Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
Chilengezo
Chinenero chatsopano chomwe chilipo: Betsileo
  • Lero

Lachitatu, October 29

Moyo wanga utamande Yehova. Chilichonse cha mkati mwanga, chitamande dzina lake loyera.​—Sal. 103:1.

Kukonda Mulungu kumachititsa anthu okhulupirika kuti azitamanda dzina lake ndi mtima wonse. Mfumu Davide ankadziwa kuti kutamanda dzina la Yehova kumatanthauza kutamanda Yehovayo. Choncho tikamva dzinali timaganizira makhalidwe ake abwino komanso ntchito zake zodabwitsa. Davide ankafuna aziona kuti dzina la Atate wake ndi loyera komanso kumalitamanda. Iye ankafuna azichita zimenezo ndi “chilichonse cha mkati [mwake]” kapena kuti ndi mtima wonse. Mofanana ndi Davide, Alevi nawonso ankatsogolera potamanda Yehova. Modzichepetsa, iwo anavomereza kuti mawu awo sakanatha kufotokoza mokwanira ulemerero umene dzina loyera la Yehova liyenera kulandira. (Neh. 9:5) Mosakayikira, Yehova anasangalala ndi kudzichepetsa komanso kumutamanda kochokera pansi pamtima kumeneku. w24.02 6:6

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachinayi, October 30

Mulimonse mmene tapitira patsogolo, tiyeni tipitirize kupita patsogolo pochita zomwe tikuchitazo.​—Afil. 3:16.

Yehova sadzakuonani kuti ndinu wolephera chifukwa simunakwaniritse cholinga chimene simukanatha kuchikwaniritsa. (2 Akor. 8:12) Muziphunzirapo kathu mukakumana ndi zolepheretsa. Muziganizira zomwe mwakwanitsa kale kuchita. Baibulo limanena kuti “Mulungu si wosalungama woti angaiwale ntchito yanu.” (Aheb. 6:10) Choncho inunso musamaiwale zomwe mwachita. Muziganizira zolinga zomwe mwazikwaniritsa kale kaya ndi kulimbitsa ubwenzi wanu ndi Yehova, kuuza ena zokhudza iye kapena kubatizidwa. Monga mmene mwakhala mukukwaniritsira zolinga zanu m’mbuyomu, mungapitirizenso kukwaniritsa cholinga chanu panopa. Mothandizidwa ndi Yehova, inunso mungathe kukwaniritsa cholinga chanu mofanana ndi woyendetsa boti yemwe amasangalala akafika kumene akupita. Koma kumbukirani kuti oyendetsa boti ambiri amasangalalanso ndi ulendo wawo. Inunso mukayesetsa kuti mukwaniritse cholinga chanu chauzimu, muzisangalala ndi mmene Yehova akukuthandizirani komanso kukudalitsirani. (2 Akor. 4:7) Ndipo ngati simungafooke mudzapeza madalitso ambiri.—Agal. 6:9. w23.05 24:16-18

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachisanu, October 31

Atatewo amakukondani chifukwa munandikonda ndipo mwakhulupirira kuti ine ndinabwera monga nthumwi ya Mulungu.​—Yoh. 16:27.

Yehova amafunitsitsa kuuza anthu omwe amawakonda kuti amasangalala nawo. Malemba amatchula nthawi ziwiri pomwe iye anauza Yesu kuti ndi Mwana wake wokondedwa ndipo amasangalala naye. (Mat. 3:17; 17:5) Kodi mungakonde kumva Yehova akukutsimikizirani kuti amasangalala nanu? Iye salankhula nafe mwachindunji koma amatilankhula kudzera m’Mawu ake. ‘Tingamve’ mawu a Yehova onena kuti amasangalala nafe tikamawerenga mawu a Yesu m’mabuku a Uthenga Wabwino. Yesu ankatsanzira ndendende makhalidwe a Atate wake. Choncho tikamawerenga kuti Yesu ankasangalala ndi otsatira ake okhulupirika, omwe sanali angwiro, timadziwa kuti Yehova amasangalalanso ndi ifeyo. (Yoh. 15:9, 15) Tikakumana ndi mavuto sizitanthauza kuti Mulungu sakusangalala nafe. M’malomwake, zimenezi zimatipatsa mwayi wosonyeza kuti timakonda kwambiri Mulungu ndipo timamukhulupirira.—Yak. 1:12. w24.03 13:10-11

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani