Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 15
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Deuteronomo 15:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 25:2
  • +Yak 2:13
  • +De 31:10

Deuteronomo 15:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 12:43; De 14:21; 23:20

Deuteronomo 15:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 14:29; 28:8; Miy 11:25; 14:21; 28:27
  • +Nu 33:53; Sl 135:12

Deuteronomo 15:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:40; Yos 1:7; Yes 1:19

Deuteronomo 15:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 28:12; Miy 22:7
  • +De 28:13; 1Mf 4:24

Deuteronomo 15:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 21:13; Yak 2:16; 1Yo 3:17

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    9/15/2010, tsa. 8

Deuteronomo 15:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 25:35; Sl 37:26; Miy 19:17; Mt 5:42; Lu 6:35; Aga 2:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    9/15/2010, tsa. 8

Deuteronomo 15:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 4:23; Yer 17:10; Mt 15:19
  • +De 15:1
  • +Miy 28:22; 1Pe 4:9
  • +Eks 22:23; De 24:15; Yob 34:28; Miy 21:13; Yak 5:4
  • +Mt 25:45; Yak 4:17

Deuteronomo 15:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 20:35; 2Ak 9:7; 1Ti 6:18; Ahe 13:16
  • +De 15:4; 24:19; Sl 41:1; Miy 22:9; Yes 32:8; 2Ak 9:8

Deuteronomo 15:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 26:11
  • +Miy 3:27; Mt 5:42; Lu 12:33; Mac 2:45

Deuteronomo 15:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 21:2; Le 25:39
  • +De 15:1; Yer 34:14

Deuteronomo 15:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 3:21; 12:36; Miy 3:27; Akl 4:1

Deuteronomo 15:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 10:22; Mac 20:35

Deuteronomo 15:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:2; De 5:15; Mt 18:33

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2014, tsa. 19

Deuteronomo 15:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 21:5

Deuteronomo 15:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 21:6

Deuteronomo 15:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 15:10
  • +Le 19:13; De 24:15
  • +Ge 30:30

Deuteronomo 15:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 13:2; 34:19; Le 27:26; Nu 3:13; 18:15, 17
  • +Eks 22:30; De 12:6

Deuteronomo 15:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 12:5; 14:23; 16:11

Deuteronomo 15:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 22:20; De 17:1; Mki 1:8; Ahe 9:14

Deuteronomo 15:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 14:5; 1Mf 4:23
  • +De 12:15, 22

Deuteronomo 15:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 9:4; Le 7:26; 17:10; 1Sa 14:33; Mac 15:20
  • +Le 17:13; De 12:16

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    10/15/2000, ptsa. 30-31

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 15:2Le 25:2
Deut. 15:2Yak 2:13
Deut. 15:2De 31:10
Deut. 15:3Eks 12:43; De 14:21; 23:20
Deut. 15:4De 14:29; 28:8; Miy 11:25; 14:21; 28:27
Deut. 15:4Nu 33:53; Sl 135:12
Deut. 15:5De 4:40; Yos 1:7; Yes 1:19
Deut. 15:6De 28:12; Miy 22:7
Deut. 15:6De 28:13; 1Mf 4:24
Deut. 15:7Miy 21:13; Yak 2:16; 1Yo 3:17
Deut. 15:8Le 25:35; Sl 37:26; Miy 19:17; Mt 5:42; Lu 6:35; Aga 2:10
Deut. 15:9Miy 4:23; Yer 17:10; Mt 15:19
Deut. 15:9De 15:1
Deut. 15:9Miy 28:22; 1Pe 4:9
Deut. 15:9Eks 22:23; De 24:15; Yob 34:28; Miy 21:13; Yak 5:4
Deut. 15:9Mt 25:45; Yak 4:17
Deut. 15:10Mac 20:35; 2Ak 9:7; 1Ti 6:18; Ahe 13:16
Deut. 15:10De 15:4; 24:19; Sl 41:1; Miy 22:9; Yes 32:8; 2Ak 9:8
Deut. 15:11Mt 26:11
Deut. 15:11Miy 3:27; Mt 5:42; Lu 12:33; Mac 2:45
Deut. 15:12Eks 21:2; Le 25:39
Deut. 15:12De 15:1; Yer 34:14
Deut. 15:13Eks 3:21; 12:36; Miy 3:27; Akl 4:1
Deut. 15:14Miy 10:22; Mac 20:35
Deut. 15:15Eks 20:2; De 5:15; Mt 18:33
Deut. 15:16Eks 21:5
Deut. 15:17Eks 21:6
Deut. 15:18De 15:10
Deut. 15:18Le 19:13; De 24:15
Deut. 15:18Ge 30:30
Deut. 15:19Eks 13:2; 34:19; Le 27:26; Nu 3:13; 18:15, 17
Deut. 15:19Eks 22:30; De 12:6
Deut. 15:20De 12:5; 14:23; 16:11
Deut. 15:21Le 22:20; De 17:1; Mki 1:8; Ahe 9:14
Deut. 15:22De 14:5; 1Mf 4:23
Deut. 15:22De 12:15, 22
Deut. 15:23Ge 9:4; Le 7:26; 17:10; 1Sa 14:33; Mac 15:20
Deut. 15:23Le 17:13; De 12:16
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano (nwt)
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 15:1-23

Deuteronomo

15 “Kumapeto kwa zaka 7 zilizonse uzilengeza kuti anthu amene anakongola zinthu zako amasuka ku ngongoleyo. 2 Kumasula anthu angongoleko kuzichitika motere:+ munthu aliyense asafunse ngongole imene anabwereketsa mnzake. Asakakamize mnzake kapena m’bale wake kupereka ngongoleyo,+ chifukwa chilengezo choti anthu angongole amasuke chiyenera kuperekedwa pamaso pa Yehova.+ 3 Mlendo+ ungam’kakamize kubweza ngongole, koma ngati m’bale wako wakongola chinthu chako chilichonse usam’kakamize kuchibweza. 4 Pakati panu pasapezeke munthu wosauka, chifukwa Yehova adzakudalitsa ndithu+ m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa kuti likhale cholowa chako.+ 5 Adzakudalitsa ngati udzamveradi mawu a Yehova Mulungu wako ndi kutsatiradi malamulo onsewa amene ndikukupatsa lero.+ 6 Yehova Mulungu wako adzakudalitsa ndithu monga mmene anakulonjezera ndipo mitundu yambiri idzakongola+ zinthu zako mwa kukupatsa chikole, pamene iwe sudzakongola kanthu. Udzalamulira mitundu yambiri koma mitundu sidzakulamulira.+

7 “Wina mwa abale ako akasauka pakati panu, mu umodzi mwa mizinda yanu, m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa, usamuumire mtima kapena kumuumitsira dzanja lako.+ 8 Uzim’kongoza m’bale wako mowolowa manja,+ mulimonse mmene iye wafunira atakupatsa chikole, ndipo uzim’kongoza zimene akusowa. 9 Samala kuti usalankhule mawu achabe mumtima mwako+ kuti, ‘Chaka cha 7, chaka choti anthu angongole amasuke chayandikira,’+ kuti usaolowere manja m’bale wako wosaukayo,+ osam’patsa kalikonse. Pamenepo iye adzafuulira Yehova chifukwa cha zimene iweyo wam’chitira+ ndipo udzapezeka kuti wachimwa.+ 10 Mulimonse mmene zingakhalire uzim’patsa zimene akufunazo,+ ndipo mtima wako usakhale woumira pomupatsa zinthu zimenezo, chifukwa ukakhala wowolowa manja, Yehova Mulungu wako adzakudalitsa pa chilichonse chimene ukuchita ndi pa ntchito zako zonse.+ 11 Pakuti sipadzalephera kukhala wosauka m’dziko lako.+ N’chifukwa chake ndikukulamula kuti, ‘Uzikhala wowolowa manja kwa m’bale wako wovutika ndi wosauka m’dziko lanu.’+

12 “Ngati anakugulitsa m’bale wako, Mheberi wamwamuna kapena wamkazi,+ ndipo wakutumikira zaka 6, m’chaka cha 7 uzim’masula ndi kumulola kuchoka.+ 13 Ndipo ukam’masula ndi kumulola kuchoka, usamulole kuchoka chimanjamanja.+ 14 Uzim’patsako ndithu zina mwa nkhosa zako, mbewu zochokera pamalo ako opunthira, mafuta ochokera pamalo oyengera ndi vinyo wochokera moponderamo mphesa. Uzim’patsa malinga ndi mmene Yehova Mulungu wako wakudalitsira.+ 15 Uzikumbukira kuti unali kapolo m’dziko la Iguputo ndipo Yehova Mulungu wako anakuwombola.+ N’chifukwa chake lero ndikukulamula zinthu zimenezi.

16 “Koma kapoloyo akakuuza kuti, ‘Ine sindikusiyani!’ chifukwa chakuti amakukonda komanso amakonda banja lako, popeza unali kukhala naye bwino,+ 17 uzitenga choboolera ndi kuboola khutu lake ali pakhomo, mpaka chobooleracho chigunde chitseko ndipo azikhala kapolo wako moyo wake wonse.+ Uzichitanso zimenezi ndi kapolo wako wamkazi. 18 Zisakhale zovuta kwa iwe kum’masula kuti achoke,+ chifukwa wakutumikira zaka 6, moti malipiro ake akanafanana ndi malipiro a anthu awiri aganyu,+ ndipo Yehova Mulungu wako wakudalitsa pa chilichonse chimene wachita.+

19 “Mwana aliyense wamphongo woyamba kubadwa wa ng’ombe kapena wa nkhosa uzim’patulira Yehova Mulungu wako.+ Usagwiritse ntchito mwana woyamba kubadwa wa ng’ombe, kapena kumeta ubweya wa mwana woyamba kubadwa wa nkhosa.+ 20 Chaka ndi chaka iweyo ndi banja lako muzidya mwana woyamba kubadwa wa ng’ombe kapena wa nkhosa pamaso pa Yehova Mulungu wako, pamalo amene Yehova adzasankhe.+ 21 Akakhala ndi vuto, monga kulumala kapena khungu, kapena chilema chilichonse chachikulu, usamam’pereke nsembe kwa Yehova Mulungu wako.+ 22 Uzimudyera mumzinda wanu ngati mmene umadyera insa ndi mbawala yamphongo.+ Nayenso munthu wodetsedwa komanso munthu woyera azidya.+ 23 Koma magazi ake okha usadye.+ Uziwathira pansi ngati madzi.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena