LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 December masa. 26-30
  • Inu Okalamba, Ndinu Ofunika Kwambili Mumpingo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Inu Okalamba, Ndinu Ofunika Kwambili Mumpingo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • ZIMENE YEHOVA AMAFUNA KUTI MUZICITA
  • MUNGAWATHANDIZE KWAMBILI ANTHU ENA
  • YEHOVA AMAYAMIKILA UTUMIKI WANU
  • KHALANI NDI ZOCITA ZAMBILI MMENE MUNGATHELE
  • Pezani Cimwemwe Popatsa Yehova Zabwino Zimene Mungathe Pacanu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Muziona Okalamba Okhulupilika Kuti ni Ofunika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2021
  • Tumikilani Yehova Asanafike Masiku Oipa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Kodi Mudzalola Yehova Kukucititsani Kukhala Ndani?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 December masa. 26-30
Zithunzi: Abale ndi alongo acikulile akusangalala potumikila Yehova. 1. M’bale akumwetulila pomwe akuganizila ciyembekezo ca tsogolo labwino cimene ali naco. 2. Mlongo yemwe ali pa njinga ya olemala akugawila kathilakiti kwa munthu amene amasewenza pa cipatala. 3. Mlongo akupeleka ndemanga pa msonkhano wa mpingo. 4. Mlongo wagwila dzanja la m’bale wacinyamata pomwe akulalikila limodzi. 5. M’bale akuceza m’Nyumba ya Ufumu ndi acicepele awili limodzi ndi mai ao.

Inu Okalamba, Ndinu Ofunika Kwambili Mumpingo

“Ndimadabwa ndikaganizila kuculuka kwa zinthu zimene ndinali kukwanitsa kucita ndili mtsikana. Koma popeza tsopano ndakalamba, sindikukwanitsanso kucita zinthu zimenezo.”​—Connie, wa zaka 83.

Mwina inunso mukulephela kucita zinthu zina cifukwa cakuti ndinu wokalamba. Ngakhale kuti mwatumikila Yehova kwa zaka zambili, mungayambe kukhala ndi maganizo olefula cifukwa cakuti mukulephela kucita zinthu zina tsopano. Mwacitsanzo, mungayambe kuyelekezela zimene mukucita pali pano ndi zimene munali kucita m’mbuyomo. Ngati n’conco, n’ciani cimene cingakuthandizeni kupewa maganizo otelo?

ZIMENE YEHOVA AMAFUNA KUTI MUZICITA

Dzifunseni kuti, ‘Kodi Yehova amafuna kuti ndizicita ciani?’ Mau a pa Deuteronomo 6:5 angakulimbikitseni kwambili. Amati: “Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, moyo wanu wonse ndi mphamvu zanu zonse.”

Malinga ndi lembali, Yehova amafuna kuti muzim’tumikila ndi mtima wanu wonse, moyo wanu wonse, ndi mphamvu zanu zonse. Mfundoyi ingakuthandizeni kupewa kudziyelekezela ndi anthu ena. Ingakuthandizeninso kupewa kuyelekezela zimene mumacita palipano ndi zimene munali kucita kale.

Ganizilani izi: Kodi munali kum’patsa zotani Yehova muli wacinyamata? Atumiki ambili a Yehova anganene kuti anali kum’patsa zabwino koposa. Munali kum’patsa zabwino koposa malinga ndi mmene zinthu zinalili pa nthawiyo. Nanga tsopano mukutha kum’patsa zotani Yehova? Mwacionekele, panopa mukucita zonse zotheka kuti mum’patse zabwino koposa malinga ndi mmene zinthu zili kwa inu. Mukamaona zinthu mwa njila imeneyi, mudzakhala otsimikiza kuti mofanana ndi kale, mukum’patsa zabwino koposa Yehova. Kalelo munali kum’patsa zabwino koposa ndipo panopa mukupitiliza kutelo.

Zithunzi: Mlongo akutumikila Yehova mokhulupilika kwa zaka zambili. 1. Zaka zambili m’mbuyomo, mlongoyo akulalikila mzimai pocita ulaliki wa nyumba ndi nyumba. 2. Mlongoyu tsopano wakalamba ndipo akucita ulaliki wapafoni ndi mlongo wacitsikana.

