39 Ndiyeno anapanga zovala+ zosokedwa bwino zoti azivala potumikira m’malo oyera,+ pogwiritsa ntchito ulusi wabuluu, ubweya wa nkhosa wonyika mu utoto wofiirira ndi ulusi wofiira kwambiri.+ Motero anapanga zovala zopatulika+ za Aroni, monga mmene Yehova analamulira Mose.