30 Tsiku lotsatira, pofunitsitsa kudziwa chenicheni chimene Ayudawo anali kumuimbira mlandu, anamumasula. Atatero analamula ansembe aakulu ndi Khoti lonse Lalikulu la Ayuda kuti asonkhane pamodzi. Ndiyeno anabweretsa Paulo ndi kumuimiritsa pakati pawo.+