LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb16 September tsa. 7
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Limbikitsani Anthu Acidwi Kupezeka pa Misonkhano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Limbikitsani Anthu Acidwi Kupezeka pa Misonkhano
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Misonkhano ya Mboni za Yehova Ingakupindulileni Motani?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Thandizani Maphunzilo Anu a Baibo Kumapezeka pa Misonkhano
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Maulaliki a Citsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Maulaliki a Citsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
mwb16 September tsa. 7

UMOYO WATHU WACIKHIRISTU

Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Limbikitsani Anthu Acidwi Kupezeka pa Misonkhano

M’bale agaŵila munthu kapepa koitanila ku misonkhano

CIFUKWA CAKE KULI KOFUNIKA: Misonkhano imatipatsa mwayi ‘woimba’ ndi ‘kutamanda’ Yehova. (Sal. 149:1) Pa misonkhano, timaphunzitsidwa kucita cifunilo ca Mulungu. (Sal. 143:10) Anthu acidwi ndiponso amene timaphunzila nawo Baibulo amapita patsogolo mwamsanga akayamba kupezeka pa misonkhano.

COGAŴILA MU OCTOBER: KAPEPALA KOITANILA KU MISONKHANO

Anthu ena atapezeka pa misonkhano kwa nthawi yoyamba, anakamba kuti: “Zoonadi Mulungu ali pakati panu.” (1 Akor. 14:25) M’mwezi wa October, tidzayesetse kuitanila anthu ambili ku misonkhano ya kumapeto kwa mlungu. Tidzagaŵila kapepala koitanila ku misonkhano. Komanso, ngati mwininyumba wavomela, muonetseni vidiyo yakuti N’ciani Cimacitika ku Nyumba ya Ufumu?

MMENE TINGACITILE:

  • Itanilani munthu wacidwi ku misonkhano mwamsanga. Musayembekezele kuti mukhazikitse phunzilo la Baibulo.—Chiv. 22:17

  • Mboni za Yehova ziloŵa m’Nyumba ya Ufumu

    Fotokozelani munthu wacidwi zimene zimacitika ku misonkhano ndi zimene tidzaphunzila pa msonkhano wotsatila. Mungaseŵenzetse zinthu zotsatilazi: Kapepala koitanila ku misonkhano, vidiyo yakuti N’ciani Cimacitika ku Nyumba ya Ufumu?, ndi kabuku ka Cifunilo ca Yehova, phunzilo 5 ndi 7

  • M’bale aŵelenga Baibulo lake pamodzi na munthu wacidwi

    M’thandizeni. Kodi munthuyo afunika kukamutenga kapena kumuthandiza kusankha zovala zoyenelela? Khalani naye pafupi pa misonkhano, ndipo muzionela pamodzi mabuku amene mukuseŵenzetsa. Mudziŵikitseni kwa ena

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani