LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 November masa. 6-7
  • November 17-23

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • November 17-23
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 November masa. 6-7

NOVEMBER 17-23

NYIMBO YA SOLOMO 6-8

Nyimbo 34 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Khalani Khoma, Osati Citseko

(Mph. 10)

Alongo ake a mtsikana wa Cisulami anali kufuna kuti iye akhalebe woyela (Nyimbo 8:​8, 9; w15 1/15 32 ¶15-16)

Iye anapeza mtendele cifukwa cakuti anakhalabe woyela (Nyimbo 8:10; yp-E 188 ¶2)

Pankhani yokhalabe woyela, mtsikanayu ndi citsanzo cabwino kwa acinyamata (yp2-CN 33)

Amuna atatu Aciisiraeli aimilila kutsogolo kwa khoma atapinda manja awo.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi ndingathandize bwanji Akhristu a mumpingo mwathu amene ndi mbeta kukhala khoma, osati citseko?’

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Nyimbo 8:6​—N’cifukwa ciyani cikondi ceniceni cimachedwanso “lawi la Ya”? (w15 1/15 29 ¶3)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Nyimbo 7:​1-13 (th phunzilo 12)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Gwilitsani nchito kakhadi kolowela pawebusaiti ya jw.org poyambitsa makambilano. (lmd phunzilo 4 mfundo 4)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAPOYELA. Gwilitsani nchito thilakiti poyambitsa makambilano m’gawo la malonda. (lmd phunzilo 1 mfundo 4)

6. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAMWAYI. Yambani kukambilana naye mwaubwenzi, koma makambilanowo athe musanamulalikile. (lmd phunzilo 2 mfundo 4)

7. Kufotokoza Zimene Mumakhulupilila

(Mph. 5) Citsanzo. ijwfq nkhani 43​—Mutu: Kodi a Mboni za Yehova Amatsatila Mfundo Ziti pa Nkhani Yokhala ndi Cibwenzi? (th phunzilo 7)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 121

8. Thawani Ciwelewele

(Mph. 15) Kukambilana.

M’buku la Nyimbo ya Solomo, m’busa anaitana mtsikana wa Cisulami kuti apite naye kokayenda. (Nyimbo 2:​10-14) Ngakhale kuti zolinga za m’busa wacinyamatayo zinali zabwino, alongo ake a mtsikana wa Cisulami anacita zinthu mwanzelu. Anamupatsa nchito yoti agwile n’colinga coti asapite kokayendako. (Nyimbo 2:15) Alongo akewo anadziwa kuti akanamulola kupita kokayenda ndi wokondedwa wake kumalo kwaokha, zikanawacititsa kuti agwele m’mayeselo.

Baibo imalangiza Akhristu kuti ayenela ‘kuthawa ciwelewele.’ (1 Akor. 6:18) Tiyenela kupewa zilizonse zimene zingatigwetsele m’chimo la ciwelewele. Wolemba buku la Nyimbo ya Solomo analembanso kuti: “Munthu wocenjela akaona tsoka amabisala, koma wosadziwa zinthu amangopitabe ndipo amakumana ndi mavuto.”​—Miy 22:3.

Onetsani VIDIYO yakuti Mulungu “Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.” Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi mwaphunzila ciyani mu vidiyo iyi?

    Cithunzi cocokela mu vidiyo yakuti “Mulungu ‘Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.’ ” M’bale walandila meseji misonkhano ili mkati.
    Cithunzi cocokela mu vidiyo yakuti “Mulungu ‘Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.’ ” M’bale wakhala pafupi ndi mtsikana kusukulu ndipo mtsikanayo wagwila dzanja lake.
    Cithunzi cocokela mu vidiyo yakuti “Mulungu ‘Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.’ ” M’bale akukambilana ndi makolo ake pa nthawi ya cakudya.

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 6 ¶14-19

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 143 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani