Numeri
25 Tsopano Aisiraeli anali kukhala ku Sitimu.+ Ali kumeneko, iwo anayamba kuchita chiwerewere ndi akazi a ku Mowabu.+ 2 Akaziwo ankabwera kudzaitana Aisiraeliwo kuti azipita nawo limodzi kokapereka nsembe kwa milungu yawo.+ Kumeneko, Aisiraeliwo ankadya ndi kugwadira milungu ya Amowabuwo.+ 3 Chotero Aisiraeli anayamba kupembedza nawo Baala wa ku Peori.+ Pamenepo, mkwiyo wa Yehova unawayakira.+ 4 Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: “Gwira onse amene akutsogolera anthuwo, uwaphe ndipo mitembo yawo uindandalike padzuwa pamaso pa Yehova.+ Uchite zimenezo kuti mkwiyo wa Yehova umene wayakira Aisiraeli uchoke.” 5 Chotero Mose anauza oweruza a mu Isiraeli+ kuti: “Aliyense wa inu aphe+ anthu ake amene akukapembedza nawo Baala wa ku Peori.”
6 Kenako anthuwo anangoona mwamuna wina wachiisiraeli+ akubwera ndi mkazi wachimidiyani.+ Anali kubwera naye kufupi ndi abale ake, pamaso pa Mose ndi pamaso pa khamu lonse la ana a Isiraeli. Pa nthawiyi n’kuti Aisiraeliwo akulira pakhomo la chihema chokumanako. 7 Koma Pinihasi+ mwana wa Eleazara, mdzukulu wa wansembe Aroni, ataona zimenezi nthawi yomweyo ananyamuka pakati pa khamulo n’kutenga mkondo waung’ono m’dzanja lake. 8 Iye anathamangira mwamuna wachiisiraeli uja mpaka kukalowa m’hema wake n’kubaya* awiriwo ndi mkondowo. Anabaya mwamuna wachiisiraeli limodzi ndi mkaziyo, mpaka mkondowo unakadutsa kumaliseche kwa mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa ana a Isiraeli.+ 9 Amene anaphedwa ndi mliriwo analipo 24,000.+
10 Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: 11 “Pinihasi+ mwana wa Eleazara, mdzukulu wa wansembe Aroni, wabweza mkwiyo wanga+ pa ana a Isiraeli, chifukwa sanalekerere konse zoti anthu azipikisana nane pakati pawo.+ Inetu ndikanawafafanizadi ana a Isiraeliwa, chifukwa ndimafuna kuti azikhala odzipereka kwa ine ndekha basi.+ 12 Pa chifukwa chimenechi, umuuze Pinihasi kuti, ‘Tsopano ndikupangana naye pangano la mtendere. 13 Likhale pangano la unsembe kwa iye ndi mbadwa zake mpaka kalekale,+ chifukwa sanalekerere zoti anthu azipikisana ndi Mulungu wake,+ ndiponso waphimba machimo a ana a Isiraeli.’”+
14 Dzina la mwamuna wachiisiraeli, amene anaphedwa limodzi ndi mkazi wachimidiyani uja, linali Zimiri mwana wa Salu. Saluyo anali mtsogoleri+ wa nyumba ya makolo a Asimiyoni. 15 Dzina la mkazi wachimidiyani amene anaphedwayo linali Kozibi, mwana wa Zuri.+ Zuri anali mtsogoleri wa fuko la nyumba ina ya makolo ku Midiyani.+
16 Pambuyo pake Yehova anauza Mose kuti: 17 “Amuna inu, athireni nkhondo Amidiyani, ndipo muwakanthe,+ 18 chifukwa akubweretserani tsoka mochenjera,+ pokukopani kuti muchimwe ku Peori.+ Muwakanthe ndithu, chifukwanso cha zochita za mlongo wawo Kozibi,+ mwana wa mtsogoleri wa ku Midiyani, amene anaphedwa+ pa tsiku limene mliri unakugwerani chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”+