LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 5/1 tsa. 32
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • N’cifukwa Ciani Mulungu Amalolela Kuti Anthu Azivutika?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli?
    Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli
  • N’cifukwa Ciani Pa Dziko Pali Mavuto Ambili Conco?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • N’cifukwa Ciani Mulungu Amalolela Kuti Anthu Azivutika?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 5/1 tsa. 32

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi ndani kwenikweni akulamulila dzikoli?

Anthu ambili amakhulupilila kuti Mulungu woona ndiye akulamulila dziko. Ngati zimenezi n’zoona, kodi m’dziko mukanakhala mavuto ambili conco? (Deuteronomo 32:4, 5) Baibulo limanena kuti pali wina wake woipa amene akulamulila dzikoli.—Ŵelengani 1 Yohane 5:19.

Kodi woipayo anayamba bwanji kulamulila anthu? Kuciyambi kwa mbili ya anthu, mngelo wina anapandukila Mulungu ndipo anacititsa kuti anthu aŵili oyambilila apandukilenso Mulungu. (Genesis 3:1-6) Anthuwo anasankha kumvela mngelo wochedwa Satana kuti aziwalamulila. Mulungu wamphamvu zonse ndi yekhayo woyenela kulamulila. Koma iye amafuna kuti anthu asankhe ulamulilo wake cifukwa com’konda. (Deuteronomo 6:6; 30:16, 19) Koma n’zacisoni kuti anthu ambili asoceletsedwa mofanana ndi anthu oyambilila.—Ŵelengani Chivumbulutso 12:9.

Kodi ndani adzathetsa mavuto a anthu?

Kodi Mulungu adzalola Satana kupitiliza kulamulila anthu? Iyai. Mulungu adzagwilitsila nchito Yesu kucotsapo zinthu zoipa zimene Satana wabweletsa.—Ŵelengani 1 Yohane 3:8.

Mulungu adzapatsa Yesu mphamvu zoononga Satana. (Aroma 16:20) Ndiyeno, Mulungu adzalamulila anthu ndi kubwezeletsa cimwemwe ndi mtendele monga mmene anafunila paciyambi.—Ŵelengani Chivumbulutso 21:3-5.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 3 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani