11 Ndipo ena mwa inu munali otero.+ Koma mwasambitsidwa kukhala oyera,+ mwapatulidwa,+ mwayesedwa olungama+ m’dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu,+ komanso ndi mzimu wa Mulungu wathu.+
5 Iye sanatero chifukwa cha ntchito+ zolungama zimene tinachita+ ayi. Koma malinga ndi chifundo+ chake, anatipulumutsa mwa kutisambitsa+ ndipo chifukwa chakuti tinasambitsidwa choncho, tinafika ku moyo+ watsopano. Komanso, anatipulumutsa potisandutsa atsopano mwa mzimu woyera.+
7 Komatu, ngati tikuyenda m’kuunika ngati mmene iye alili m’kuunika,+ ndiye kuti ndife ogwirizana,+ ndipo magazi+ a Yesu Mwana wake akutiyeretsa+ ku uchimo wonse.+
5 Komanso, kuchokera kwa Yesu Khristu, “Mboni Yokhulupirika,”+ “Woyamba kubadwa kuchokera kwa akufa,”+ ndiponso “Wolamulira wa mafumu a dziko lapansi.”+
Kwa iye amene amatikonda,+ amenenso anatimasula ku machimo athu ndi magazi ake enieniwo,+