LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 July masa. 8-9
  • July 28–August 3

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • July 28–August 3
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 July masa. 8-9

JULY 28–AUGUST 3

MIYAMBO 24

Nyimbo 38 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Konzekelani Pasadakhale Kulimbana ndi Zovuta

(Mph. 10)

Muziphunzila Baibo kuti muwonjezele cidziwitso canu (Miy. 24:5; w23.07 18 ¶15)

Mukakumana ndi zolefula musaleke kucita zinthu zauzimu (Miy. 24:10; w09-CN 10/15 12)

Kukhala wolimba mwauzimu kudzatithandiza kupezanso mphamvu tikakumana ndi zovuta (Miy. 24:16; w20.12 15)

Mlongo yemwe akudwala matenda aakulu, akucita ulaliki wa kunyumba ndi nyumba mosangalala ndi mnzake. Akuonetsa mzimayi wina zina zake pa tabuleti.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 24:27​—Kodi mwambi uwu utiphunzitsa ciyani? (w09-CN 12/15 18 ¶12-13)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Miy. 24:​1-20 (th phunzilo 11)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAMWAYI. Makambilano atha musanamulalikile n’komwe. (lmd phunzilo 2 mfundo 4)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. (lmd phunzilo 3 mfundo 4)

6. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) ULALIKI WAPOYELA. Muuzeni za pulogilamu yathu yophunzitsa Baibo ndi kumusiyila kakhadi kopemphela phunzilo la Baibo. (lmd phunzilo 4 mfundo 3)

7. Nkhani

(Mph. 3) lmd zakumapeto A mfundo 11​—Mutu: Mulungu Anatipatsa Uthenga Wofunika Kwambili. (th phunzilo 6)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 99

8. Tizithandizana pa Nthawi ya Mavuto

(Mph. 15) Kukambilana.

Mwadzidzidzi kungabuke matenda ena ake, kungacitike masoka azacilengedwe, cipolowe, nkhondo kapena tingayambe kuzunzidwa. Zaconco zikacitika, abale ndi alongo athu amene akumana ndi mavuto amenewa amathandizana ndi kulimbikitsana. Komabe, ngakhale zitakhala kuti mavutowa sanacitikile ife, timakhudzidwa ndi zimene zacitikila Akhristu anzathu, ndipo timacita zilizonse zotheka kuti tiwathandize.​—1 Akor. 12:​25, 26.

Cithunzi: Abale ndi alongo akuthandiza Akhristu anzawo m’njila zosiyanasiyana. 1. Abale ndi alongo akumanganso Nyumba ya Ufumu imene inaonongeka pa nthawi ya tsoka la cilengedwe. 2. Abale ndi alongo mwacikondi akulandila mlongo ndi mwana wake amene anathawa kwawo. 3. Mlongo akucita copeleka mu kabokosi ka zopeleka ku Nyumba ya Ufumu. 4. Abale ndi alongo ali pa Nyumba ya Ufumu ndipo akupeleka zofunikila kwa Akhristu anzawo amene anathawa kwawo. 5. Abale ndi alongo odzipeleka akupeleka madzi a m’mabotolo. 6. M’bale akupemphela.

Welengani 1 Mbiri 13:6 ndi Yakobo 5:16b. Kenako funsani omvela kuti:

  • N’cifukwa ciyani mapemphelo amene atumiki a Mulungu amapeleka popemphelela ena amakhala amphamvu?

Welengani Maliko 12:42-44 ndi 2 Akorinto 8:1-4. Kenako funsani omvela kuti:

  • Ngakhale titakhala ndi ndalama zocepa ndipo tilibe zambili zopeleka pa nchito ya padziko lonse yothandiza abale athu amene akukumana ndi mavuto, n’cifukwa ciyani sitiyenela kuleka kucita zopeleka?

Tambitsani VIDIYO yakuti Kulimbikitsa Abale pa Nthawi ya Ciletso. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi abale anadzimana ciyani kuti athandize Akhristu anzawo omwe anali kukhala kudela komwe nchito yathu inali yoletsedwa?

  • Pa nthawi ya ciletso, kodi abale anacita ciyani kuti atsatile lamulo loti azisonkhana pamodzi komanso kulimbikitsana?​—Aheb. 10:​24, 25

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 1 ¶8-14 ndi bokosi 1A

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 40 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani