LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Ciŵili, September 30

Mulungu ndi wokhulupilika ndipo sadzalola kuti muyesedwe kufika pamene simungapilile, koma pamene mukukumana ndi mayeselowo iye adzapeleka njila yopulumukila kuti muthe kuwapilila.​—1 Akor. 10:13.

Kusinkhasinkha pemphelo limene munapeleka podzipatulila kwa Yehova, kudzakuthandizani kugonjetsa mayeselo alionse amene mungakumane nawo. Mwacitsanzo, kodi mungayambe kuceza mokopana na mkazi wa mwini kapena mwamuna wa mwini? M’pang’ono pomwe! Cifukwa munasankhilatu kuti simungacite za mtundu umenewu. Ngati simulola zilakolako zoipa kuzika mizu mwa inu, simudzafunika kulimbana nazo mtsogolo. Ndipo mudzapewa kuyenda “panjila yoipa.” (Miy. 4:14, 15) Kuganizila citsanzo ca Yesu kungakuthandizeni. Iye anali wofunitsitsa kukondweletsa Atate ake. Nanunso muyenela kukana nthawi yomweyo komanso mosasunthika ciliconse cimene cingakhumudwitse Mulungu amene munadzipatulila kwa Iye. (Mat. 4:10; Yoh. 8:29) Kwenikweni, mayeso na mayeselo amakupatsani mpata woonetsa kuti ndinu wofunitsitsa kum’tsatilabe Yesu. Mwa kutelo, dziŵani kuti Yehova adzakuthandizani. w24.03 9-10 ¶8-10

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Citatu, October 1

Nzelu yocokela kumwamba . . . ndi yokonzeka kumvela.​—Yak. 3:17.

Kodi kukhala womvela kumakuvutani? Davide nayenso, zinali kumuvuta nthawi zina. Ndiye cifukwa cake anapemphela kuti: “Ndipatseni mtima wofunitsitsa kukumvelani.” (Sal. 51:12) Davide anali kukonda Yehova. Ngakhale n’telo, nthawi zina Davide zinali kumuvuta kuonetsa mtima womvela, ndipo ni mmenenso zilili kwa ise. Cifukwa ciyani? Coyamba, cifukwa cakuti tinatengela mzimu wa kusamvela kwa makolo athu. Caciŵili, Satana amayesetsa kutinyengelela kuti tipandukile Yehova mmene iye anacitila. (2 Akor. 11:3) Cacitatu, tikukhala m’dziko mmene khalidwe la kupanduka lili paliponse, ndipo “mpweya umenewu, kapena kuti kaganizidwe kameneka, tsopano kakugwila nchito mwa ana osamvela.” (Aef. 2:2) Tiyenela kucita zonse zothekha kuti tilimbane na ucimo, Satana, komanso dziko, kuti timvele Yehova komanso aja amene wapatsa ulamulilo. w23.10 6 ¶1

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Cinayi, October 2

Iwe wasunga vinyo wabwino mpaka nthawi ino.​—Yoh. 2:10.

Kodi tiphunzilapo ciyani pa cozizwitsa ca Yesu cosandutsa madzi kukhala vinyo? Kukhala odzicepetsa. Yesu sanadzitame pa cozizwitsaco ayi. Ndipo sanadzitamepo pa zonse zimene anali kucita. M’malo mwake, nthawi zonse anali kudzicepetsa mwa kupeleka ulemu na ulemelelo kwa Atate wake. (Yoh. 5:19, 30; 8:28) Tikatengela citsanzo ca Yesu mwa kukhala odzicepetsa, sitidzadzitama pa zilizonse tingakwanitse kucita. Tisadzitame ayi, koma tidzitamandile kuti Mulungu wathu ni wabwino, ndipo tili na mwayi wom’tumikila. (Yer. 9:23, 24) Tizim’patsa ulemelelo wake. Ndi iko komwe, n’ciyani cabwino cimene tingakwanitse kucita popanda thandizo la Yehova? (1 Akor. 1:26-31) Ngati tikhala odzicepetsa, sitidzafuna kudzipezela ulemu pa zabwino zimene tacitila ena. Timakhutila kudziŵa kuti Yehova amaona komanso amayamikila zimene timacita. (Yelekezelani na Mateyu 6:2-4; Aheb. 13:16) Ndithudi, timakondweletsa Yehova tikamatengela Yesu poonetsa kudzicepetsa.​—1 Pet. 5:6. w23.04 4 ¶9; 5 ¶11-12

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani