LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Cinayi, September 11

Asonyezeni kuti mumawakonda.​—2 Akor. 8:24.

Tingawaonetse cikondi abale na alongo athu pokhala nawo pa ubwenzi. (2 Akor. 6:11-13) Ambili tili m’mipingo muli abale na alongo a zikhalidwe zosiyana-siyana, komanso zibadwa zosiyana-siyana. Tingakulitse cikondi cathu kwa onsewo mwa kuyang’ana kwambili pa makhalidwe awo abwino. Tikamaona ena mmene Yehova amawaonela, timaonetsa kuti timawakonda. Pa cisautso cacikulu, cikondi cidzakhala cofunika kwambili. Kodi n’kuti kumene tidzapeza citetezo cisautsoco cikadzayamba? Onani malangizo amene Yehova anauza atumiki ake Babulo wakale ataukilidwa. Iye anawauza kuti: “Inu anthu anga, pitani mukaloŵe m’zipinda zanu zamkati ndipo mukatseke zitseko. Mukabisale kwa kanthawi mpaka mkwiyo utadutsa.” (Yes. 26:20) Zioneka kuti malangizo amenewa adzagwilanso nchito kwa ife pa cisautso cacikulu. w23.07 6-7 ¶14-16

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Cisanu, September 12

Zocitika zapadzikoli zikusintha.​—1 Akor. 7:31.

Dzifunseni kuti: ‘Kodi anthu amanidziŵa kuti ndine munthu wololela? Kapena amanidziŵa kuti ndine woumitsa zinthu, wokhwimitsa zinthu, kapena wa zimene ndanena-ndanena? Kodi nimamvako za ena na kulolela kuti zinthu zicitike mmene iwo afunila ngati n’kotheka?’ Tikamaonetsa kwambili kulolela, timaonetsanso kuti tikutengela kwambili Yehova na Yesu. Munthu wololela amakhala wokonzeka kusintha pamene mikhalidwe yasintha. Zinthu zikasintha, tingakumane na mavuto amene sitinawayembekezele. Mwacitsanzo, tingadwale mwadzidzidzi. Mwina kusintha mosayembekezela kwa zacuma kapena zandale, kungapangitse umoyo wathu kukhala wovuta kwadzaoneni. (Mlal. 9:11) Ngakhale kusinthidwa pa udindo, utumiki, kapena malo otumikilako kungatiike pa mayeso. Tikhoza kusintha mogwilizana na mikhalidwe yathu yatsopano ngati tatsatila masitepe anayi otsatilawa: (1) civomelezeni kuti zinthu zasintha, (2) yang’anani kutsogolo, (3) muziika maganizo anu pa zinthu zolimbikitsa, komanso (4) muzithandiza ena. w23.07 21-22 ¶7-8

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Ciŵelu, September 13

Ndiwe munthu wokondedwa kwambili.​—Dan. 9:23.

Mneneli Danieli anali wacinyamata pamene Ababulo anam’tengela kutali na kwawo monga mkaidi. Koma Ababulowo anacita naye cidwi Danieli. Iwo anaona kuti iye ‘analibe cilema ciliconse, anali wooneka bwino,’ komanso kuti anacokela m’banja lolemekezeka. (1 Sam. 16:7) Pa zifukwa zimenezi, Ababulowo anam’phunzitsa kuti akatumikile m’nyumba yacifumu. (Dan. 1:3, 4, 6) Yehova anali kum’konda Danieli, cifukwa ca khalidwe lake labwino. Ndipo Danieli ayenela kuti anali na zaka za m’ma 20 pamene Yehova anam’chula kuti wolungama pamodzi na Nowa komanso Yobu​—amuna amene anapanga mbili yabwino na Mulungu kwa zaka zambili. (Gen. 5:32; 6:9, 10; Yobu 42:16, 17; Ezek. 14:14) Yehova sanaleke kum’konda Danieli pa umoyo wake wonse.​—Dan. 10:11, 19. w23.08 2 ¶1-2

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani