24 Chotero monga momwe lawi la moto limanyeketsera mapesi+ komanso monga mmene udzu wouma umanyekera m’malawi a moto, muzu wawo udzawola n’kuyamba kununkha.+ Maluwa awo adzauma n’kuuluzika ngati fumbi, chifukwa akana malamulo a Yehova wa makamu+ ndipo anyoza mawu a Woyera wa Isiraeli.+