Ciŵelu, September 20
Muzikondana.—Yoh. 13:34.
Sitingamvele lamulo la Yesu lakuti tizikondana ngati timakonda ena mu mpingo na kupewa kukonda ena. Monga mmene zinalili kwa Yesu, nafenso sitingakhale omasuka kwa onse. (Yoh. 13:23; 20:2) Koma mtumwi Petulo akutikumbutsa kuti tiyenela kuyesetsa ‘kukonda gulu lonse la abale,’ cifukwa ni mbali ya banja lathu. (1 Pet. 2:17) Petulo anatilimbikitsa kuti tiyenela ‘kukondana kwambili kucokela mu mtima.’ (1 Pet. 1:22) Palembali, mawu akuti kukonda “kwambili” aphatikizapo kuonetsa cikondi kwa munthu wina ngakhale kuti zingakhale zovuta kucita zimenezo. Mwacitsanzo, ngati m’bale watikhumudwitsa m’njila ina yake, mwacibadwa tingafune kubwezela m’malo moonetsa cikondi. Komabe, Petulo anaphunzila kuti kubwezela sikukondweletsa Mulungu. (Yoh. 18:10, 11) Petulo analemba kuti: “Osabwezela coipa pa coipa kapena cipongwe pa cipongwe, koma m’malomwake muzidalitsa.” (1 Pet. 3:9) Lolani cikondi kukusonkhezelani kukhala okoma mtima komanso oganizila ena. w23.09 28-29 ¶9-11
Sondo, September 21
Nawonso akazi akhale . . . ocita zinthu mosapitilila malile, okhulupilika m’zinthu zonse.—1 Tim. 3:11.
Timacita cidwi kuona mmene mwana amakulila mwamsanga kukhala wamkulu. Kukula kumeneku kumacitika pakokha. Komabe, kukhala Mkhristu wokhwima sikucitika pakokha. (1 Akor. 13:11; Aheb. 6:1) Kuti tikwanilitse colinga cimeneci, tiyenela kukhala paubwenzi wa thithithi na Yehova. Tifunikilanso mzimu wake woyela pokulitsa makhalidwe aumulungu, kukulitsa maluso othandiza komanso kukonzekela maudindo a m’tsogolo. (Miy. 1:5) Yehova ndiye analenga amuna na akazi. (Gen. 1:27) N’zoonekelatu kuti amuna na akazi amasiyana m’maonekedwe. Ndipo amasiyananso m’njila zina. Mwacitsanzo, Yehova analenga amuna na akazi kuti azigwila nchito zosiyana. Conco, onse ayenela kukhala na makhalidwe komanso maluso amene angawathandize kukwanilitsa maudindo awo.—Gen. 2:18. w23.12 18 ¶1-2
Mande, September 22
Mukaphunzitse anthu a mitundu yonse kuti akhale ophunzila anga. Muziwabatiza mʼdzina la Atate, ndi la Mwana.—Mat. 28:19.
Mosakayikila, Yesu anafuna kuti ena aziseŵenzetsa dzina lenileni la Atate wake. Atsogoleli ena a cipembedzo a m’nthawi imeneyo anali kunena kuti dzina la Mulungu ni lolemekezeka kwambili moti siliyenela kuchulidwa. Koma Yesu sanalole kuti miyambo yosazikika m’Malemba imeneyo imulepheletse kulemekeza dzina la Atate wake. Ganizilani zimene zinacitika atacilitsa munthu wogwidwa na ziŵanda m’cigawo ca Agerasa. Anthu anacita mantha kwambili, ndipo anacondelela Yesu kuti acoke. Conco, iye sanakhalitse m’cigawo cimeneco. (Maliko 5:16, 17) Ngakhale n’telo, iye anafunabe kuti anthu adziŵe dzina la Yehova m’cigawo cimeneci. Conco, anauza wocilitsidwayo kuti aziuza anthu zimene Yehova anam’citila, osati zimene Yesu anacita. (Maliko 5:19) N’zimenenso amafuna masiku ano—kuti tidziŵikitse dzina la Atate ake pa dziko lonse lapansi! (Mat. 24:14; 28:20) Tikacita zimenezi, timakondweletsa Mfumu yathu, Yesu. w24.02 10 ¶10