9 Pamenepo iwo anati: “Choka apa!” Ananenanso kuti: “Uyu ndi wobwera kwathu kuno, ndipo akukhala monga mlendo.+ Ndiye lero azitiuza zochita?+ Tsopano iweyo tikuchita zoopsa kuposa iwowo.” Atatero iwo anamukhamukira Lotiyo ndi kumupanikiza,+ moti anatsala pang’ono kuthyola chitseko.+