Mukamacita zonse zomwe mungathe potumikila Yehova mu ukalamba wanu, mumakhala kuti mukum’patsa zabwino koposa monga mmene munali kucitila pa unyamata wanu

MUNGAWATHANDIZE KWAMBILI ANTHU ENA

M’malo moganizila kwambili zinthu zimene simungathenso kucita, muziganizila zinthu zosiyana-siyana zimene mungacite pothandiza ena. Kunena zoona, pokhala Mkhristu wokalamba, pali zinthu zina zimene mungacite pali pano zimene simukanatha kucita pamene munali wacinyamata. Mwacitsanzo, mungathe kucita zotsatilazi:

Muzifotokozelako ena zimene mudziwa. Ganizilani mau otsatilawa opezeka m’Baibo:

Mfumu Davide anati: “Ndinali mwana ndipo tsopano ndakula koma sindinaonepo munthu aliyense wolungama atasiyidwa, kapena ana ake akupemphapempha cakudya.”​—Sal. 37:25.

Yoswa anati: “Tsopano ine ndatsala pangʼono kufa. Inu mukudziwa bwino ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, kuti palibe mau ngakhale amodzi pa malonjezo onse abwino amene Yehova Mulungu wanu ananena, omwe sanakwanilitsidwe. Onse akwanilitsidwa kwa inu. Palibe ngakhale mau amodzi omwe sanakwanilitsidwe.”​—Yos. 23:14.

N’kutheka kuti munakambako mau ngati amenewa muli wacinyamata. Davide ndi Yoswa anakamba zimenezi cifukwa ca zimene anaona pa zaka zambili zomwe anakhala ndi moyo. Izi n’zimene zinapangitsa mau ao kukhala ogwila mtima.

Ngati mwatumikila Yehova kwa nthawi yaitali, inunso mungafotokozeleko ena mapindu amene mwapeza pocita zimenezi. Kodi mukukumbukilako nthawi pamene munaona Yehova akuthandiza anthu ake m’njila yapadela? Ngati n’telo, muziuzako ena zocitika zimenezi. Kucita zimenezo kungawatsitsimule ndipo inunso kungakutsitsimuleni. Conco, mungalimbikitse abale ndi alongo mwa kuwafotokozelako zinthu zosiyana-siyana zimene mwaona potumikila Yehova.​—Aroma 1:​11, 12.

Ngati n’kotheka, muzipezeka pa misonkhano ya pamaso-m’pamaso. Ndipo iyi ndi njila inanso imene mungalimbikitsile ena. Kucita zimenezi kungakulimbikitseni kwambili, ndipo mungalimbikitsenso abale ndi alongo. Connie, amene tam’chulapo kale, anati: “Kupezeka pa misonkhano kumandithandiza kuti ndisafooke. Ndimalimbikitsidwa cifukwa ku Nyumba ya Ufumu abale ndi alongo amandionetsa cikondi. Ndimapatsako ena timphatso poonetsa kuwayamikila. Conco, ndimayesetsa mmene ndingathele kuti ndiciteko zinthu zauzimu limodzi ndi abale ndi alongo anga.”

YEHOVA AMAYAMIKILA UTUMIKI WANU

M’Malemba muli zitsanzo zambili za anthu amene Yehova anali kuwakonda ngakhale kuti sanali kukwanitsa kucita zambili. Ganizilani za Simiyoni, Mwisiraeli amene anali wokalamba pa nthawi imene Yesu anabadwa. Simiyoni akapezeka pa kacisi, mwina anali kuona acinyamata akugwila nchito zofunika za pa kacisi zimene iye sakanakwanitsa. Izi zikanapangitsa Simiyoni kuona kuti sanali wofunika kweni-kweni pamaso pa Yehova. Koma Yehova sanali kumuona conco. Yehova anaona Simiyoni kuti anali “wolungama komanso wodzipeleka kwa Mulungu.” Ndipo anam’dalitsa mwa kum’patsa mwai woona Yesu ali wakhanda. Anam’patsanso mzimu woyela ndi kum’gwilitsa nchito kulosela kuti khandalo ndi limene lidzakhala Mesiya wolonjezedwa. (Luka 2:​25-35) Conco, n’zoonekelatu kuti Yehova sanangoona ukalamba wa Simiyoni, koma anaonanso cikhulupililo cake colimba.

Mwacimwemwe, Yosefe ndi Mariya akuonetsa Yesu wakhanda kwa Simiyoni.

Yehova anadalitsa Simiyoni mwa kum’patsa mwai woonako Yesu ali wakhanda komanso kum’gwilitsa nchito kulosela kuti khandalo ndi limene lidzakhale Mesiya

Inunso dziwani kuti Yehova amayamikila mukamam’tumikila mokhulupilika ngakhale pamene simungathe kucita zambili. Musaiwale kuti “mphatso yocokela pansi pa mtima ndi imene Mulungu amakondwela nayo cifukwa Mulungu amafuna kuti munthu apeleke zimene angakwanitse, osati zimene sangakwanitse.”​—2 Akor. 8:12.

Conco, muzingocita zimene mungakwanitse. Mwacitsanzo, ganizilani njila zocitila ulaliki zimene mungathe kutengamo mbali, ngakhale kwa nthawi yocepa. Mwina mungalimbikitseko ena mwa kuwatumilako foni kapena kuwalembelako kakalata. Kucita zinthu ngakhale zing’ono-zing’ono zoonetsa cikondi, kungawalimbikitse kwambili alambili anzathu maka-maka ngati amene wacita zinthuzo ndi munthu amene watumikila Yehova kwa nthawi yaitali.

Ena amalephela kucita zambili cifukwa ca mabvuto monga kulemala ndi kudwala. Onani citsanzo ca mlongo wina wa ku East Africa cimene cionetsa kuti anthu otelewa Yehova angawagwilitsebe nchito. Citsanzoci cili m’bokosi la mutu wakuti “Linapulumutsa Moyo Wake.”

Muzikumbukila kuti ena amalimbikitsidwa akaona zaka zimene mwakhala mukutumikila Yehova mokhulupilika. Ndinu citsanzo pa nkhani ya kupilila, ndipo khalani otsimikiza kuti “Mulungu si wosalungama kuti angaiwale nchito yanu ndiponso cikondi cimene munacisonyeza pa dzina lake, potumikila oyela ndipo mukupitiliza kuwatumikila.”​—Aheb. 6:10.

KHALANI NDI ZOCITA ZAMBILI MMENE MUNGATHELE

Kafuku-fuku aonetsa kuti amuna ndi akazi ambili okalamba amene amayesetsa kuthandiza ena, amakhala ndi thanzi labwino, amakwanitsa kuganiza bwino ndiponso amakhala ndi moyo wautali.

Koma kucitila ena zabwino sikungacotseletu mabvuto a ukalamba. Ndi Ufumu wa Mulungu wokha umene udzawathetse. Udzacita izi mwa kucotsapo ucimo umene umabweletsa ukalamba ndi imfa.​—Aroma 5:12.

Ngakhale n’telo, mukapitiliza kutumikila Yehova, kumene kuphatikizapo kuthandiza ena kuti am’dziwe, ciyembekezo canu cidzakhala cowala, ndipo mungakhale ndi thanzi labwino. Inu okalamba, dziwani kuti Yehova amayamikila zimene mumakwanitsa kucita pom’tumikila. Nawonso mpingo umakuyamikilani cifukwa ca cikhulupililo canu.

Mlongo wacikulile akucita ulaliki wa pakasitandi. Akuwelengela lemba mtsikana amene akugwetsa misozi.

Linapulumutsa Moyo Wake

Mtsikana wina anali kudutsa pafupi ndi kasitandi ka ulaliki. Mlongo wacikulile amene anali pakasitandipo atam’patsa moni, anafunsa mtsikanayo ngati angakonde kuti amuwelengeleko lemba lolimbikitsa. Mlongoyo anawelenga lemba la Yeremiya 29:11 limene limanena kuti Yehova akuganiza zotipatsa mtendele osati matsoka. Pambuyo powelenga lembalo, mlongoyo anafunsa kuti, “Kodi mwaliona tsogolo limene Mulungu akukufunilani?”

Mtsikanayo anaonekelatu kuti wakhudzika. Ndipo misozi ili m’maso, anayankha kuti: “Akufuna kuti ndikhale ndi ciyembekezo komanso ndi tsogolo la mtendele. Zikomo kwambili cifukwa condiwelengela vesili. Ndikhulupilila kuti ili ndi yankho la pemphelo langa. Ndakhala ndikukumana ndi mabvuto otsatizana-tsatizana posacedwapa. Zinthu zakhala zondibvuta kwambili cakuti ndinali kuganiza zongodzipha. M’mawa ndapemphela kwa Mulungu kuti andionetse ngati amandikondabe, ndipo ndangodabwa kuti inuyo ngakhale kuti simundidziwa, mwandiimitsa n’kundiwelengela vesi limene lionetsa mmene Mulungu amandionela. Ndiona kuti izi sizinacitike mwangozi.”

Mlongoyo anaonetsa mtsikanayo nkhani zingapo za pa jw.org zofotokoza mmene angasewenzetsele Baibo pofuna kuthetsa maganizo ofuna kudzipha. Mlongoyo anam’fotokozela mmene phunzilo la Baibo limacitikila ndipo anamuitanila ku misonkhano. Mlungu wotsatila, mtsikanayo anapezeka pa msonkhano wa kumapeto kwa mlungu, ndipo anayamba kuphunzila Baibo m’bulosha yakuti Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!

Conco, kaya muli pa msinkhu wotani, inunso mungaciteko ulaliki wa pa kasitandi.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani