Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 5:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Antchito anga adzainyamula ku Lebanoni+ n’kutsikira nayo kunyanja, ndipo ineyo kumbali yanga ndidzaimanga pamodzi ngati phaka n’kuiyandamitsa panyanja kuti ikafike kumalo kumene mudzandiuze.+ Kenako ndidzauza anthu kuti aimasule, ndipo inuyo mukaitengera kumeneko. Ndipo inu mudzachita zofuna zanga pondipatsa chakudya cha banja langa.”+

  • 2 Mbiri 2:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ineyo ndipereka chakudya cha antchito anu otola nkhuni ndi odula mitengo. Ndipereka tirigu wokwanira makori* 20,000,+ balere makori 20,000, vinyo mitsuko* 20,000,+ ndi mafuta mitsuko 20,000.”

  • Ezara 3:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Kenako anthuwo anapereka ndalama+ kwa anthu osema miyala+ ndi kwa amisiri,+ ndiponso anapereka chakudya,+ zakumwa ndi mafuta+ kwa Asidoni+ ndi kwa anthu a ku Turo,+ kuti abweretse matabwa a mkungudza kuchokera ku Lebanoni+ n’kudzawasiya m’mphepete mwa nyanja ku Yopa.+ Anachita zimenezi malinga ndi chilolezo chimene Koresi+ mfumu ya ku Perisiya anawapatsa.

  • Machitidwe 12:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Tsopano Herode anali wokwiya ndi anthu a ku Turo ndi ku Sidoni, ndipo anafuna kuwathira nkhondo. Choncho onse anabwera kwa iye mogwirizana. Ndipo iwo atanyengerera Balasito, amene anali woyang’anira chipinda chogona cha mfumu, anayamba kupempha mtendere. Iwo anachita zimenezi chifukwa dziko lawo linali kudalira chakudya+ chochokera m’dziko la mfumuyo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena