi zinthu zina zofunika, monga cikhalidwe ca kwawo ndi zikumbumtima za anthu ena, ayenela kusankha yekha zocita pa nkhaniyi.

Mwamuna ndi mkazi omwe ali pa citomelo akukambilana ngati angakaikepo mowa kapena ayi pa phwando la ukwati wawo. Pa thebulo pali Baibo yotsegula ndipo pa tabuleti pakuoneka mabotolo a mowa osiyanasiyana.

Tambitsani VIDIYO yakuti Kodi Niikeponso Mowa? Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi mfundo za m’Baibo zotsatilazi, zingathandize bwanji munthu amene akufuna kuitanila anthu kumaceza kudziwa ngati angaikepo mowa kapena ayi?

    • Yoh. 2:9​—Yesu anasandutsa madzi kukhala vinyo pa phwando la ukwati.

    • 1 Akor. 6:10​—‘Zidakwa . . . sizidzalowa mu ufumu wa Mulungu.’

    • 1 Akor. 10:​31, 32​—“Kaya mukudya kapena kumwa . . . , muzicita zinthu zonse kuti zibweletse ulemelelo kwa Mulungu. Muzipewa kukhumudwitsa” ena.

  • Kodi ndi zinthu ziti zimene muyenela kuganizila?

  • N’cifukwa ciyani tiyenela kusewenzetsa “luso la kuganiza” kuti tione mmene tingagwilitsile nchito mfundo zosiyanasiyana za m’Baibo?​—Aroma 12:1; Mlal. 7:​16-18

8. Zofunikila za Mpingo

(Mph. 7)

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 1 ¶1-7 ndi vidiyo ya zimene zili mmutu 1.a

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 37 ndi Pemphelo

a Ngati pa phunzilo paikidwa vidiyo yofotokoza zimene zili mmutuwo, coyamba onetsani vidiyoyo musanayambe kukambilana ndime.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani