16 Pa nthawi imeneyo anthu oopa Yehova+ analankhulana, aliyense ndi mnzake, ndipo Yehova anatchera khutu ndi kumvetsera.+ Buku la chikumbutso linayamba kulembedwa pamaso pake.+ Buku limeneli linali lonena za anthu oopa Yehova ndi anthu amene anali kuganizira za dzina lake.+