1 Timoteyo
5 Usadzudzule mwamuna wachikulire mokalipa,+ koma umudandaulire ngati bambo ako. Amuna achinyamata uwadandaulire ngati abale ako, 2 ndipo akazi achikulire+ ngati amayi ako. Akazi achitsikana uwadandaulire ngati alongo ako,+ ndipo pochita zimenezi usakhale ndi maganizo alionse oipa.
3 Lemekeza akazi amasiye amene alidi amasiye.+ 4 Koma ngati mkazi wamasiye aliyense ali ndi ana kapena adzukulu, amenewo aphunzire kukhala odzipereka kwa Mulungu m’banja mwawo choyamba,+ mwa kubwezera kwa makolo+ ndi agogo awo zowayenerera, pakuti zimenezi zimakondweretsa Mulungu.+ 5 Mkazi amene alidi wamasiye, amene akusowa womusamala,+ amadalira Mulungu+ ndipo amalimbikira mapembedzero ndi mapemphero usiku ndi usana.+ 6 Koma amene amatsatira zilakolako zake kuti azikhutiritse,+ ndi wakufa+ ngakhale kuti ali ndi moyo. 7 Choncho, uziwapatsa malamulo amenewa+ nthawi zonse kuti asakhale ndi chifukwa chowanenezera.+ 8 Ndithudi, ngati munthu sasamalira anthu amene ndi udindo wake kuwasamalira,+ makamaka a m’banja lake,+ wakana+ chikhulupiriro+ ndipo ndi woipa kuposa munthu wosakhulupirira.
9 Mkazi wamasiye wolembedwa pamndandanda wa akazi amasiye, akhale wazaka zoposa 60. Akhale amene anali wokhulupirika kwa mwamuna wake,*+ 10 wodziwika kuti anachita ntchito zabwino,+ analera bwino ana,+ anali kuchereza alendo,+ anasambitsa mapazi a oyera,+ anathandiza ena m’masautso,+ ndiponso anali kugwira mwakhama ntchito iliyonse yabwino.+
11 Koma usalole kuika akazi amasiye achitsikana pamndandanda umenewu, pakuti chilakolako chawo chofuna mwamuna chikaima pakati pa iwo ndi Khristu,+ amafuna kukwatiwa. 12 Zikatero, amapezeka olakwa chifukwa sanasunge chikhulupiriro chimene anasonyeza poyamba.+ 13 Komanso pa nthawi yomweyo, amayamba chizolowezi chomangokhala osachita kanthu, n’kumangoyendayenda m’makomo mwa anzawo. Kuwonjezera pa kumangokhala osachita kanthu, amakhalanso amiseche ndi olowerera nkhani za eni,+ n’kumalankhula zimene sayenera kulankhula. 14 Choncho ndimafuna kuti akazi amasiye achitsikana azikwatiwa,+ azibereka ana,+ ndi kusamalira banja, kuti wotsutsa asapeze chifukwa chonenera zachipongwe.+ 15 Ndipotu ena apatutsidwa kale moti ayamba kutsatira Satana. 16 Ngati mkazi aliyense wokhulupirira ali ndi achibale amene ndi akazi amasiye, aziwathandiza,+ kuti akazi amasiyewo asakhale cholemetsa ku mpingo. Zikatero, mpingowo ungathe kuthandiza amene alidi akazi amasiye.+
17 Akulu otsogolera+ bwino apatsidwe ulemu waukulu,+ makamaka amene amachita khama kulankhula ndi kuphunzitsa.+ 18 Pakuti lemba limati: “Usamange ng’ombe pakamwa pamene ikupuntha mbewu.”+ Komanso limati: “Wantchito ayenera kulandira malipiro ake.”+ 19 Usavomereze mlandu woneneza mkulu, kupatulapo ngati pali umboni wa mboni ziwiri kapena zitatu.+ 20 Anthu amene ali ndi chizolowezi chochita tchimo,+ uwadzudzule+ pamaso pa onse kuti ena onse akhale ndi mantha.+ 21 Ndikukulamula mwamphamvu, pamaso pa Mulungu ndi Khristu Yesu+ ndiponso angelo ochita kusankhidwa, kuti uzitsatira malangizo amenewa popanda kuweruziratu. Usachite kanthu ndi maganizo okondera.+
22 Usafulumire kuika munthu aliyense pa udindo,*+ kapena kugawana ndi anthu ena machimo awo.+ Pitiriza kukhala ndi khalidwe loyera.+
23 Usamangomwa madzi okha, koma uzimwanso vinyo pang’ono,+ chifukwa cha vuto lako la m’mimba ndi kudwaladwala kwako kuja.
24 Machimo a anthu ena amaonekera poyera,+ ndipo zimenezi zimachititsa kuti aweruzidwe. Koma anthu ena, machimo awo amadzaonekera pambuyo pake.+ 25 Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera,+ ndipo ngakhale kuti zisaonekere sizingabisike mpaka kalekale.+