2 Timoteyo
2 Choncho iwe mwana wanga,+ pitiriza kupeza mphamvu+ m’kukoma mtima kwakukulu+ kumene kuli mwa Khristu Yesu. 2 Zinthu zimene unazimva kwa ine ndi kwa mboni zambiri+ zokhudza ine, zimenezo uziphunzitse kwa anthu okhulupirika amene nawonso, adzakhala oyenerera bwino kuphunzitsa ena.+ 3 Monga msilikali wabwino+ wa Khristu Yesu, khala wokonzeka kumva zowawa.+ 4 Msilikali amene ali pa nkhondo+ sachita nawo zamalonda zimene anthu wamba amachita,+ pofuna kukondweretsa amene anamulemba usilikali. 5 Komanso, ngati munthu akuchita nawo mpikisano ngakhale pa masewera,+ savekedwa nkhata yaulemerero kumutu akapanda kupikisana nawo motsatira malamulo. 6 Mlimi wogwira ntchito molimbikira ndiye ayenera kukhala woyamba kudya zipatso zimene anabzala.+ 7 Uziganizira zimene ndikukuuzazi nthawi zonse. Ndithudi, Ambuye adzakuthandiza kuzindikira+ zinthu zonse.
8 Kumbukira kuti, malinga ndi uthenga wabwino umene ndikulalikira,+ Yesu Khristu anauka kwa akufa+ ndipo anali mbewu ya Davide.+ 9 Chifukwa cha uthengawu, ndikumva zowawa mpaka kutsekeredwa m’ndende+ ngati wochita zoipa. Komabe, mawu a Mulungu samangika.+ 10 Pa chifukwa chimenechi, ndikupirirabe zinthu zonse chifukwa cha anthu osankhidwa ndi Mulungu,+ kuti iwonso alandire chipulumutso chimene chimabwera chifukwa chokhala ogwirizana ndi Khristu Yesu, ndiponso alandire ulemerero wosatha.+ 11 Mawu awa ndi oona,+ akuti: Ndithudi, ngati tinafa naye limodzi, tidzakhalanso ndi moyo limodzi naye.+ 12 Tikapitiriza kupirira, tidzalamuliranso limodzi ndi iye monga mafumu.+ Tikamukana,+ iyenso adzatikana, 13 ndipo tikakhala osakhulupirika,+ iye adzakhalabe wokhulupirika, pakuti sangadzikane.
14 Uziwakumbutsa+ zimenezi nthawi zonse. Uziwachenjeza mwamphamvu+ pamaso pa Mulungu,+ kuti asamakangane pa mawu.+ Kuchita zimenezo kulibe phindu m’pang’ono pomwe chifukwa kumawononga chikhulupiriro cha omvetsera. 15 Chita chilichonse chotheka kuti usonyeze kuti ndiwe wovomerezeka+ pamaso pa Mulungu, wantchito+ wopanda chifukwa chochitira manyazi+ ndi ntchito imene wagwira, ndiponso wophunzitsa ndi kufotokoza bwino mawu a choonadi.+ 16 Koma pewa nkhani zopeka zimene zimaipitsa zinthu zoyera,+ pakuti kusaopa Mulungu kudzachulukirachulukira+ mwa anthu olankhula zotero, 17 ndipo mawu awo adzafalikira ngati chilonda chonyeka.+ Ena mwa anthu amenewo ndi Hemenayo ndi Fileto.+ 18 Anthu amenewa apatuka pa choonadi,+ ponena kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale+ ndipo akuwononga chikhulupiriro cha ena.+ 19 Komabe, maziko olimba a Mulungu adakali chikhalire,+ ndipo ali ndi chidindo cha mawu akuti: “Yehova* amadziwa anthu ake,”+ ndiponso akuti: “Aliyense wotchula dzina la Yehova+ aleke kuchita zosalungama.”+
20 M’nyumba yaikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha ayi, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Ziwiya zina zimakhala za ntchito yolemekezeka koma zina zimakhala za ntchito yonyozeka.+ 21 Choncho, ngati munthu akupewa ziwiya za ntchito yonyozekazo, adzakhala chiwiya cha ntchito yolemekezeka, choyera, chofunika kwa mwiniwake, ndi chokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.+ 22 Chotero, thawa zilakolako zaunyamata,+ koma tsatira chilungamo,+ chikhulupiriro, chikondi, ndi mtendere+ limodzi ndi anthu oitana pa Ambuye ndi mtima woyera.+
23 Ndiponso, uzikana mafunso opusa ndi opanda nzeru,+ podziwa kuti amayambitsa mikangano.+ 24 Kapolo wa Ambuye sayenera kukangana ndi anthu,+ koma ayenera kukhala wodekha kwa onse.+ Ayeneranso kukhala woyenerera kuphunzitsa,+ wougwira mtima pokumana ndi zoipa,+ 25 ndi wolangiza mofatsa anthu otsutsa+ kuti mwina Mulungu angawalole kulapa,+ kuti adziwe choonadi molondola.+ 26 Komanso kuti mwina nzeru zawo zingabwereremo kuti awonjoke mumsampha+ wa Mdyerekezi, poona kuti wawagwira amoyo+ pofuna kukwaniritsa cholinga chake.