1 Akorinto
13 Ngati ndimalankhula malilime+ a anthu ndi a angelo koma ndilibe chikondi, ndakhala ngati belu longolira, kapena chinganga chosokosera.+ 2 Ndipo ngati ndili ndi mphatso yonenera,+ yodziwa zinsinsi zonse zopatulika,+ yodziwa zinthu zonse,+ komanso ngati ndili ndi chikhulupiriro chonse choti n’kusuntha nacho mapiri,+ koma ndilibe chikondi, sindili kanthu.+ 3 Ngati ndapereka zanga zonse kudyetsa ena,+ ndipo ngati ndapereka thupi langa+ kuti ndidzitame, koma ndilibe chikondi,+ sindinapindule m’pang’ono pomwe.
4 Chikondi+ n’choleza mtima+ ndiponso n’chokoma mtima.+ Chikondi sichichita nsanje,+ sichidzitama,+ sichidzikuza,+ 5 sichichita zosayenera,+ sichisamala zofuna zake zokha,+ sichikwiya.+ Sichisunga zifukwa.+ 6 Sichikondwera ndi zosalungama,+ koma chimakondwera ndi choonadi.+ 7 Chimakwirira zinthu zonse,+ chimakhulupirira zinthu zonse,+ chimayembekezera zinthu zonse,+ chimapirira zinthu zonse.+
8 Chikondi sichitha.+ Koma kaya pali mphatso za kunenera, zidzatha. Kaya kulankhula malilime, kudzatha. Ngakhale mphatso ya kudziwa zinthu, idzatha.+ 9 Pakuti tikudziwa+ moperewera ndipo tikunenera mopereweranso.+ 10 Koma chokwanira chikadzafika,+ choperewerachi chidzatha. 11 Pamene ndinali kamwana, ndinali kulankhula ngati kamwana, kuganiza ngati kamwana, ndiponso kuona zinthu ngati kamwana. Koma tsopano pamene ndakula,+ ndasiya zachibwana. 12 Pakuti pa nthawi ino sitikuona bwinobwino chifukwa tikugwiritsa ntchito galasi losaoneka bwinobwino,+ koma pa nthawiyo zidzakhala maso ndi maso.+ Pa nthawi ino zimene ndikudziwa n’zoperewera, koma pa nthawiyo ndidzadziwa bwinobwino ngati mmene ineyo ndikudziwikira bwinobwino.+ 13 Komabe, tsopano patsala zitatu izi: Chikhulupiriro, chiyembekezo, chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.+