Cisanu, September 12
Zocitika zapadzikoli zikusintha.—1 Akor. 7:31.
Dzifunseni kuti: ‘Kodi anthu amanidziŵa kuti ndine munthu wololela? Kapena amanidziŵa kuti ndine woumitsa zinthu, wokhwimitsa zinthu, kapena wa zimene ndanena-ndanena? Kodi nimamvako za ena na kulolela kuti zinthu zicitike mmene iwo afunila ngati n’kotheka?’ Tikamaonetsa kwambili kulolela, timaonetsanso kuti tikutengela kwambili Yehova na Yesu. Munthu wololela amakhala wokonzeka kusintha pamene mikhalidwe yasintha. Zinthu zikasintha, tingakumane na mavuto amene sitinawayembekezele. Mwacitsanzo, tingadwale mwadzidzidzi. Mwina kusintha mosayembekezela kwa zacuma kapena zandale, kungapangitse umoyo wathu kukhala wovuta kwadzaoneni. (Mlal. 9:11) Ngakhale kusinthidwa pa udindo, utumiki, kapena malo otumikilako kungatiike pa mayeso. Tikhoza kusintha mogwilizana na mikhalidwe yathu yatsopano ngati tatsatila masitepe anayi otsatilawa: (1) civomelezeni kuti zinthu zasintha, (2) yang’anani kutsogolo, (3) muziika maganizo anu pa zinthu zolimbikitsa, komanso (4) muzithandiza ena. w23.07 21-22 ¶7-8
Ciŵelu, September 13
Ndiwe munthu wokondedwa kwambili.—Dan. 9:23.
Mneneli Danieli anali wacinyamata pamene Ababulo anam’tengela kutali na kwawo monga mkaidi. Koma Ababulowo anacita naye cidwi Danieli. Iwo anaona kuti iye ‘analibe cilema ciliconse, anali wooneka bwino,’ komanso kuti anacokela m’banja lolemekezeka. (1 Sam. 16:7) Pa zifukwa zimenezi, Ababulowo anam’phunzitsa kuti akatumikile m’nyumba yacifumu. (Dan. 1:3, 4, 6) Yehova anali kum’konda Danieli, cifukwa ca khalidwe lake labwino. Ndipo Danieli ayenela kuti anali na zaka za m’ma 20 pamene Yehova anam’chula kuti wolungama pamodzi na Nowa komanso Yobu—amuna amene anapanga mbili yabwino na Mulungu kwa zaka zambili. (Gen. 5:32; 6:9, 10; Yobu 42:16, 17; Ezek. 14:14) Yehova sanaleke kum’konda Danieli pa umoyo wake wonse.—Dan. 10:11, 19. w23.08 2 ¶1-2
Sondo, September 14
Muthe kumvetsa bwino m’lifupi ndi m’litali, kukwela ndi kuzama kwa coonadi.—Aef. 3:18.
Mukafuna kugula nyumba mungafune kudzionela nokha nyumbayo, kuizungulila na kuona milingo yake yonse. Tiyenela kucita cimodzi-modzi poŵelenga na kuphunzila Baibo. Mukamaŵelenga mothamanga, mungadziŵe mfundo zocepa cabe—“mfundo zoyambilila za m’mawu opatulika a Mulungu.” (Aheb. 5:12) M’malo mwake, monga mmene mungacitile na nyumba, “fufuzani” kuti mumvetse mfundo zamtengo wapatali. Njila yabwino koposa yoŵelengela mawu a Mulungu ni kuyesa kuona mmene mfundo zosiyana-siyana zikugwilizanila. Muziyesetsa kumvetsa zimene mumakhulupilila komanso cifukwa cake mumazikhulupilila. Kuti timvetse Mawu a Mulungu, tiyenela kuŵelenga mfundo zozama za coonadi. Mtumwi Paulo analimbikitsa Akhristu anzake kuti ayenela kuŵelenga Mawu a Mulungu mwakhama ‘kuti athe kudziŵa bwino m’lifupi ndi m’litali ndi kukwela ndi kuzama’ kwa coonadi. Kucita zimenezi kunawathandiza ‘kuti azike mizu mokhazikika’ pa cikhulupililo. (Aef. 3:14-19) Ifenso tiyenela kucita cimodzi-modzi. w23.10 18 ¶1-3