Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 25:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 M’chaka cha 9+ cha ufumu wa Zedekiya, m’mwezi wa 10,+ pa tsiku la 10 la mweziwo, Nebukadinezara+ mfumu ya Babulo anabwera+ ku Yerusalemu pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo. Anabwera kudzachita nkhondo ndi mzindawo ndipo anamanga misasa ndi khoma kuzungulira mzinda wonsewo.+

  • 2 Mbiri 36:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Choncho anawabweretsera mfumu ya Akasidi+ yomwe inapha anyamata awo ndi lupanga+ m’nyumba yopatulika.+ Sinachitire chisoni mnyamata kapena namwali, wachikulire kapena nkhalamba yotheratu.+ Mulungu anapereka zonse m’manja mwake.

  • Yeremiya 21:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 “‘“Mzinda uwu ndaukana* ndipo ukumana ndi tsoka osati zabwino,”+ watero Yehova. “Ndidzaupereka m’manja mwa mfumu ya Babulo+ ndipo idzautentha ndi moto.”+

  • Yeremiya 32:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Anam’tsekera kumeneko chifukwa Zedekiya mfumu ya Yuda sanafune kuti Yeremiya azinenera,+ moti anamuuza kuti:

      “N’chifukwa chiyani ukulosera+ kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Ine ndikupereka mzinda uwu m’manja mwa mfumu ya Babulo moti iulanda,+

  • Yeremiya 52:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ndiyeno m’chaka cha 9 cha ufumu wa Zedekiya,+ m’mwezi wa 10, pa tsiku la 10 la mweziwo, Nebukadirezara mfumu ya Babulo pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwera ku Yerusalemu+ kudzaukira mzindawo. Atafika anayamba kumanga misasa ndi khoma kuzungulira mzinda wonsewo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena