LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 September masa. 10-11
  • October 6-12

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • October 6-12
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 September masa. 10-11

OCTOBER 6-12

MLALIKI 5-6

Nyimbo 42 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Aisiraeli ali pafupi ndi geti la mzinda, iwo akumvetsela pamene wansembe akulankhula. Wansembeyo wanyamula mpukutu.

Aisiraeli akumvetsela mwachelu pamene wansembe akuwafotokozela mawu a m’Cilamulo

1. Mmene Timaonetsela Ulemu Waukulu kwa Mulungu Wathu Wamkulu

(Mph. 10)

Timaonetsa ulemu pamisonkhano yathu mwa kumvetsela komanso kuvala ndi kudzikongoletsa moyenela (Mla. 5:1; w08-CN 8/15 15-16 ¶17-18)

Tikamapeleka pemphelo pamisonkhano, mapemphelo athu azikhala oonetsa ulemu osati ongoculukitsa mawu (Mla. 5:2; w09-CN 11/15 11 ¶21)

Timakwanilitsa lonjezo lathu la kudzipatulila (Mla. 5:​4-6; w17.04 6 ¶12)

Abale ndi alongo amisinkhu yosiyanasiyana akumvetsela mwachelu pamsonkhano m’Nyumba ya Ufumu.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Mla. 5:8​—Kodi lembali lingatilimbikitse bwanji tikamacitilidwa zinthu zopanda cilungamo? (w20.09 31 ¶3-5)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Mla. 5:​1-17 (th phunzilo 12)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 1) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Munthuyo akungofuna kukangana nanu. (lmd phunzilo 4 mfundo 5)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAMWAYI. Kambilanani naye imodzi mwa “Mfundo za m’Baibo Zimene Timafunitsitsa Kuphunzitsa Anthu” zopezeka pa zakumapeto A m’kabuku ka Kondani Anthu. (lmd phunzilo 1 mfundo 3)

6. Kubwelelako

(Mph. 3.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Muonetseni vidiyo ya m’thuboksi yathu. (lmd phunzilo 7 mfundo 3)

7. Kupanga Ophunzila

(Mph. 5) lff phunzilo 17, mawu oyamba, komanso mfundo 1-3 (lmd phunzilo 11 mfundo 3)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 160

8. Kodi Mumagwilitsa Nchito Mbali Yakuti “Mfundo za m’Baibo Zimene Timafunitsitsa Kuphunzitsa Anthu”?

(Mph. 15) Kukambilana.

Mwamuna ndi mkazi wake akucita ulaliki wa kunyumba ndi nyumba ndipo akuwelengela mnyamata wina lemba.

Kungocokela pamene kabuku kakuti Kondani Anthu Kuti Mupange Ophunzila kanatulutsidwa, katithandiza kuonjezela luso lathu lokambilana ndi anthu. Mbali ya zakumapeto A inapangidwa kuti izitithandiza kuuzako ena coonadi ca m’Baibo cosavuta kumva pamene tikuceza ndi anthu. (Ahe. 4:12) Kodi mumaidziwa bwino mitu yonse 9 yopezeka pa mbali yakuti “Mfundo za m’Baibo Zimene Timafunitsitsa Kuphunzitsa Anthu”?

  • Tikamaceza ndi anthu, kodi tingacite ciyani kuti tiwauzeko coonadi ca m’Baibo cosavuta kumva pa nthawi yoyenela?​—lmd zakumapeto A

  • Ndi nkhani ziti zimene anthu a m’gawo lanu amacita nazo cidwi kwambili?

  • Mungacite ciyani kuti muwadziwe bwino Malemba amene ali pa zakumapeto A?

COLINGA:

Yesani kuloweza lemba limodzi pa nkhani iliyonse yopezeka pa zakumapeto A. Yambani ndi Malemba opezeka pa nkhani zimene anthu a m’dela lanu angacite nazo cidwi kwambili.

Tikamagwilitsa nchito Malemba amenewa kawilikawili mu utumiki, m’pamenenso tidzawadziwa bwino. Koma kuti tigwilitse nchito malembawa mu utumiki coyamba tifunika kukambilana ndi anthu a m’gawo lathu.

Onetsani VIDIYO yakuti “Citsulo Cimanola Citsulo Cinzake”​—Kufikila Anthu Ambili. kenako funsani omvela kuti:

  • N’ciyani cingatithandize kuti tizikambilana ndi anthu oculuka m’gawo lathu?

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 4 ¶10-17

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 1 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani