Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Deuteronomo 5:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 1:1; 29:10
  • +De 4:5
  • +De 4:1

Deuteronomo 5:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:5; De 4:23; Ahe 9:19

Deuteronomo 5:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:9, 18; 20:22; De 4:33; Mac 7:38

Deuteronomo 5:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:19; De 34:10; Aga 3:19
  • +Eks 19:16

Deuteronomo 5:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 81:10; Ho 13:4
  • +Eks 13:3; 20:2

Deuteronomo 5:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:3; 2Mf 17:35; Yer 25:6

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    3/1/2012, tsa. 23

Deuteronomo 5:8

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani mawu a m’munsi pa Eks 20:4.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:4; Le 26:1; De 4:16, 23; 27:15
  • +Mac 17:29

Deuteronomo 5:9

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti “Mulungu wansanje (wachangu); Mulungu wosalola aliyense kupikisana naye.”

  • *

    Kapena kuti “wolanga ana, m’badwo wachitatu ndi m’badwo wachinayi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:24; Da 3:18; 1Ak 10:14
  • +Eks 34:14; De 4:24; Yos 24:19; Yes 42:8; Nah 1:2; Mt 4:10
  • +Eks 20:5; 34:7; 1Mf 21:29; Mt 23:35

Deuteronomo 5:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:6; Yer 32:18; Da 9:4; Aro 11:28

Deuteronomo 5:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:7; 22:28; Le 19:12
  • +Le 24:16

Deuteronomo 5:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 16:23; 20:8; 31:13

Deuteronomo 5:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:9; 23:12; 34:21

Deuteronomo 5:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 16:29
  • +Ne 13:15
  • +Eks 20:10; 23:12; Le 24:22
  • +De 10:17; Aro 2:11; Aef 6:9

Deuteronomo 5:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 15:15; 24:18
  • +Eks 6:6; De 4:34; Yes 63:12
  • +Eks 31:17

Deuteronomo 5:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 21:15; Le 19:3; De 27:16; Miy 1:8; Mko 7:10
  • +Eks 20:12; Aef 6:3

Deuteronomo 5:17

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani mawu a m’munsi pa Eks 20:13.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 9:6; Eks 20:13; Nu 35:21; Mt 5:21; Aro 13:9

Deuteronomo 5:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:14; Miy 6:32; 1Ak 6:18; Ahe 13:4

Deuteronomo 5:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:15; Le 19:11; Miy 30:9; 1Ak 6:10; Aef 4:28

Deuteronomo 5:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:16; 23:1; Le 19:16; De 19:16; Miy 6:19; 19:5

Deuteronomo 5:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Sa 11:3; Mt 5:28
  • +Eks 20:17; 1Mf 21:4; Lu 12:15; Aro 7:7

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    2/2019, ptsa. 21-22

    Nsanja ya Olonda,

    5/15/2012, tsa. 7

Deuteronomo 5:22

Mawu a M'munsi

  • *

    Pano, “Mawu” akutanthauza mawu olamula, kapena kuti malamulo. Onani Eks 34:28.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:9, 18; De 4:12
  • +Eks 24:12; 31:18; De 4:13

Deuteronomo 5:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:18; Ahe 12:18

Deuteronomo 5:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:18; 24:17; De 4:36
  • +De 4:33

Deuteronomo 5:25

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ahe 12:29
  • +Eks 20:19; De 18:16; Mac 7:38; Aga 3:19

Deuteronomo 5:26

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:33; 5:5; Sl 29:4; 1At 1:9

Deuteronomo 5:27

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:19; Ahe 12:19

Deuteronomo 5:28

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 18:17

Deuteronomo 5:29

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12; Yob 28:28; Miy 1:7; Mt 10:28; 1Pe 2:17
  • +Miy 4:4; 7:2; Mla 12:13; Yes 48:18; 1Yo 5:3
  • +Sl 19:11; Yak 1:25

Deuteronomo 5:31

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:45; 6:1; Eze 20:11; Mki 4:4; Aga 3:19

Deuteronomo 5:32

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 6:3, 25; 8:1
  • +De 12:32; Yos 1:7; Miy 4:27

Deuteronomo 5:33

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12; Yer 7:23
  • +De 4:40; 12:28; Miy 19:16; Aro 10:5

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 5:1De 1:1; 29:10
Deut. 5:1De 4:5
Deut. 5:1De 4:1
Deut. 5:2Eks 19:5; De 4:23; Ahe 9:19
Deut. 5:4Eks 19:9, 18; 20:22; De 4:33; Mac 7:38
Deut. 5:5Eks 20:19; De 34:10; Aga 3:19
Deut. 5:5Eks 19:16
Deut. 5:6Sl 81:10; Ho 13:4
Deut. 5:6Eks 13:3; 20:2
Deut. 5:7Eks 20:3; 2Mf 17:35; Yer 25:6
Deut. 5:8Eks 20:4; Le 26:1; De 4:16, 23; 27:15
Deut. 5:8Mac 17:29
Deut. 5:9Eks 23:24; Da 3:18; 1Ak 10:14
Deut. 5:9Eks 34:14; De 4:24; Yos 24:19; Yes 42:8; Nah 1:2; Mt 4:10
Deut. 5:9Eks 20:5; 34:7; 1Mf 21:29; Mt 23:35
Deut. 5:10Eks 20:6; Yer 32:18; Da 9:4; Aro 11:28
Deut. 5:11Eks 20:7; 22:28; Le 19:12
Deut. 5:11Le 24:16
Deut. 5:12Eks 16:23; 20:8; 31:13
Deut. 5:13Eks 20:9; 23:12; 34:21
Deut. 5:14Eks 16:29
Deut. 5:14Ne 13:15
Deut. 5:14Eks 20:10; 23:12; Le 24:22
Deut. 5:14De 10:17; Aro 2:11; Aef 6:9
Deut. 5:15De 15:15; 24:18
Deut. 5:15Eks 6:6; De 4:34; Yes 63:12
Deut. 5:15Eks 31:17
Deut. 5:16Eks 21:15; Le 19:3; De 27:16; Miy 1:8; Mko 7:10
Deut. 5:16Eks 20:12; Aef 6:3
Deut. 5:17Ge 9:6; Eks 20:13; Nu 35:21; Mt 5:21; Aro 13:9
Deut. 5:18Eks 20:14; Miy 6:32; 1Ak 6:18; Ahe 13:4
Deut. 5:19Eks 20:15; Le 19:11; Miy 30:9; 1Ak 6:10; Aef 4:28
Deut. 5:20Eks 20:16; 23:1; Le 19:16; De 19:16; Miy 6:19; 19:5
Deut. 5:212Sa 11:3; Mt 5:28
Deut. 5:21Eks 20:17; 1Mf 21:4; Lu 12:15; Aro 7:7
Deut. 5:22Eks 19:9, 18; De 4:12
Deut. 5:22Eks 24:12; 31:18; De 4:13
Deut. 5:23Eks 20:18; Ahe 12:18
Deut. 5:24Eks 19:18; 24:17; De 4:36
Deut. 5:24De 4:33
Deut. 5:25Ahe 12:29
Deut. 5:25Eks 20:19; De 18:16; Mac 7:38; Aga 3:19
Deut. 5:26De 4:33; 5:5; Sl 29:4; 1At 1:9
Deut. 5:27Eks 20:19; Ahe 12:19
Deut. 5:28De 18:17
Deut. 5:29De 10:12; Yob 28:28; Miy 1:7; Mt 10:28; 1Pe 2:17
Deut. 5:29Miy 4:4; 7:2; Mla 12:13; Yes 48:18; 1Yo 5:3
Deut. 5:29Sl 19:11; Yak 1:25
Deut. 5:31De 4:45; 6:1; Eze 20:11; Mki 4:4; Aga 3:19
Deut. 5:32De 6:3, 25; 8:1
Deut. 5:32De 12:32; Yos 1:7; Miy 4:27
Deut. 5:33De 10:12; Yer 7:23
Deut. 5:33De 4:40; 12:28; Miy 19:16; Aro 10:5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano (nwt)
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 5:1-33

Deuteronomo

5 Ndiyeno Mose anaitana Aisiraeli+ onse n’kuwauza kuti: “Inu Aisiraeli, mverani malangizo ndi zigamulo+ zimene ndikukuuzani lero, ndipo muziphunzire ndi kuzitsatira mosamala.+ 2 Yehova Mulungu wathu anachita nafe pangano ku Horebe.+ 3 Yehova sanachite pangano limeneli ndi makolo athu, koma ndi ife, tonsefe amene tili ndi moyo pano lero. 4 Yehova analankhula nanu pamasom’pamaso m’phiri, kuchokera pakati pa moto.+ 5 Ine ndinaima pakati pa Yehova ndi inu pa nthawi imeneyo,+ kuti ndikuuzeni mawu a Yehova, (pakuti munali kuopa moto, ndipo simunakwere m’phirimo).+ Pamenepo iye anati,

6 “‘Ine ndine Yehova Mulungu wako,+ amene ndinakutulutsa m’dziko la Iguputo, m’nyumba yaukapolo.+ 7 Usakhale ndi milungu ina iliyonse motsutsana ndi ine.+

8 “‘Usadzipangire fano+ kapena chifaniziro+ cha chinthu chilichonse chakumwamba, kapena chapadziko lapansi, kapenanso cha m’madzi a pansi pa dziko lapansi.* 9 Usaziweramire kapena kuzitumikira,+ chifukwa ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wofuna kuti anthu azidzipereka kwa ine ndekha,*+ wolanga ana, zidzukulu ndi ana a zidzukuluzo,* chifukwa cha zolakwa za anthu odana ndi ine.+ 10 Koma ndimasonyeza kukoma mtima kosatha ku mibadwo masauzande chifukwa cha anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.+

11 “‘Usagwiritse ntchito dzina la Yehova Mulungu wako mosasamala,+ pakuti Yehova sadzalekerera aliyense wogwiritsa ntchito dzina lake mosasamala osam’langa.+

12 “‘Posunga tsiku la sabata ndi kuliona kukhala lopatulika, mmene Yehova Mulungu wako anakulamulira,+ 13 uzigwira ntchito zako zonse masiku 6.+ 14 Koma tsiku la 7 ndi sabata la Yehova Mulungu wako.+ Usagwire ntchito iliyonse,+ iweyo kapena mwana wako wamwamuna, mwana wako wamkazi, kapolo wako wamwamuna, kapolo wako wamkazi, ng’ombe yako yamphongo, bulu wako, chiweto chako chilichonse, kapena mlendo wokhala mumzinda wanu,+ kuti nayenso kapolo wako wamwamuna ndi kapolo wako wamkazi, azipumula monga iwe.+ 15 Uzikumbukira kuti unali kapolo m’dziko la Iguputo+ ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasula.+ N’chifukwa chake Yehova Mulungu wako anakulamula kuti uzisunga tsiku la sabata.+

16 “‘Uzilemekeza bambo ako ndi mayi ako+ monga mmene Yehova Mulungu wako anakulamulira, kuti masiku ako atalike, ndi kuti zinthu zikuyendere bwino+ m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.

17 “‘Usaphe munthu.*+

18 “‘Usachite chigololo.+

19 “‘Usabe.+

20 “‘Usapereke umboni wonamizira mnzako.+

21 “‘Usalakelake mkazi wa mnzako.+ Usalakelake mwadyera nyumba ya mnzako, munda wake, kapolo wake wamwamuna, kapolo wake wamkazi, ng’ombe yake yamphongo, bulu wake, kapena chinthu chilichonse cha mnzako.’+

22 “Yehova analankhula Mawu* amenewa mokweza kumpingo wanu wonse, kuchokera pakati pa moto m’phiri,+ pamene kunachita mtambo wakuda ndi mdima wandiweyani, ndipo pa Mawuwo sanawonjezerepo kalikonse. Kenako anawalemba pamiyala iwiri yosema n’kundipatsa.+

23 “Ndiyeno mutangomva mawu amenewo kuchokera pamalo amdima, phiri likuyaka moto,+ munabwera kwa ine. Atsogoleri onse a mafuko anu ndi akulu anu onse anabwera kwa ine. 24 Pamenepo munati, ‘Yehova Mulungu wathu watisonyezatu ulemerero wake ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera pakati pa moto.+ Lero taona kuti Mulungu angalankhule ndi munthu, munthuyo n’kukhalabe ndi moyo.+ 25 Moto waukuluwu utipsereza.+ Tiferenji tsono? Tikapitiriza kumvetsera mawu a Yehova Mulungu wathu tifa basi.+ 26 Pakuti ndani mwa anthu onse amene anamvetserapo mawu a Mulungu wamoyo,+ akulankhula kuchokera pakati pa moto monga mmene tachitira ife n’kukhalabe ndi moyo? 27 Iweyo pita pafupi ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu adzanena. Iweyo ndiye udzatiuze zonse zimene Yehova Mulungu wathu adzakuuza,+ ndipo tidzamvera ndi kuchita zomwezo.’

28 “Motero Yehova anamva mawu anu onse amene munalankhula nane, ndipo Yehova anapitiriza kundiuza kuti, ‘Ndamva mawu amene anthu awa akuuza. Mawu onse amene akuuza ali bwino.+ 29 Zikanakhala bwino kwambiri akanakhala ndi mtima wondiopa+ ndi kusunga malamulo anga+ nthawi zonse, kuti iwo ndi ana awo zinthu ziwayendere bwino mpaka kalekale!*+ 30 Pita ukawauze kuti: “Bwererani kumahema anu.” 31 Koma iwe ima pompano, ndipo ndikuuza malamulo onse, malangizo ndi zigamulo zimene uyenera kuwaphunzitsa+ kuti azikazitsatira m’dziko limene ndikuwapatsa kukhala lawo.’ 32 Ndipo anthu inu muonetsetse kuti mukuchita monga mmene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani.+ Musatembenukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.+ 33 Muyende m’njira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulani,+ kuti mukhale ndi moyo ndi kuti zinthu zikuyendereni bwino+ ndiponso kuti mutalikitsedi masiku anu m’dziko limene mudzalitenga kukhala lanu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena